< Deuteronomo 27 >

1 Mose ndi akuluakulu a Israeli analamula anthu kuti, “Sungani malamulo onse amene ndikukupatsani lero lino.
Then Moses and the elders of Israel instructed the people, saying: “Keep each commandment that I instruct to you this day.
2 Mukawoloka mtsinje wa Yorodani kulowa mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani, muyimiritse miyala ingapo ikuluikulu ndi kuyikulungiza.
And when you have crossed over the Jordan, into the land which the Lord your God will give to you, you shall erect immense stones, and you shall coat them with plaster,
3 Mulembepo mawu onse a malamulo amenewa pamene muwoloka kulowa mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani, dziko loyenda mkaka ndi uchi, monga momwe Yehova Mulungu wa makolo anu anakulonjezerani.
so that you may be able to write upon them all the words of this law, when you have crossed the Jordan so as to enter into the land which the Lord your God will give to you, a land flowing with milk and honey, just as he swore to your fathers.
4 Ndipo mukawoloka Yorodani muyimike miyala iyi pa Phiri la Ebala monga momwe ndikukulamulirani lero lino ndipo muyikulungize.
Therefore, when you have crossed over the Jordan, erect the stones, just as I instruct you to do this day, on Mount Ebal. And you shall coat them with plaster,
5 Pamenepo mumange guwa lansembe la miyala la Yehova Mulungu wanu. Musagwiritse ntchito chida chilichonse chachitsulo pa miyalapo.
and you shall build, in that place, an altar to the Lord your God out of stones which have not been touched by iron,
6 Mumange guwa lansembe la Yehova Mulungu wanu ndi miyala yakutchire ndi kuperekerapo nsembe yopsereza kwa Yehova Mulungu wanu.
out of stones which have not been hewn or polished. And you shall offer holocausts on it to the Lord your God.
7 Muperekerepo nsembe zopereka za chiyanjano, muzidye ndi kukondwera pamaso pa Yehova Mulungu wanu.
And you shall immolate peace victims. And you shall eat and feast in that place, in the sight of the Lord your God.
8 Ndipo pa miyalapo mudzalembepo mawu onse a malamulo ndi malemba akuluakulu.”
And you shall write upon the stones all the words of this law, plainly and clearly.”
9 Kenaka Mose ndi ansembe, amene ndi Alevi anati kwa Aisraeli onse, “Khalani chete Aisraeli inu ndipo mumvetsere! Tsopano inu ndinu anthu a Yehova Mulungu wanu.
And Moses and the priests of Levitical stock said to all of Israel: “Attend and listen, O Israel! Today you have become the people of the Lord your God.
10 Muzimvera Yehova Mulungu wanu ndi kutsata malamulo ake ndi malangizo ake omwe ndikukupatsani lero lino.”
You shall listen to his voice, and you shall do the commandments and justices, which I am entrusting to you.”
11 Tsiku lomwelo Mose analamula anthu kuti:
And Moses instructed the people in that day, saying:
12 Mukawoloka Yorodani, mafuko awa akayimirire pa Phiri la Gerizimu ndi kudalitsa anthu: Simeoni, Levi, Yuda, Isakara, Yosefe ndi Benjamini.
“These shall stand upon Mount Gerizim, as a blessing to the people, when you will have crossed the Jordan: Simeon, Levi, Judah, Issachar, Joseph, and Benjamin.
13 Ndipo mafuko awa akayimirire pa Phiri la Ebala ndi kutchula matemberero: Rubeni, Gadi, Aseri, Zebuloni, Dani ndi Nafutali.
And in the opposite region, there shall stand upon Mount Ebal, as a curse: Reuben, Gad, and Asher, and Zebulun, Dan, and Naphtali.
14 Alevi adzayankhula mokweza kwa Aisraeli onse kuti:
And the Levites shall pronounce and declare to all the men of Israel, with an exalted voice:
15 “Ndi wotembereredwa munthu amene asema chifanizo kapena kupanga fano, ndi kuchiyika mobisa, pakuti chimenechi ndi chinthu chodetsedwa pamaso pa Yehova, ntchito za manja a anthu.”
Cursed be the man who makes a graven or molten idol, an abomination to the Lord, a work of the hands of its maker, and who puts it in a secret place. And all the people shall respond by saying: Amen.
16 “Ndi wotembereredwa munthu amene sachitira ulemu abambo ake kapena amayi ake.”
Cursed be he who does not honor his father and mother. And all the people shall say: Amen.
17 “Ndi wotembereredwa munthu amene amasuntha mwala wa malire wa mnzake.”
Cursed be he who removes his neighbor’s landmarks. And all the people shall say: Amen.
18 “Ndi wotembereredwa munthu amene amasocheretsa munthu wosaona pa msewu.”
Cursed be he who causes the blind to go astray on a journey. And all the people shall say: Amen.
19 “Ndi wotembereredwa munthu amene sachitira chilungamo mlendo, ana amasiye kapena mkazi wamasiye.”
Cursed be he who subverts the judgment of the new arrival, the orphan, or the widow. And all the people shall say: Amen.
20 “Ndi wotembereredwa munthu amene agonana ndi mkazi wa abambo ake pakuti iye sachitira ulemu pogona pa abambo ake.”
Cursed be he who lies with his father’s wife, and so exposes the covering of his bed. And all the people shall say: Amen.
21 “Ndi wotembereredwa munthu amene achita chigololo ndi nyama ya mtundu uli wonse.”
Cursed be he who lies with any beast. And all the people shall say: Amen.
22 “Ndi wotembereredwa munthu amene agonana ndi mlongo wake, mwana wamkazi wa abambo ake kapena mwana wamkazi wa amayi ake.”
Cursed be he who lies with his sister, the daughter of his father, or of his mother. And all the people shall say: Amen.
23 “Ndi wotembereredwa munthu amene agonana ndi apongozi ake.”
Cursed be he who lies with his mother-in-law. And all the people shall say: Amen.
24 “Ndi wotembereredwa munthu amene apha mnzake mwachinsinsi.”
Cursed be he who secretly strikes down his neighbor. And all the people shall say: Amen.
25 “Ndi wotembereredwa munthu amene alandira chiphuphu kuti aphe munthu wosalakwa.”
Cursed be he who accepts gifts in order to strike down the life of innocent blood. And all the people shall say: Amen.
26 “Ndi wotembereredwa aliyense amene sachita kapena sasunga mawu a malamulo awa.”
Cursed be he who does not remain in the words of this law, and does not carry them out in deed. And all the people shall say: Amen.”

< Deuteronomo 27 >