< Ezekieli 16 >

1 Yehova anayankhula nane kuti,
RAB bana şöyle seslendi:
2 “Iwe mwana wa munthu, udzudzule Yerusalemu za ntchito zake zonyansa.
“İnsanoğlu, Yeruşalim'e yaptığı iğrenç uygulamaları bildir.
3 Umuwuze kuti, ‘Ambuye Yehova akukuwuza, iwe Yerusalemu kuti: Kwawo kwa makolo ako ndi ku Kanaani ndipo iwe unabadwira komweko. Abambo ako anali Mwamori, amayi ako anali Mhiti.
De ki, ‘Egemen RAB Yeruşalim'e şöyle diyor: Kökenin ve doğumun açısından Kenan ülkesindensin; baban Amorlu, annense Hititli'ydi.
4 Pa tsiku lomwe unabadwa sanadule mchombo wako. Sanakusambitse mʼmadzi kuti uyere. Sanakuthire mchere kapena kukukulunga mʼnsalu.
Doğduğun gün göbek bağın kesilmedi, temizlemek için seni yıkamadılar, tuzla ovalamadılar, kundağa sarmadılar.
5 Palibe ndi mmodzi yemwe anakusamala kapena kukumvera chisoni kuti akuchitire zimenezi. Mʼmalo mwake anakutaya panja poyera, chifukwa ananyansidwa nawe pa tsiku lako lobadwa.
Kimse bunlardan birini yapacak kadar sana acımadı, sevecenlik göstermedi. Senden tiksindikleri için doğduğun gün seni kıra attılar.
6 “‘Tsono pamene ndinkadutsa, ndinakuona ukuvimvinizika mʼmagazi ako. Ndinakuyankhula uli mʼmagazi ako omwewo kuti, ‘Khala ndi moyo,’
“‘Yanından geçtim, senin kendi kanının içinde kımıldadığını gördüm. Kendi kanının içindeyken yaşa! dedim. Evet, Kendi kanının içindeyken yaşa! dedim.
7 ndi kuti ukule ngati mbewu ya mʼmunda. Iwe unakula ndipo unatalika ndi kutha msinkhu. Mawere ako anayamba kumera ndi tsitsi lakonso linayamba kutalika. Komabe unali wamaliseche ndi wausiwa.
Kırda yetişen bir bitki gibi seni geliştirdim. Geliştin, büyüdün, kusursuz bir güzelliğe eriştin. Göğüslerin oluştu, saçların uzadı. Ama çırılçıplaktın.
8 “‘Tsono pamene ndinkadutsanso ndinaona kuti nthawi yako yomanga banja inakwana. Tsono ndinakufunditsa chovala changa ndi kubisa umaliseche wako. Ndinachita nawe pangano la ukwati ndipo unakhala wanga, akutero Ambuye Wamphamvuzonse.
“‘Yine yanından geçtim, sana baktım, sevgi çağındı. Giysimin eteğini üzerine serdim, çıplaklığını örttüm. Sana ant içtim, seninle antlaşma yaptım. Egemen RAB böyle diyor. Ve benim oldun.
9 “‘Ine ndinakusambitsa mʼmadzi kutsuka magazi ako ndikukudzoza mafuta.
“‘Seni yıkadım, üzerindeki kanı temizledim, derine zeytinyağı sürdüm.
10 Ndinakuveka zovala zopetapeta ndi nsapato za chikopa. Ndinakuveka zovala zabafuta ndi kukuveka zovala za bafuta.
Sana işlemeli giysiler giydirdim, deriden çarık verdim. Beline ince keten kuşak bağladım, seni pahalı giysilerle örttüm,
11 Ndinakukongoletsa ndi zokometsera zamtengowapatali: ndinakuveka zibangiri mʼmanja mwako ndi mkanda mʼkhosi mwako,
takılarla süsledim. Bileklerine bilezikler, boynuna gerdanlık taktım.
