+ Genesis 1 >

1 Pachiyambi Mulungu analenga kumwamba ndi dziko lapansi.
In the begynnynge God created heaven and erth.
2 Dziko lapansi linali losakonzedwa ndi lopanda kanthu. Mdima wandiweyani unakuta nyanja ndipo Mzimu wa Mulungu unkayendayenda pamwamba pa madziwo.
The erth was voyde and emptie ad darcknesse was vpon the depe and the spirite of god moved vpon the water
3 Pamenepo Mulungu anati, “Kuwale” ndipo kunawaladi.
Than God sayd: let there be lyghte and there was lyghte.
4 Mulungu anaona kuti kuwalako kunali bwino ndipo Iye analekanitsa kuwala ndi mdima.
And God sawe the lyghte that it was good: and devyded the lyghte from the darcknesse
5 Mulungu anatcha kuwalako “usana” ndipo mdima anawutcha “usiku.” Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku loyamba.
and called the lyghte daye and the darcknesse nyghte: and so of the evenynge and mornynge was made the fyrst daye
6 Kenaka Mulungu anati, “Pakhale thambo pakati pa madzi kuti lilekanitse madzi a mʼmwamba ndi madzi a pansi.”
And God sayd: let there be a fyrmament betwene the waters ad let it devyde the waters a sonder.
7 Ndipo Mulungu anapanga thambo nalekanitsa madzi amene anali pansi ndi pamwamba pa thambo lija, ndipo zinachitikadi.
Than God made the fyrmament and parted the waters which were vnder the fyrmament from the waters that were above the fyrmament: And it was so.
8 Mulungu anatcha thambo lija “kumwamba.” Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku lachiwiri.
And God called the fyrmament heaven And so of the evenynge and morninge was made the seconde daye
9 Mulungu anati, “Madzi a pansi pa thambo asonkhane pa malo amodzi kuti mtunda uwoneke,” ndipo zinachitikadi.
And God sayd let the waters that are vnder heaven gather them selves vnto one place that the drye londe may appere: And it came so to passe.
10 Mulungu anawutcha mtundawo “dziko,” madzi osonkhana pamodziwo anawatcha “nyanja.” Ndipo Mulungu anaona kuti zinali bwino.
And god called the drye lande the erth and the gatheringe togyther of waters called he the see. And God sawe that it was good
11 Kenaka Mulungu anati, “Dziko libereke zomera zobala mbewu, mitengo yobala zipatso za mbewu, molingana ndi mitundu yake.” Ndipo zinachitikadi.
And God sayd: let the erth bringe forth herbe and grasse that sowe seed and frutefull trees that bere frute every one in his kynde havynge their seed in them selves vpon the erth. And it came so to passe:
12 Dziko linabereka zomera zokhala ndi mbewu monga mwa mitundu yake ndi mitengo yokhala ndi zipatso za mbewu mʼkati mwake monga mwa mitundu yake. Ndipo Mulungu anaona kuti zinali bwino.
ad the erth brought forth herbe and grasse sowenge seed every one in his kynde and trees berynge frute and havynge their seed in the selves every one in his kynde. And God sawe that it was good:
13 Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku lachitatu.
and the of the evenynge and mornynge was made the thyrde daye.
14 Mulungu anati, “Pakhale zowunikira kuthambo kuti zilekanitse usana ndi usiku. Ndipo zimenezi zikhale zizindikiro zoonetsa nyengo, masiku ndi zaka;
Than sayd God: let there be lyghtes in ye firmament of heaven to devyde the daye fro the nyghte that they may be vnto sygnes seasons days and yeares.
15 zikhale kuthambo kuti ziwunikire pa dziko lapansi. Ndipo zinachitikadi.”
And let them be lyghtes in the fyrmament of heave to shyne vpon the erth. and so it was.
16 Mulungu anapanga zowunikira zazikulu ziwiri; chachikulu chilamulire usana ndi chachingʼono chilamulire usiku. Iye anapanganso nyenyezi.
And God made two great lyghtes A greater lyghte to rule the daye and a lesse lyghte to rule the nyghte and he made sterres also.
17 Mulungu anaziyika mlengalenga kuti ziziwunikira pa dziko lapansi,
And God put them in the fyrmament of heaven to shyne vpon the erth
18 kuti zilamulire usana ndi usiku, ndi kuti zilekanitse kuwala ndi mdima. Mulungu anaona kuti zinali bwino.
and to rule the daye and the nyghte ad to devyde the lyghte from darcknesse. And god sawe yt it was good:
19 Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku lachinayi.
and so of the evenynge ad mornynge was made the fourth daye.
