< 2 Mbiri 24 >

1 Yowasi anali wa zaka zisanu ndi ziwiri pamene anakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka makumi anayi. Dzina la amayi ake linali Zibiya wa ku Beeriseba.
Joas avait sept ans lorsqu'il devint roi, et il régna quarante ans à Jérusalem. Sa mère s'appelait Sébia, de Bersabée.
2 Yowasi anachita zolungama pamaso pa Yehova nthawi yonse ya moyo wa wansembe Yehoyada.
Joas fit ce qui est droit aux yeux de Yahweh pendant toute la vie du prêtre Joïada.
3 Yehoyada anamupezera iye akazi awiri, ndipo anabereka ana aamuna ndi aakazi.
Joïada prit deux femmes pour Joas, qui engendra des fils et des filles.
4 Patapita nthawi Yowasi anatsimikiza zokonzanso Nyumba ya Yehova.
Après cela, Joas eut à cœur de restaurer la maison de Yahweh.
5 Iye anayitanitsa pamodzi ansembe ndi Alevi ndipo anawawuza kuti, “Pitani ku mizinda ya Yuda ndi kukasonkhetsa ndalama za pa chaka kwa Aisraeli onse zokonzera Nyumba ya Mulungu wanu. Chitani zimenezi tsopano.” Koma Alevi sanachite zimenezi mwachangu.
Il assembla les prêtres et les lévites et leur dit: " Allez dans les villes de Juda, et vous recueillerez parmi tout Israël de l'argent, chaque année, pour réparer la maison de votre Dieu, et faites cela avec hâte. " Mais les lévites ne se hâtèrent point.
6 Choncho mfumu inayitanitsa Yehoyada, mkulu wa ansembe ndipo inati kwa iye, “Kodi nʼchifukwa chiyani simunawuze Alevi kuti asonkhetse ndalama ku Yuda ndi Yerusalemu, msonkho umene anakhazikitsa Mose mtumiki wa Yehova ndiponso gulu lonse la Aisraeli mu tenti yaumboni?”
Le roi appela Joïada, le grand prêtre, et lui dit: " Pourquoi n'as-tu pas veillé sur les lévites pour qu'ils apportent de Juda et de Jérusalem la taxe imposée à Israël par Moïse, serviteur de Yahweh, et par l'assemblée, pour la tente du témoignage?
7 Ana a mkazi woyipa, Ataliya, anathyola chitseko cha Nyumba ya Mulungu ndipo anagwiritsa ntchito zinthu zopatulika popembedza Baala.
Car l'impie Athalie et ses fils ont ravagé la maison de Dieu, et ils ont fait servir pour les Baals toutes les choses consacrées à la maison de Yahweh. "
8 Mfumu italamulira, bokosi linapangidwa ndipo linayikidwa panja pa chipata cha Nyumba ya Yehova.
Alors le roi ordonna qu'on fit un coffre et qu'on le plaçât à la porte de la maison de Yahweh, en dehors.
9 Ndipo analengeza kwa anthu a mu Yuda ndi mu Yerusalemu kuti abweretse kwa Yehova msonkho umene Mose mtumiki wa Mulungu analamulira Aisraeli mʼchipululu.
Et l'on publia dans Juda et dans Jérusalem que chacun eût à apporter à Yahweh la taxe imposée dans le désert à Israël par Moïse, serviteur de Yahweh.
10 Akuluakulu onse ndi anthu onse anabweretsa zopereka zawo mokondwera ndipo anaziponya mʼbokosi mpaka linadzaza.
Tous les chefs et tout le peuple en eurent de la joie, et ils apportèrent et jetèrent dans le coffre tout ce qu'ils devaient payer.
11 Nthawi ina iliyonse imene Alevi abweretsa bokosilo kwa akuluakulu a mfumu ndipo akaona kuti muli ndalama zambiri, mlembi waufumu ndi nduna yayikulu ya mkulu wa ansembe amabwera ndi kuchotsa ndalama mʼbokosi muja ndipo amalitenga kukaliyika pamalo pake. Iwo amachita izi nthawi ndi nthawi ndipo anapeza ndalama zambiri.