12 ndipo ndinakuveka chipini pa mphuno yako, ndolo ku makutu ako ndiponso chipewa chaufumu pa mutu wako.
Burnuna halka, kulaklarına küpeler, başına görkemli bir taç taktım.
13 Choncho unavala zokongoletsa zagolide ndi siliva. Zovala zako zinali zabafuta, zasilika ndi za nsalu zopetapeta. Chakudya chako chinali ufa wosalala uchi ndi mafuta a olivi. Motero unakhala wokongola kwambiri ndipo unasanduka mfumukazi.
Altınla gümüşle süslendin; giysilerin ince ketenden, pahalı, işlemeli kumaştandı. İnce unla, balla, zeytinyağıyla beslendin. Gitgide güzelleştin, krallığa yaraştın.
14 Ndipo mbiri ya kukongola kwako inawanda pakati pa anthu a mitundu ina, chifukwa ulemerero umene ndinakupatsa unapititsa patsogolo kukongola kwako, akutero Ambuye Yehova.
Güzelliğinden ötürü ünün uluslar arasında yayıldı. Çünkü seni görkemimle donattığım için güzelliğin kusursuzdu. Egemen RAB böyle diyor.
15 “‘Koma iwe unatama kukongola kwako ndipo unayamba kuchita zadama chifukwa cha kutchuka kwako. Unkachita chigololo ndi kumangodzipereka kwa aliyense wodutsa ndipo kukongola kwako kunakhala kwake.
“‘Ama sen güzelliğine güvendin, ününü kullanarak fahişelik ettin. Her geçene gönlünü kaptırdın, kendini teslim ettin.
16 Unatenga zovala zako zina nukakongoletsera malo opembedzerako mafano, ndipo kumeneko umachitirako zigololo. Zinthu izi sizinachitikepo nʼkale lomwe ndipo sizidzachitikanso.
Giysilerinden alıp kendine süslü tapınma yerleri yaptın, oralarda fahişelik ettin. Böylesi ne olmuştur, ne de olacaktır.
17 Unatenga zokongoletsera zopangidwa ndi golide ndi siliva zimene ndinakupatsa ndipo unadzipangira wekha mafano aamuna amene unkachita nawo za dama.
Sana verdiğim altın, gümüş süslerden erkek suretleri yaptın, onlarla fahişelik ettin.
18 Ndipo iwe unatenga zovala zako zopetapeta ndi kuveka mafano. Mafuta anga ndi lubani wanga unapereka kwa mafanowo.
İşlemeli giysilerini alıp onların üzerine örttün. Onlara zeytinyağımı, buhurumu sundun.
19 Chakudya chimene ndinakupatsa, ufa, mafuta ndi uchi, zimene ndinkakudyetsa nazo unazitenga nʼkuzipereka kwa mafanowo ngati nsembe ya fungo lokoma. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
Yemen için sağladığım yiyeceği –ince unu, zeytinyağını, balı– güzel kokulu bir sunu olarak onlara sundun. Böyle yaptın diyor Egemen RAB.
20 “‘Ndipo unatenga ana ako aamuna ndi ana aakazi amene unandibalira ine, ndipo unakawapereka ngati nsembe kwa mafanowo. Kodi zigololo zakozo sizinakukwanire
“‘Bana doğurduğun oğulları, kızları alıp yiyecek olarak putlara kurban ettin. Fahişelik etmen yetmiyormuş gibi,
21 kuti uziphanso ana anga ndi kuwapereka ngati nsembe kwa mafano akowo?
çocuklarımı kesip sunu olarak ateşte putlara kurban ettin.
22 Chifukwa cha zadama zako zonyansazi unayiwala masiku a ubwana wako pamene unali wamaliseche, wausiwa ndiponso womangovivinizika mʼmagazi.
Bütün iğrenç uygulamalarını, fahişeliklerini yaparken gençlik günlerini, çırılçıplak olduğun, kanının içinde kımıldandığın zamanı anımsamadın.
