< Yeremiya 34 >

1 Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni ndi gulu lake lonse lankhondo, pamodzi ndi maufumu onse a pa dziko lapansi amene ankawalamulira ndiponso anthu a mitundu yonse ankathira nkhondo Yerusalemu ndi mizinda yonse yozungulira Yehova anayankhula ndi Yeremiya kuti,
The word that came to Jeremiah from the Lord, when Nebuchadnezzar, the king of Babylon, and his entire army, and all the kingdoms of the earth that were under the authority of his hand, and all the people were making war against Jerusalem and against all of its cities, saying:
2 “Yehova, Mulungu wa Israeli akuti: Pita kwa Zedekiya mfumu ya Yuda ndipo ukamuwuze kuti Yehova akuti mzinda uno ndidzawupereka mʼmanja mwa mfumu ya ku Babuloni ndipo adzawutentha ndi moto.
“Thus says the Lord, the God of Israel: Go, and speak to Zedekiah, the king of Judah. And you shall say to him: Thus says the Lord: Behold, I will deliver this city into the hands of the king of Babylon, and he will burn it with fire.
3 Iweyo sudzapulumuka mʼmanja mwake koma udzagwidwa ndithu ndipo adzakupereka mʼmanja mwake. Udzayiona mfumu ya ku Babuloni maso ndi maso ako ndipo udzayankhula nayo pakamwa ndi pakamwa. Ndipo udzapita ku Babuloni.
And you will not escape from his hand. Instead, you will be overtaken and captured, and you will be delivered into his hand. And your eyes will see the eyes of the king of Babylon, and his mouth will speak with your mouth, and you will enter into Babylon.
4 “Koma iwe Zedekiya mfumu ya Yuda, imva lonjezo ili la Yehova. Izi ndi zimene Yehova akunena za iwe: Sudzaphedwa pa nkhondo;
Even so, listen to the word of the Lord, Zedekiah, king of Judah: Thus says the Lord to you: You will not die by the sword.
5 udzafera pa mtendere. Monga anthu ankafukiza lubani poyika maliro a makolo ako akale, amene anali mafumu iwe usanalowe ufumu, choncho nawenso podzayika maliro ako adzafukiza lubani ndipo polira azidzati, ‘Kalanga, mbuye wanga!’ Ine mwini ndalonjeza zimenezi, akutero Yehova.”
Instead, you will die in peace. And, in accord with the burnings of your fathers, the former kings who were before you, so will they burn you. And they will mourn you, saying: ‘Alas, lord!’ For I have spoken the word, says the Lord.”
6 Ndipo mneneri Yeremiya anawuza zonsezi Zedekiya mfumu ya Yuda, mu Yerusalemu.
And Jeremiah, the prophet, spoke all these words to Zedekiah, the king of Judah, in Jerusalem.
7 Nthawi imeneyi nʼkuti gulu lankhondo la mfumu ya ku Babuloni likuthira nkhondo Yerusalemu ndi mizinda ina yotsala ya Yuda, Lakisi ndi Azeka. Imeneyi yokha ndiye inali mizinda yotetezedwa yotsala ya ku Yuda.
And the army of the king of Babylon fought against Jerusalem and against all the cities of Judah that remained, against Lachish and against Azekah. For only these remained out of the cities of Judah that were fortified cities.
8 Yehova anayankhulanso ndi Yeremiya. Nthawi imeneyi nʼkuti mfumu Zedekiya atachita pangano ndi anthu onse a mu Yerusalemu kuti alengeze zakuti akapolo awo adzawamasule.
The word that came to Jeremiah from the Lord, after king Zedekiah had struck a pact with all the people in Jerusalem, proclaiming
9 Aliyense amene anali ndi akapolo a Chihebri, aamuna kapena aakazi awamasule; palibe amene ayenera kusunga mu ukapolo Myuda mnzake.
that each one should release his man servant, and each one his woman servant, as a free Hebrew man and a free Hebrew woman, and that they should never be rulers over them, that is, over the Jews, their own brothers.
10 Choncho akuluakulu pamodzi ndi anthu onse amene anachita pangano ili anagwirizana kuti amasule akapolo awo aamuna ndi aakazi ndi kuti asawasungenso mu ukapolo. Iwo anachitadi zimenezi ndipo anawamasuladi.
Then all the leaders and all the people who entered into the pact, heard that each one should release his man servant, and each one his woman servant, to be free, and that they should no longer rule over them. Therefore, they listened, and they released them.
11 Koma pambuyo pake anasintha maganizo awo ndi kuwatenganso amuna ndi akazi amene anawamasula aja ndipo anawasandutsanso akapolo.
But later on, they turned back. And they took back again their man servants and their woman servants, whom they had released to be free. And they subjugated them as male and female servants.
