< Yobu 24 >

1 “Chifukwa chiyani Wamphamvuzonse sayikiratu nthawi yoti aweruze? Chifukwa chiyani iwo amene amadziwa Iyeyo amayembekezera pachabe masiku oterewa?
¿Por qué no son reservados los tiempos oportunos por ʼEL-Shadday? ¿Por qué los que lo conocen no vislumbran sus días?
2 Anthu amasuntha miyala ya mʼmalire, kuti akuze dziko lawo; amadyetsa ziweto zimene aba.
Hay los que remueven los linderos, roban los rebaños y los devoran,
3 Amalanda abulu a ana amasiye ndipo amatenganso ngʼombe ya mkazi wamasiye ngati chikole.
se llevan el asno de los huérfanos, toman en prenda el buey de la viuda,
4 Amachotsa mʼmisewu anthu osauka, ndipo amathamangitsa amphawi onse mʼdziko.
apartan del camino a los necesitados y hacen que se escondan todos los pobres de la tierra.
5 Amphawiwo amakhala ngati mbidzi mʼchipululu, amayendayenda kufuna chakudya; dziko lowuma limapereka chakudya cha ana awo.
Allí están, como asnos del desierto. Salen a su tarea y buscan con ansia el sustento. La región fría es la que ofrece alimento a sus hijos,
6 Iwo amakolola za mʼminda ya eni ake, ndipo amakunkha mphesa mʼminda ya anthu oyipa.
cosechan en campo ajeno, y tienen que rebuscar en la viña del perverso.
7 Amagona maliseche usiku wonse kusowa zovala; pa nthawi yozizira amasowa chofunda.
Pasan la noche desnudos, faltos de ropa y no tienen cobertura contra el frío.
8 Amavumbwa ndi mvula ya mʼmapiri ndipo amakangamira ku matanthwe kusowa pobisalapo.
El aguacero de las montañas los empapa, y se pegan a las rocas por falta de refugio.
9 Amatsomphola mwana wamasiye wa ku bere; ndipo amagwira mwana wakhanda wa mʼmphawi kuti akhale chikole.
Hay otros que arrancan del pecho al huérfano, y toman en prenda al bebé del pobre.
10 Amphawi amangoyenda maliseche kusowa zovala; amasenza mitolo ya tirigu, koma nʼkumagonabe ndi njala.
Hacen que anden mudos, sin ropa, y quitan las gavillas al hambriento,
11 Iwo amayenga mafuta a olivi mʼminda ya anthu oyipa; amapsinya mphesa, koma nʼkumamvabe ludzu.
los que exprimen el aceite en sus molinos, y pisan sus lagares, pero tienen sed.
12 Kubuwula kwa anthu amene akufa kumamveka kuchokera mu mzinda, anthu ovulala akulirira chithandizo. Koma Mulungu sakuyimba mlandu wina aliyense.
Desde la ciudad gimen los hombres y claman los heridos, pero ʼElohim no atiende sus necedades.
13 “Pali ena amene amakana kuwala, amene safuna kuyenda mʼkuwalako kapena kukhala mʼnjira zake.
Son los que se rebelan contra la luz. No quieren conocer sus caminos ni están en sus sendas.
14 Dzuwa likalowa, wopha anzake amadzuka ndipo amakapha osauka ndi amphawi; nthawi ya usiku iye amasanduka mbala.
De madrugada se levanta el asesino, mata al pobre y al menesteroso, y de noche actúa como ladrón.
15 Munthu wachigololo amadikira chisisira; iyeyo amaganiza kuti, ‘Palibe amene akundiona,’ ndipo amaphimba nkhope yake.
El adúltero espera la llegada de la noche y se dice: Nadie me verá. Y cubre su cara.
16 Mbala zimathyola nyumba usiku, koma masana zimadzitsekera; izo zimathawa kuwala.
Mina las casas en la oscuridad. Durante el día se encierra. No conoce la luz del sol.
17 Pakuti kwa onsewa mdima wandiweyani ndiye kuti kwawachera. Iwo amachita ubale ndi zoopsa za mdima.
Porque la mañana le es lo mismo que densa oscuridad, porque está familiarizado con los terrores de densa oscuridad.
18 “Komatu iwowo ndi thovu loyandama pa madzi; minda yawo ndi yotembereredwa pa dzikolo kotero kuti palibe amene amapita ku minda ya mpesa.
Es veloz sobre la superficie del agua. Su parte es maldita en la tierra. No volverá por el camino de las viñas.
19 Monga momwe kutentha ndi chilala zimasungunulira madzi owundana ndi momwemonso mmene manda amachotsera omwe achimwa. (Sheol h7585)
Como la sequía y el calor le roban el agua a la nieve, así hace el Seol a los que pecaron. (Sheol h7585)
20 Mayi wowabereka amawayiwala, mphutsi zimasangalala powadya; anthu oyipa sakumbukiridwanso koma amathyoka ngati mtengo.
Los olvidará el seno materno. Dulce será su sabor a los gusanos. Nunca serán recordados, y como un árbol serán quebrantados los perversos.
21 Amachitira nkhanza mayi wosabala ndi mayi amene alibe mwana, ndipo sakomera mtima mkazi wamasiye.
Porque maltrataron a la estéril, a la que no da a luz, y no hacen bien a la viuda.
22 Koma Mulungu amawononga munthu wamphamvu mwa mphamvu zake; ngakhale munthuyo atakhazikika, alibe chiyembekezo cha moyo wake.
La sequía arruina también a los poderosos con su poder. Se levantan y no creen ni en su propia vida.
23 Mulungu atha kuwalola kuti akhale mosatekeseka, koma amakhala akupenyetsetsa njira zawo.
ʼElohim les da seguridad, y ellos confían en ella. Los ojos de Él observan sus caminos.
24 Kwa kanthawi kochepa oyipa amakwezedwa ndipo kenaka saonekanso; amatsitsidwa ndipo amachotsedwa monga ena onse; amadulidwa ngati ngala za tirigu.
Aunque ensalzados por un tiempo, desaparecen. Son abatidos, marchitados como plantas y cortados como espigas.
25 “Ngati zimenezi sizoona, ndani angaonetse kuti ndine wabodza ndi kusandutsa mawu anga kukhala wopanda pake?”
Si esto no es así, ¿quién me puede probar que soy un mentiroso, y dejar sin valor mis palabras?

< Yobu 24 >