< 2 Petro 3 >

1 Inu okondedwa, iyi ndi kalata yanga yachiwiri kwa inu. Ine ndalemba makalata onse awiri kuti ndikukumbutseni ndi kukutsitsimutsani ndi cholinga choti muzilingalira moyenera.
Mis queridos hermanos, esta es ahora mi segunda carta para ustedes, y en esta como en la primera, estoy tratando de hacerlos pensar rectamente y mantener sus mentes alertas con mis consejos;
2 Ndikufuna kuti mukumbukire mawu amene anayankhulidwa kale ndi aneneri oyera mtima ndiponso lamulo limene Ambuye ndi Mpulumutsi wathu analipereka kudzera mwa atumwi.
Para que tengan en cuenta las palabras de los santos profetas del pasado, y la ley del Señor y Salvador que les fueron dados por sus apóstoles.
3 Poyamba mudziwe kuti mʼmasiku otsiriza kudzafika anthu onyoza, adzanyoza ndi kutsata zilakolako zawo zoyipa.
Teniendo primero de todo el conocimiento de que en los últimos días habrá hombres que, gobernados por sus malos deseos, se burlaran de las cosas santas,
4 Iwo adzati, “Kodi suja Ambuye analonjeza kuti adzabweranso? Nanga ali kuti? Lija nʼkale anamwalira makolo athu, koma zinthu zonse zili monga anazilengera poyamba paja.”
Diciendo: ¿Dónde está la promesa de su venida? Porque desde él día que los padres durmieron hasta ahora, todo ha continuado como fue desde la creación del mundo.
5 Koma iwo akuyiwala dala kuti Mulungu atanena mawu, kumwamba kunakhalapo ndipo analenga dziko lapansi ndi madzi.
Pero al tomar este punto de vista, olvidaron la memoria de que en los viejos tiempos había un cielo y una tierra levantada del agua y rodeada de agua y que por el agua subsiste;
6 Ndi madzinso achigumula, dziko lapansi la masiku amenewo linawonongedwa.
Y que el mundo que entonces llegó a su fin por el desbordamiento de las aguas.
7 Dziko la kumwamba ndi lapansi la masiku ano akulisunga ndi mawu omwewo kuti adzalitentha ndi moto. Akuzisunga mpaka tsiku limene adzaweruza ndi kuwononga anthu onse osapembedza Mulungu.
Pero el presente cielo y la tierra han sido guardados para destrucción por el fuego, por la misma palabra, Ese fuego los quemará en él día del juicio y de la perdición de los malvados.
8 Koma abale okondedwa, musayiwale chinthu chimodzi ichi: Kuti pamaso pa Ambuye tsiku limodzi lili ngati zaka 1,000, ndipo zaka 1,000 zili ngati tsiku limodzi!
Pero, mis queridos hermanos, tengan en cuenta esta única cosa, que con el Señor un día es lo mismo que mil años, y mil años no son más que un día.
9 Ambuye sazengereza kuchita zimene analonjeza, monga ena amaganizira. Iwo akukulezerani mtima, sakufuna kuti aliyense awonongeke, koma akufuna kuti aliyense alape.
El Señor no tarda en cumplir su palabra, como a algunos les parece, sino que es paciente con nosotros, no deseando la destrucción de ninguno, sino que todos se aparten de sus malos caminos.
10 Koma tsiku la Ambuye lidzafika ngati mbala. Pa tsikuli zinthu zakumwamba zidzachoka ndi phokoso lalikulu. Zinthu zonse zidzawonongedwa ndi moto, ndipo dziko lapansi ndi zonse zili mʼmenemo zidzapsa.
Pero el día del Señor vendrá como un ladrón; y en ese día los cielos se envolverán con un gran ruido, y la sustancia de la tierra será cambiada por el calor violento, y el mundo y todo lo que hay en él se consumirá.
11 Popeza kuti zinthu zonse zidzawonongedwa motere, kodi inu muyenera kukhala anthu otani? Muyenera kukhala moyo wachiyero ndi opembedza Mulungu
Viendo que todas estas cosas están llegando a ese fin, ¿con cuánta devoción y santidad deben andar ustedes, en toda conducta santa y justicia,
12 pamene mukuyembekezera tsiku la Mulungu ndi kufulumiza kufika kwake. Pa tsiku limeneli zinthu zakumwamba zidzawonongedwa ndi moto, ndipo zidzasungunuka ndi kutentha.
Buscando y verdaderamente deseando la venida del día de Dios, cuando los cielos llegará a su fin a través del fuego, y la sustancia de la tierra será cambiada por el gran calor?
13 Koma ife tikudikira kumwamba kwatsopano ndi dziko lapansi latsopano, zimene Mulungu analonjeza, mʼmene chilungamo chidzakhalamo.
Pero teniendo fe en su palabra, estamos buscando un cielo nuevo y una tierra nueva, que será el lugar donde mora la justicia.
14 Chomwecho okondedwa, popeza inu mukudikira zimenezi, chitani changu kuti mukhale wopanda chilema kuti mukhale pa mtendere ndi Iye.
Por esta razón, mis queridos hermanos, como ustedes están buscando estas cosas, tengan mucho cuidado de que cuando él venga puedan estar en paz delante de él, libre del pecado y de todo mal.
15 Zindikirani kuti kuleza mtima kwa Ambuye kukutanthauza chipulumutso, monga momwe mʼbale wathu wokondedwa Paulo anakulemberaninso ndi nzeru zimene Mulungu anamupatsa.
Y tengan entendido que la paciencia del Señor es para la salvación; tal como nuestro hermano Pablo lo dijo en sus cartas, por la sabiduría que le fue dada;
16 Iye walemba chimodzimodzi makalata ake onse, kuyankhula za zinthu izi. Mʼmakalata ake mumakhala zinthu zina zovuta kuzimvetsa, zimene anthu osadziwa ndi osakhazikika amazipotoza, monga amachita ndi malemba ena onse, potero akudziwononga okha.
Y como dijo en todas sus cartas, que tenía que ver con estas cosas; en el cual hay algunos dichos duros, de modo que, como el resto de las Sagradas Escrituras, son torcidos por aquellos que son inciertos y sin conocimiento, para la destrucción de sus almas.
17 Nʼchifukwa chake, abale okondedwa, popeza mukuzidziwa kale zimenezi, chenjerani kuti musatengeke ndi zolakwa za anthu osaweruzika, mungagwe ndi kuchoka pamalo otetezedwa.
Por esta razón, mis seres queridos, teniendo conocimiento de estas cosas antes de que ocurran, tengan cuidado de no ser arrastrados por el error de los inicuos, cayendo así de su verdadera fe.
18 Koma kulani mu chisomo ndi mʼchidziwitso cha Ambuye ndi Mpulumutsi wathu Yesu Khristu. Kwa Iye kukhale ulemerero tsopano mpaka muyaya. Ameni. (aiōn g165)
Más bien, crezcan en la gracia y en el conocimiento de nuestro Señor y Salvador Jesucristo. Que él tenga la gloria ahora y para siempre. Que así sea. (aiōn g165)

< 2 Petro 3 >

The World is Destroyed by Water
The World is Destroyed by Water