12 Tsono Yehova anawuza Yeremiya kuti:
And the word of the Lord came to Jeremiah from the Lord, saying:
13 “Yehova Mulungu wa Israeli akuti: Ine ndinachita pangano ndi makolo anu pamene ndinawatulutsa ku Igupto, mʼdziko la ukapolo. Ine ndinati,
“Thus says the Lord, the God of Israel: I struck a pact with your fathers in the day when I led them away from the land of Egypt, from the house of servitude, saying:
14 ‘Chaka chachisanu ndi chiwiri chilichonse aliyense wa inu ayenera kumasula mʼbale wake wa Chihebri amene anadzigulitsa yekha kwa inuyo. Iyeyo amasulidwe akagwira ntchito zaka zisanu ndi chimodzi, mumulole apite mwaufulu.’ Komatu makolo anu sanandimvere kapena kusamala konse.
‘When seven years have been completed, let each one release his brother, a Hebrew, who had been sold to him. And so he will serve you for six years, and then you shall release him to be free from you.’ But your fathers did not listen to me, nor did they incline their ear.
15 Posachedwa pomwepa inu munalapa ndi kuchita zinthu zabwino pamaso panga: Aliyense wa inu anamasula mʼbale wake. Ndipo munachita pangano pamaso panga mʼNyumba imene imadziwika ndi dzina langa kuti mudzachitadi zimenezi.
And today you converted, and you did what is right in my eyes, so that you proclaimed liberty, each one to his friend. And you entered into a pact in my sight, in the house in which and over which my name is invoked.
16 Koma tsopano mwasintha maganizo anu ndipo mwayipitsa dzina langa. Mwatenganso ukapolo aamuna ndi aakazi amene munawamasula aja kuti apite kumene akufuna. Mwawakakamiza kuti akhalebe akapolo anu.
But now you have turned back, and you have stained my name. For you have led back again, each one his man servant, and each one his woman servant, whom you had released so that they would be free and under their own authority. And you have subjugated them, so that they would be your servants and handmaids.”
17 “Nʼchifukwa chake Yehova akuti: Inu simunandimvere Ine; simunalengeze kuti abale anu amasulidwe. Chabwino! Ine ndidzakupatsani ufulu; ufulu wake ukhala wophedwa ndi nkhondo, mliri ndi njala. Ndidzakusandutsani chinthu chochititsa mantha pakati pa maufumu onse a dziko lapansi.
Because of this, thus says the Lord: “You have not heeded me, though you proclaimed liberty, each one to his brother and each one to his friend. Behold, I am proclaiming a liberty for you, says the Lord, to the sword, to pestilence, and to famine. And I will cause you to be removed to all the kingdoms of the earth.
18 Inu simunasunge pangano limene munachita ndi Ine. Simunasamale lonjezo limene munachita pamaso panga. Choncho ndidzakusandutsani ngati mwana wangʼombe uja amene ankamudula pawiri napita pakati pa zigawozo.
And I will give over the men who have betrayed my covenant, and who have not observed the words of the covenant, to which they assented in my sight when they cut the calf into two parts and passed between its parts:
19 Amene ankadutsa pakati pa zigawozo anali atsogoleri a Yuda ndi Yerusalemu, akuluakulu a bwalo, ansembe ndi anthu onse a mʼdzikomo.
the leaders of Judah, and the leaders of Jerusalem, the eunuchs and the priests, and all the people of the land, who have passed between the parts of the calf.
20 Onsewa ndidzawapereka kwa adani awo amene akufuna kuwapha. Mitembo yawo idzakhala chakudya cha mbalame zamlengalenga ndi zirombo za dziko lapansi.
And I will give them into the hands of their enemies and into the hands of those who are seeking their life. And their dead bodies will be food for the birds of the air and for the beasts of the earth.
21 “Ndidzapereka Zedekiya mfumu ya Yuda ndi nduna zake kwa adani awo amene akufuna kuwapha, kwa gulu lankhondo la mfumu ya ku Babuloni limene nthawi ino layamba kubwerera mʼmbuyo.
And Zedekiah, the king of Judah, and his leaders, I will give over to the hands of their enemies, and to the hands of those who are seeking their lives, and to the hands of the armies of the king of Babylon, which had withdrawn from you.
22 Taonani, Ine ndidzawalamula, akutero Yehova, ndipo ndidzawabweretsanso ku mzinda uno. Adzathira nkhondo mzindawu, kuwulanda ndi kuwutentha. Ndipo Ine ndidzasandutsa chipululu mizinda ya Yuda kotero kuti palibe amene adzakhalemo.”
Behold, I will command, says the Lord, and I will lead them back to this city, and they will fight against it, and seize it, and set it on fire. And I will make the cities of Judah into a desolation, for there shall be no inhabitant.”

< Yeremiya 34 >