< Yesaya 8 >

1 Yehova anati kwa ine, “Tenga cholembapo chachikulu ndipo ulembepo malemba odziwika bwino: Kusakaza-Kwamsanga Kufunkha-Kofulumira.
The LORD said to me, "Take a large tablet, and write on it with a man's pen, 'For Maher Shalal Hash Baz;'
2 Ndipo ndidzayitana wansembe Uriya ndi Zekariya mwana wa Yeberekiya kuti akhale mboni zanga zodalirika.”
and I will take for myself faithful witnesses to testify: Uriah the priest, and Zechariah the son of Berechiah."
3 Ndipo ine ndinapita kwa mneneri wamkazi, ndipo anakhala woyembekezera nabala mwana wamwamuna. Ndipo Yehova anati kwa ine, “Umutche dzina lakuti, ‘Kusakaza-Kwamsanga Kufunkha-Kofulumira.’
I went to the prophetess, and she conceived, and bore a son. Then said the LORD to me, "Call his name 'Maher Shalal Hash Baz.'
4 Mwanayo asanayambe kudziwa kuyitana kuti, ‘Ababa’ kapena ‘Amama’ chuma cha Damasiko ndi zofunkha za Samariya zidzatengedwa ndi mfumu ya ku Asiriya.”
For before the child knows how to say, 'My father,' and, 'My mother,' the riches of Damascus and the spoil of Samaria will be carried away by the king of Assyria."
5 Yehova anayankhulanso ndi Ine;
The LORD spoke to me yet again, saying,
6 “Popeza anthu a dziko ili akana madzi anga oyenda mwachifatse a ku Siloamu, ndipo akukondwerera Rezini ndi mwana wa Remaliya,
"Because this people have refused the waters of Shiloah that go softly, and rejoice in Rezin and Remaliah's son;
7 nʼchifukwa chake Ambuye ali pafupi kubweretsa madzi amkokomo a mtsinje wa Yufurate kudzalimbana nawo; mfumu ya ku Asiriya ndi gulu lake lonse lankhondo. Madziwo adzasefukira mʼngalande zake zonse ndi mʼmagombe ake onse.
now therefore, look, the LORD brings upon them the mighty flood waters of the River: the king of Assyria and all his glory. It will come up over all its channels, and go over all its banks.
8 Ndipo adzalowa mwamphamvu mʼdziko la Yuda, adzasefukira, adzapitirira mpaka kumuyesa mʼkhosi. Mapiko ake otambasuka adzaphimba dziko lako lonse, iwe Imanueli!”
It will sweep onward into Judah. It will overflow and pass through; it will reach even to the neck; and the stretching out of its wings will fill the breadth of your land, Immanuel.
9 Chitani phokoso lankhondo, inu mitundu ya anthu, ndipo munjenjemere! Tamverani, inu mayiko onse akutali. Konzekerani nkhondo ndipo munjenjemere! Konzekerani nkhondo ndipo munjenjemere!
Make an uproar, you peoples, and be broken in pieces. Listen, all you from far countries. Prepare for battle, and be shattered.
10 Konzani kachitidwe kanu kankhondo, koma simudzaphula kanthu, kambiranani zochita, koma zidzalephereka, pakuti Mulungu ali nafe.
Take counsel together, and it will be brought to nothing; speak the word, and it will not stand: for God is with us."
11 Yehova anandiyankhula ine mwamphamvu, ndipo anandichenjeza kuti ndisamayende mʼnjira za anthuwa. Iye anati:
For the LORD spoke thus to me with a strong hand, and instructed me not to walk in the way of this people, saying,
12 “Usamanene kuti ndi chiwembu, chilichonse chimene anthuwa amati ndi chiwembu usamaope zimene anthuwa amaziopa, ndipo usamachite nazo mantha.
"Do not say, 'A conspiracy.' concerning all about which this people say, 'A conspiracy.' And do not fear what they fear, nor be in dread.
13 Yehova Wamphamvuzonse ndiye amene uyenera kumuona kuti ndi woyera, ndiye amene uyenera kumuopa, ndiye amene uyenera kuchita naye mantha,
The LORD of hosts is who you must regard as holy. He is the one you must fear. He is the one you must dread.
14 ndipo ndiye amene adzakhala malo opatulika; koma kwa anthu a ku Yuda ndi kwa anthu a ku Israeli adzakhala mwala wopunthwitsa, mwala umene umapunthwitsa anthu, thanthwe limene limagwetsa anthu. Ndipo kwa anthu a mu Yerusalemu adzakhala ngati msampha ndi khwekhwe.
And he will be a sanctuary; but for a stone of stumbling and for a rock that makes them fall to both the houses of Israel, for a trap and for a snare to the inhabitants of Jerusalem.
15 Anthu ambiri adzapunthwapo adzagwa ndi kuthyokathyoka, adzakodwa ndi kugwidwa.”
Many will stumble over it, fall, be broken, be snared, and be captured."
16 Manga umboniwu ndipo umate malamulowa pamaso pa ophunzira anga.
Wrap up the testimony. Seal the law among my disciples.
17 Ndidzayembekezera Yehova, amene akubisira nkhope yake nyumba ya Yakobo. Ine ndidzakhulupirira Iyeyo.
I will wait for the LORD, who hides his face from the house of Jacob, and I will trust in him.
18 Onani, ine ndili pano pamodzi ndi ana amene Yehova wandipatsa, ndife zizindikiro ndi zodabwitsa kwa Aisraeli zochokera kwa Yehova Wamphamvuzonse, amene amakhala pa Phiri la Ziyoni.
Look, I and the children whom God has given me are for signs and wonders in Israel from the LORD of hosts, who dwells on Mount Zion.
19 Anthu akakuwuza kuti kafunsire kwa oyankhula ndi mizimu, amene amayankhula monongʼona ndi mongʼungʼudza, kodi anthu sayenera kukafunsira kwa Mulungu wawo? Chifukwa chiyani amafunsira kwa anthu akufa mʼmalo mwa kwa anthu amoyo,
When they tell you, "Consult with the spirits of the dead and familiar spirits who chirp and who mutter. Shouldn't a people consult with their gods, by consulting the dead on behalf of the living?"
20 kuti akalandireko mawu enieni ndi malangizo? Ngati anthuwo sayankhula monga mwa mawu awa, mwa iwo mulibe kuwala.
Turn to the law and to the testimony. If they do not speak according to this word, surely there is no morning for them.
21 Anthu adzayendayenda mʼdziko movutika kwambiri ali ndi njala; pamene afowokeratu ndi njala, iwo adzakwiya kwambiri ndipo adzayangʼana kumwamba ndi kutemberera mfumu yawo ndi Mulungu wawo.
They will pass through it, greatly distressed and hungry; and it will happen that when they are hungry, they will worry, and curse by their king and by their God. They will turn their faces upward,
22 Ndipo akadzayangʼana pa dziko lapansi adzangoona mavuto okhaokha ndi mdima woopsa ndi wodetsa nkhawa, ndipo adzaponyedwa mu mdima wandiweyani.
and look to the earth, and see distress, darkness, and the gloom of anguish. They will be driven into thick darkness.

< Yesaya 8 >