23 “‘Tsoka! Tsoka kwa iwe, akutero Ambuye Yehova chifukwa powonjezera pa zoyipa zako zonse,
“‘Egemen RAB, vay, vay başına diyor! Yaptığın kötülüklere ek olarak,
24 wadzimangira wekha nsanja ndi guwa pa mabwalo onse.
kendine fuhuş yuvaları kurdun, bütün meydanlarda yüksek tapınma yerleri yaptın.
25 Pa msewu uliwonse wamanga nsanjazo. Motero wanyazitsa kukongola kwako podzipereka kwa aliyense amene adutsapo.
Her yolun başına kendin için yüksek tapınma yerleri kurdun, güzelliğini kirlettin, her geçene kendini teslim ettin, fahişeliklerini artırdın.
26 Umachita chigololo ndi Aigupto, anthu adama oyandikana nawe. Choncho unandikwiyitsa chifukwa unachulukitsa za dama zako.
Şehvet düşkünü komşuların Mısırlılar'la fahişelik ettin. Fahişeliklerini artırmakla beni öfkelendirdin.
27 Nʼchifukwa chake ndinatambasula dzanja langa kukukantha ndi kuchepetsa dziko lako. Ndinakupereka kwa adani ako, Afilisti amene amayipidwa ndi makhalidwe ako onyansa.
İşte bu yüzden elimi sana karşı uzattım, yiyecek payını azalttım. Ahlaksız davranışından utanç duyan düşmanların Filist kızları dilediklerini yapsınlar diye seni onlara teslim ettim.
28 Chifukwa cha chilakolako chako unachitanso zadama ndi Aasiriya. Ngakhale unachita nawo chigololo koma sunakhutitsidwebe.
Asurlular'la da fahişelik ettin, çünkü doymamıştın. Evet, onlarla fahişelik ettin, yine doymadın.
29 Choncho unapitirirabe kuchita chigololo ndi Ababuloni, anthu a mʼdziko lokonda zamalonda. Ngakhale unachita izi, komabe sunakhutitsidwe.
Fahişeliğini ticaret diyarı olan Kildan ülkesine dek artırdın, yine de doymadın.
30 “‘Ambuye Yehova akuti: Mtima wako ndi wofowoka kwambiri chifukwa unachita zonsezo monga ngati mkazi wopanga manyazi.
“‘Bütün bunları yaparken yüreğin ne kadar yıpranmış’ diyor Egemen RAB, ‘Yüzsüz bir fahişe gibi davrandın!
31 Unamanga nsanja pa msewu uliwonse. Unamanganso kachisi pabwalo lililonse. Komabe sunachite ngati mkazi wadama chifukwa unakana malipiro.
Her yolun başına fuhuş yuvaları kurarken, bütün meydanlarda yüksek tapınma yerleri yaparken, fahişe gibi bile değildin, ücretini küçümsedin.
32 “‘Iwe mkazi wachigololo! Umakonda amuna achilendo kupambana mwamuna wakowako!
“‘Kocasının yerine yabancıları yeğleyen, zina eden bir kadındın!
33 Amuna ndiwo amapereka malipiro kwa mkazi wadama. Koma iwe ndi amene ukupereka mphatso kwa zibwenzi zako zonse. Choncho umazinyengerera kuti zizibwera kwa iwe kuchokera mbali zonse kudzagona nawe.
Fahişelere ücret ödenir. Oysa sen bütün oynaşlarına armağanlar dağıttın. Fahişelik etmek için her yandan sana gelsinler diye rüşvet verdin.
34 Chotero iwe ukusiyana ndi akazi ena achigololo, pakuti palibe amene ankakunyengerera kuti uchite naye chigololo. Iweyo ndiye unkapereka ndalama osati ena kukupatsa ndalama ayi. Motero unalidi wosiyana kwambiri ndi akazi ena.