20 Mulungu anati, “Mʼmadzi mukhale zamoyo zochuluka ndipo mbalame ziwuluke mlengalenga pamwamba pa dziko lapansi.”
And God sayd let the water bryng forth creatures that move and have lyfe and foules for to flee over the erth vnder the fyrmament of heaven.
21 Choncho Mulungu analenga zamoyo zikuluzikulu za mʼnyanja ndi chamoyo chamtundu uliwonse chokhala mʼmadzi ndi mbalame iliyonse ya mapiko monga mwa mtundu wake. Mulungu anaona kuti zinali bwino.
And God created greate whalles and all maner of creatures that lyve and moue which the waters brought forth in their kindes ad all maner of federed foules in their kyndes. And God sawe that it was good:
22 Mulungu anazidalitsa nati, “Muswane, ndi kudzaza mʼmadzi a mʼnyanja, ndipo mbalame zichuluke pa dziko lapansi.”
and God blessed them saynge. Growe and multiplye ad fyll the waters of the sees and let the foules multiplye vpo the erth.
23 Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku lachisanu.
And so of the evenynge and morninge was made the fyfth daye.
24 Kenaka Mulungu anati, “Dziko lapansi litulutse zolengedwa zamoyo monga mwa mitundu yawo: ziweto, zolengedwa zokwawa ndi nyama zakuthengo, iliyonse monga mwa mtundu wake.” Ndipo zinaterodi.
And God sayd: leth the erth bring forth lyvynge creatures in thir kyndes: catell and wormes and beastes of the erth in their kyndes and so it came to passe.
25 Mulungu anapanga nyama zakuthengo monga mwa mitundu yawo, nyama zoweta monga mwa mitundu yawo ndi nyama zokwawa monga mwa mitundu yawo. Ndipo Mulungu anaona kuti zinali bwino.
And god made the beastes of the erth in their kyndes and catell in their kyndes ad all maner wormes of the erth in their kyndes: and God sawe that it was good.
26 Zitatha izi Mulungu anati, “Tipange munthu mʼchifanizo chathu, mofanana ndi ife kuti alamulire nsomba za mʼnyanja, mbalame zamlengalenga, nyama zonse zoweta ndi zonse zokwawa za pa dziko lapansi ndi zamoyo zonse zakutchire.”
And God sayd: let vs make man in oure symilitude ad after oure lycknesse: that he may have rule over the fysh of the see and over the foules of the ayre and over catell and over all the erth and over all wormes that crepe on the erth.
27 Ndipo Mulungu analenga munthu mʼchifanizo chake. Anawalengadi mʼchifanizo cha Mulungu; analenga iwo, mwamuna ndi mkazi.
And God created man after hys lycknesse after the lycknesse of god created he him: male and female created he them.
28 Mulungu anawadalitsa nati kwa iwo, “Muberekane, muchulukane, mudzaze dziko lapansi ndipo muligonjetse. Mulamulire nsomba zamʼnyanja, mbalame zamlengalenga ndi cholengedwa chamoyo chilichonse chimene chimayenda mokwawa pa dziko lapansi.”
And God blessed them and God sayd vnto them. Growe and multiplye and fyll the erth and subdue it and have domynyon over the fysh of the see and over the foules of the ayre and over all the beastes that move on the erth.
29 Kenaka Mulungu anati, “Ine ndakupatsani chomera chilichonse cha pa dziko lapansi chimene chili ndi mbewu komanso mtengo uliwonse wobala zipatso zokhala ndi mbewu mʼkati mwake kuti zikhale chakudya chanu.
And God sayd: se I have geven yow all herbes that sowe seed which are on all the erth and all maner trees that haue frute in them and sowe seed: to be meate for yow
30 Ndaperekanso msipu kwa nyama zonse za pa dziko lapansi ndi kwa mbalame zamlengalenga ndi kwa cholengedwa chamoyo chilichonse chimene chimakwawa, chilichonse chimene chili ndi moyo.” Ndipo zinachitikadi.
and for all beastes of the erth and vnto all foules of the ayre and vnto all that crepeth on the erth where in is lyfe that they may haue all maner herbes and grasse for to eate and even so it was.
31 Mulungu anaona zonse zimene anazilenga kuti zinali zabwino kwambiri. Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa, tsiku lachisanu ndi chimodzi.
And God behelde al that he had made ad loo they were exceadynge good: and so of the evenynge and mornynge was made the syxth daye

+ Genesis 1 >