Le temps venu de livrer le coffre aux inspecteurs du roi par l'intermédiaire des lévites, lorsque ceux-ci voyaient qu'il y avait beaucoup d'argent dans le coffre, le secrétaire du roi et le commissaire du grand prêtre venaient vider le coffre; ils le prenaient et le remettaient à sa place. Ainsi faisaient-ils chaque fois, et ils recueillaient de l'argent en abondance.
12 Mfumu pamodzi ndi Yehoyada anapereka ndalamazo kwa anthu oyangʼanira ntchito ku Nyumba ya Yehova. Analemba ntchito amisiri a miyala ndi a matabwa kuti akonzenso Nyumba ya Yehova. Analembanso ntchito amisiri a zitsulo ndi mkuwa kuti akonze Nyumba ya Mulungu.
Le roi et Joïada le donnaient à ceux qui faisaient exécuter l'ouvrage de la maison de Yahweh, et ceux-ci prenaient à gage des tailleurs de pierres et des charpentiers pour restaurer la maison de Yahweh, ainsi que des artisans en fer et en airain pour consolider la maison de Yahweh.
13 Anthu amene ankagwira ntchito anali odziwa bwino, ndipo ntchitoyo inagwiridwa bwino ndi manja awo. Iwo anamanganso Nyumba ya Mulungu motsatira mapangidwe ake oyamba ndipo anayilimbitsa.
Les ouvriers travaillèrent, et la restauration progressa en leurs mains; ils rétablirent la maison de Dieu en son état ancien et l'affermirent.
14 Atamaliza, iwo anabweretsa ndalama zotsala kwa mfumu ndi Yehoyada, ndipo anazigwiritsira ntchito popangira zida za mʼNyumba ya Yehova: ziwiya zogwiritsa ntchito potumikira ndi popereka nsembe zopsereza, komanso mbale ndi ziwiya zagolide ndi siliva. Nthawi yonse ya moyo wa Yehoyada, nsembe zopsereza zinkaperekedwa mosalekeza mʼNyumba ya Yehova.
Quand ils eurent fini, ils apportèrent devant le roi et devant Joïada l'argent qui restait, et l'on en fit des ustensiles pour la maison de Yahweh, des ustensiles pour le service et pour les holocaustes, des coupes et d'autres ustensiles d'or et d'argent. Et l'on offrit continuellement des holocaustes dans la maison de Yahweh pendant toute la vie de Joïada.
15 Tsono Yehoyada anakalamba ndipo anali ndi zaka zambiri. Pambuyo pake iye anamwalira ali ndi zaka 130.
Joïada devint vieux et rassasié de jours, et il mourut; il avait cent trente ans quand il mourut.
16 Iyeyo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi mafumu mu mzinda wa Davide chifukwa cha zabwino zimene anachita mu Israeli, kuchitira Mulungu ndi Nyumba yake.
On l'enterra dans la ville de David avec les rois, parce qu'il avait fait du bien en Israël et à l'égard de Dieu et de sa maison.
17 Atamwalira Yehoyada, akuluakulu a Yuda anabwera kudzapereka ulemu kwa mfumu, ndipo mfumu inawamvera.
Après la mort de Joïada, les chefs de Juda vinrent se prosterner devant le roi; alors le roi les écouta.
18 Iwo anasiya Nyumba ya Yehova, Mulungu wa makolo awo ndipo anapembedza Asera ndi mafano. Chifukwa cha kulakwa kwawo, mkwiyo wa Yehova unabwera pa Yuda ndi Yerusalemu.
Et, abandonnant la maison de Yahweh, le Dieu de leurs pères, ils honorèrent les aschérahs et les idoles. La colère de Yahweh vint sur Juda et sur Jérusalem, à cause de cette prévarication.
19 Ngakhale Yehova anatumiza aneneri kwa anthuwo kuti awabweze kwa Iye, ngakhale aneneri ananenera mowatsutsa, anthuwo sanamvere.
Pour les faire revenir vers lui, Yahweh envoya parmi eux des prophètes qui rendirent témoignage contre eux, mais ils ne les écoutèrent pas.