Fahişeliğinde öbür kadınlara benzemiyorsun. Çünkü fahişelik edesin diye kimse senin peşine düşmüyor. Ücret ödeyen sensin, kimse sana ücret ödemiyor. Bu yüzden öbürlerine benzemiyorsun.
35 “‘Tsono mkazi wachigololo iwe, imva mawu a Yehova!
“‘Bu nedenle, ey fahişe, RAB'bin sözünü dinle!
36 Ambuye Yehova akuti, popeza unavula ndi kuonetsa umaliseche wako mopanda manyazi, unachita chigololo ndi zibwenzi zako pamodzi ndi mafano ako onyansa, komanso popeza unapereka ana ako kuti aphedwe ngati nsembe zoperekedwa kwa mafano,
Egemen RAB şöyle diyor: Yüzsüzlüğün ortaya döküldüğü, oynaşlarınla fahişelik ederken çıplaklığın meydana çıktığı için, bütün iğrenç putların yüzünden, onlara çocuklarının kanını verdiğin için,
37 nʼchifukwa chake Ine ndidzasonkhanitsa zibwenzi zako zonse, zimene unkasangalala nazo, amene unkawakonda ndi amene unkawada. Ndidzawasonkhanitsa motsutsana nawe kuchokera ku madera onse okuzungulira ndipo Ine ndidzakuvula pamaso pawo, ndipo iwo adzaona umaliseche wako wonse.
düşüp kalktığın bütün oynaşlarını –sevdiklerini de nefret ettiklerini de– toplayacağım. Sana karşı onları her yandan toplayacak, çıplaklığını onların önüne sereceğim; bütün çıplaklığını görecekler.
38 Ine ndidzakulanga monga mmene amalangira akazi amene amachita chigololo ndiponso opha anthu. Chifukwa cha ukali wanga ndi nsanje yanga, ndidzakhetsa magazi ako mokwiya kwambiri.
Sana zina eden, kan döken kadınlara verilen cezayı vereceğim. Kanını akıtarak seni öfkemin ve kıskançlığımın öcüne terk edeceğim.
39 Ndidzakupereka mʼmanja mwa zibwenzi zako ndi kuwononga nyumba zopembedzera mafano ako. Iwo adzakuvula zovala zako ndi kutenga zodzikometsera zako zabwino. Choncho adzakusiya wa maliseche ndi wausiwa.
Seni oynaşlarının eline teslim edeceğim. Fuhuş yuvalarını yıkacak, yüksek tapınma yerlerini bozacaklar. Üzerindeki giysileri soyacak, güzel mücevherlerini alıp seni çırılçıplak bırakacaklar.
40 Iwo adzabweretsa gulu la anthu limene lidzakuponya miyala ndi kukutematema ndi malupanga awo.
Halkı sana karşı kışkırtacaklar. Seni taşlayacak, kılıçlarıyla delik deşik edecekler.
41 Adzatentha nyumba zako ndi kukulanga iwe pamaso pa akazi ambiri. Ndidzathetsa chigololo chako, ndipo sudzalipiranso zibwenzi zako.
Evlerini ateşe verecek, seni birçok kadının gözü önünde yargılayacaklar. Fahişeliklerine son vereceğim, artık oynaşlarına ücret ödemeyeceksin.
42 Ukali wanga udzalekera pamenepo ndipo sindidzakuchitiranso nsanje. Ndidzakhala chete osakwiyanso.
Böylece sana karşı öfkem yatışacak, kıskançlığım dinecek. Susacak, bir daha öfkelenmeyeceğim.
43 “‘Popeza sunakumbukire masiku a ubwana wako koma unandikwiyitsa ndi zinthu zonsezi, Ine ndidzakubwezera ndithu chilango pamutu pako chifukwa cha zimene wachita, akutero Ambuye Yehova. Paja unawonjezera chigololo pa machitidwe ako onyansa.
“‘Madem gençlik günlerini anımsamadın, yaptıklarınla beni öfkelendirdin, ben de yaptıklarını senin başına getireceğim. Böyle diyor Egemen RAB. Bu iğrenç uygulamalarına ek olarak ahlaksızlık da ettin.
44 “‘Taona, onse onena miyambi adzakuphera mwambi wakuti, ‘Make mbuu, mwana mbuu.’
“‘Herkes senin için şu deyişi söyleyecek: Annesi nasılsa kızı da öyle.
45 Ndiwedi mwana weniweni wamkazi wa mayi wako, amene amanyoza mwamuna wake ndi ana ake. Ndiwe mʼbale weniweni wa abale ako, amene amanyoza amuna awo ndi ana awo. Amayi ako anali Mhiti ndipo abambo ako anali Mwamori.
Sen kocasından ve çocuklarından tiksinen annenin kızısın; kocalarından ve çocuklarından tiksinen kızkardeşlerinin kızkardeşisin. Annen Hititli, baban Amorlu'ydu.
46 Mkulu wako anali Samariya, ndipo iye pamodzi ndi ana ake aakazi ankakhala cha kumpoto kwako. Mngʼono wako, Sodomu ankakhala cha kummwera kwako pamodzi ndi ana ake aakazi.
Kızlarıyla senin kuzeyinde yaşayan Samiriye ablan, kızlarıyla senin güneyinde yaşayan Sodom kızkardeşindir.
47 Iwe sunangotsatira kokha njira zawo zoyipa ndi kuchita zonyansa zawo, koma patangopita nthawi pangʼono machitidwe ako oyipa anaposa awo.
Sen yalnız onların yolunda yürümekle, onların iğrenç uygulamalarına uymakla kalmadın, bütün yaptıklarınla kısa sürede onlardan daha büyük kötülük ettin.
48 Ndithu pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Yehova, ngakhale mʼbale wako Sodomu ndi ana ake aakazi sanachitepo zimene iwe ndi ana ako aakazi munachita.
Varlığım hakkı için diyor Egemen RAB, kızkardeşin Sodom'la kızları, kızlarınla senin yaptıklarını asla yapmadılar.
49 “‘Tsono tchimo la mʼbale wako Sodomu linali ili: Iye ndi ana ake aakazi ankanyadira kuchuluka kwa chakudya ndi chuma chawo. Koma sanalabadireko kuthandiza osauka ndi aumphawi.
“‘Kızkardeşin Sodom'un günahı şuydu: Kendisi de kızları da gururluydu, ekmeğe doymuşlardı, umursamazlardı. Düşküne, yoksula yardım elini uzatmadılar.
50 Anali odzitukumula ndipo ankachita zonyansa pamaso panga. Nʼchifukwa chake ndinawachotsa monga mmene waoneramu.
Kendilerini beğenmişlerdi. Önümde iğrenç şeyler yaptılar. Bu nedenle, gördüğün gibi onları önümden süpürüp attım.
51 Samariya sanachite ngakhale theka la machimo amene unachita. Iwe wachita zinthu zonyansa zambiri kuposa iwo, motero kuti abale ako awiriwo amaoneka ngati olungama kuyerekeza ndi iye.
Samiriye işlediğin günahın yarısını bile işlemedi. Sen onlardan çok daha iğrenç şeyler yaptın. Yaptığın iğrençliklerle kızkardeşlerini suçsuz çıkardın.
52 Tsono iwenso uyenera kuchita manyazi popeza waonetsa abale ako ngati osachimwa. Popeza kuti machimo ako ndi onyansa kwambiri kupambana awo, tsonotu iwowo akuoneka olungama kupambana iweyo. Choncho iwenso uchite manyazi ndi kunyozedwa popeza unaonetsa abale ako ngati olungama.
Düşeceğin utanca katlanacaksın. Çünkü kızkardeşlerini haklı gibi gösterdin. İşlediğin günahlar onlarınkinden daha iğrenç olduğundan senin yanında suçsuz kalıyorlar. Bunun için utan ve düşeceğin utanca katlan. Çünkü kızkardeşlerini suçsuz çıkardın!