20 Kenaka Mzimu wa Mulungu unabwera pa Zekariya mwana wa wansembe Yehoyada. Iye anayimirira pamaso pa anthu ndipo anati, “Zimene Mulungu akunena ndi Izi: ‘Chifukwa chiyani simukumvera Malamulo a Yehova? Simudzapindula. Chifukwa mwasiya Yehova, Iyenso wakusiyani.’”
L'esprit de Dieu revêtit Zacharie, fils du prêtre Joïada, qui se présenta devant le peuple et lui dit: " Ainsi dit Dieu: Pourquoi transgressez-vous les commandements de Yahweh, pour ne point prospérer? Parce que vous avez abandonné Yahweh, il vous abandonne à son tour. "
21 Koma anthuwo anamuchitira chiwembu molamulidwa ndi mfumu ndipo anamugenda miyala ndi kumupha mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu.
Et ils conspirèrent contre lui, et ils le lapidèrent par ordre du roi, dans le parvis de la maison de Yahweh.
22 Mfumu Yowasi sinakumbukire zabwino zimene Yehoyada abambo ake a Zekariya anamuchitira, koma anapha mwana wake. Pamene amafa, iye ananena kuti, “Yehova aone zimenezi ndipo abwezere chilango.”
Joas ne se souvint pas de l'affection qu'avait eue pour lui Joïada, père de Zacharie, et il fit périr son fils. Zacharie dit en mourant: " Que Yahweh voie et fasse justice! "
23 Pakutha kwa chaka, gulu lankhondo la Aramu linadzamenyana ndi Yowasi. Linalowa mu Yuda ndi mu Yerusalemu ndi kupha atsogoleri onse a anthu. Zonse zimene analanda anazitumiza kwa mfumu ya ku Damasiko.
Au retour de l'année, l'armée des Syriens monta contre Joas et vint en Juda et à Jérusalem. Ils tuèrent parmi le peuple tous les chefs du peuple, et ils envoyèrent tout leur butin au roi de Damas.
24 Ngakhale kuti gulu lankhondo la Aramu linabwera ndi anthu ochepa okha, Yehova anapereka mʼmanja mwawo gulu lalikulu lankhondo. Chifukwa Yuda anasiya Yehova Mulungu wa makolo awo, chiweruzo chinachitika pa Yowasi.
L'armée des Syriens était venue avec un petit nombre d'hommes, et Yahweh livra entre leurs mains une armée considérable, parce qu'ils avaient abandonné Yahweh, le Dieu de leurs pères. Les Syriens exécutèrent le jugement contre Joas.
25 Pamene Aaramu amachoka, anasiya Yowasi atavulazidwa kwambiri. Akuluakulu ake anamuchitira chiwembu chifukwa anapha mwana wa wansembe Yehoyada, ndipo anamupha ali pa bedi pake. Choncho anafa ndipo anayikidwa mʼmanda mu mzinda wa Davide, koma osati manda a mafumu.
Lorsqu'ils se furent éloignés de lui, l'ayant laissé couvert de nombreuses blessures, ses serviteurs conspirèrent contre lui, à cause du sang des fils du prêtre Joïada; ils le tuèrent sur son lit, et il mourut. On l'enterra dans la ville de David, mais on ne l'enterra pas dans les sépulcres des rois.
26 Iwo amene anamuchitira chiwembu anali Zabadi mwana wa Simeati, mkazi wa ku Amoni, ndi Yehozabadi mwana wa Simiriti, mkazi wa ku Mowabu.
Voici ceux qui conspirèrent contre lui: Zabad, fils de Semmaath, femme Ammonite, et Jozabad, fils de Samarith, femme Moabite.
27 Za ana ake aamuna, uneneri wonena za iye, mbiri ya kumanganso Nyumba ya Mulungu, zalembedwa mʼbuku lofotokoza za mafumu. Ndipo Amaziya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
Ce qui concerne ses fils, le grand nombre de prophéties dirigées contre lui et la restauration de la maison de Dieu, voici que cela est écrit dans les Mémoires sur le livre des Rois. Amasias, son fils, régna à sa place.

< 2 Mbiri 24 >