53 “‘Koma, ndidzadalitsanso Sodomu ndi ana ake aakazi. Ndidzadalitsanso Samariya ndi ana ake aakazi. Pa nthawi yomweyo ndidzakudalitsanso iwe Yerusalemu.
“‘Sodom'la kızlarını, Samiriye'yle kızlarını, onlarla birlikte de seni eski gönencine kavuşturacağım.
54 Ndidzatero kuti uchite manyazi ndi kunyozeka chifukwa cha zonse zimene unachita powatonthoza anthuwa.
Utanca boğulacaksın. Bütün yaptıklarından ötürü kızkardeşlerine avuntu olacak ve utanacaksın.
55 Motero mʼbale wako Sodomu ndi ana ake akadzakhala monga mmene analili poyamba paja, ndiponso mʼbale wako Samariya akadzakhalanso monga mmene anali poyamba paja, ndiye kuti iwenso ndi ana ako mudzakhala monga mmene munalili payamba paja.
Kızkardeşlerin Sodom ve Samiriye ile kızları eski durumlarına dönecekler; kızlarınla sen de öyle.
56 Kale lija pamene unkanyada, suja unkanyogodola mʼbale wako Sodomu
Kötülüğün açığa çıkmadan önce, gururlu olduğun günlerde kızkardeşin Sodom'un adını bile anmıyordun. Şimdi sen de Edom kızlarıyla komşuları ve Filist kızlarınca –çevrende seninle alay edenlerce– küçümseniyorsun.
57 kuyipa kwako kusanadziwike? Koma tsopano wafanana naye. Wasandukano chinthu chonyozeka kwa anthu a ku Edomu ndi kwa onse owazungulira ndiponso kwa Afilisti. Ndithu onse amene akuzungulira amakunyoza.
58 Choncho udzalangidwa chifukwa cha zigololo zako ndi machitidwe anu onyansa, akutero Yehova.
Ahlaksızlığının ve yaptığın iğrençliklerin sonuçlarına katlanacaksın. RAB böyle diyor.
59 “‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzakulanga molingana ndi zimene unachita. Iwe unanyoza lumbiro lako pophwanya pangano langa.
“‘Egemen RAB şöyle diyor: Seninle yaptığım antlaşmayı bozarak içtiğin andı küçümsedin. Ben de hak ettiğin biçimde seni cezalandıracağım.
60 Komabe, Ine ndidzakumbukira pangano limene ndinachita nawe mʼmasiku a unyamata wako, ndipo ndidzakhazikitsa pangano losatha ndi iwe.
Gençlik günlerinde seninle yaptığım antlaşmayı anımsayacağım. Seninle sonsuza dek kalıcı bir antlaşma yapacağım.
61 Tsono udzakumbukira njira zako zakale. Udzachita manyazi polandiranso abale ako, wamkulu ndi wamngʼono yemwe. Ndidzawaperekanso kwa iwe kuti akhale ngati ana ako ngakhale kuti sali a mʼpangano langa ndi iwe.
Büyük, küçük kızkardeşlerini yanına aldığında yaptıklarını anımsayacak ve utanacaksın. Seninle yaptığım antlaşmada olmadığı halde onları kızların olsunlar diye sana vereceğim.
62 Kotero ndidzakhazikitsa pangano langa ndi iwe, ndipo iwe udzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
Seninle yeniden antlaşma yapacağım, benim RAB olduğumu anlayacaksın.
63 Ndikadzakukhululukira zoyipa zako zonse zimene unachita, udzazikumbukira ndipo udzachita manyazi kwambiri, kotero kuti sudzatha nʼkuyankhula komwe, akutero Ambuye Yehova.’”
Bütün yaptıklarını bağışladığımda, anımsayacak ve utanacaksın. Utancından bir daha ağzını açmayacaksın. Egemen RAB böyle diyor.’”

< Ezekieli 16 >