< Yobu 37 >

1 “Mtima wanga ukulumphalumpha pa chimenechinso ndipo ukuchoka mʼmalo mwake.
“Yes, at this my heart trembles, and is moved out of its place.
2 Tamverani! Tamverani kubangula kwa liwu lake, kugunda kumene kukuchokera mʼkamwa mwake.
Hear, oh, hear the noise of his voice, the sound that goes out of his mouth.
3 Iye amaponya chingʼaningʼani chake pansi pa thambo lonse ndipo amachitumiza ku dziko lapansi.
He sends it out under the whole sky, and his lightning to the ends of the earth.
4 Pambuyo pake kubangula kwake kumamveka. Iye amabangula ndi liwu lake laulemerero. Pamene wabangula, palibe chimene amalephera kuchita.
After it a voice roars. He thunders with the voice of his majesty. He doesn’t hold back anything when his voice is heard.
5 Liwu la Mulungu limabangula mʼnjira zambiri zodabwitsa Iye amachita zinthu zazikulu zimene sitingathe kuzimvetsa.
God thunders marvelously with his voice. He does great things, which we can’t comprehend.
6 Amalamula chisanu chowundana kuti, ‘Igwa pa dziko lapansi,’ ndipo amalamulanso mvula yamawawa kuti, ‘Khala mvula yamphamvu.’
For he says to the snow, ‘Fall on the earth,’ likewise to the shower of rain, and to the showers of his mighty rain.
7 Kuti anthu onse amene anawalenga athe kuzindikira ntchito yake. Iye amalepheretsa anthu kugwira ntchito zawo.
He seals up the hand of every man, that all men whom he has made may know it.
8 Zirombo zimakabisala ndipo zimakhala mʼmaenje mwawo.
Then the animals take cover, and remain in their dens.
9 Mphepo yamkuntho imatuluka ku malo ake, kuzizira kumatuluka mʼmphepo yamkunthoyo.
Out of its room comes the storm, and cold out of the north.
10 Mpweya wa Mulungu umawunditsa madzi ndipo madzi a mʼnyanja amawuma kuti gwaa.
By the breath of God, ice is given, and the width of the waters is frozen.
11 Iye amadzaza mitambo ndi madzi a mvula, amabalalitsa zingʼaningʼani zake kuchokera mʼmitambomo.
Yes, he loads the thick cloud with moisture. He spreads abroad the cloud of his lightning.
12 Mulungu amayendetsa mitamboyo mozungulirazungulira dziko lonse lapansi kuti ichite zonse zimene Iye akufuna pa dziko lapansi.
It is turned around by his guidance, that they may do whatever he commands them on the surface of the habitable world,
13 Iye amagwetsa mvula kuti alange anthu, kapena kubweretsa chinyontho pa dziko lapansi kuti aonetse chikondi chake.
whether it is for correction, or for his land, or for loving kindness, that he causes it to come.
14 “Abambo Yobu, tamvani izi; imani ndipo muganizire ntchito zodabwitsa za Mulungu.
“Listen to this, Job. Stand still, and consider the wondrous works of God.
15 Kodi mukudziwa momwe Mulungu amayendetsera mitambo ndi kuchititsa kuti kukhale zingʼaningʼani?
Do you know how God controls them, and causes the lightning of his cloud to shine?
16 Kodi mukudziwa momwe Mulungu amayalira mitambo, ntchito zodabwitsa za Iye amene ndi wanzeru zangwiro?
Do you know the workings of the clouds, the wondrous works of him who is perfect in knowledge?
17 Inu amene mʼzovala zanu mumatuluka thukuta pamene kunja kwatentha chifukwa cha mphepo yakummwera,
You whose clothing is warm when the earth is still by reason of the south wind?
18 kodi mungathe kuthandizana naye kutambasula thambo limene ndi lolimba ngati chitsulo?
Can you, with him, spread out the sky, which is strong as a cast metal mirror?
19 “Tiwuzeni ife zoti tikanene kwa Iye; sitingathe kufotokoza mlandu wathu chifukwa cha mdima umene uli mwa ife.
Teach us what we will tell him, for we can’t make our case by reason of darkness.
20 Kodi nʼkofunika kumudziwitsa Mulungu kuti ndili naye mawu? Kodi kutero sikuchita ngati kupempha kuti ndiwonongeke?
Will it be told him that I would speak? Or should a man wish that he were swallowed up?
21 Tsopano munthu sangathe kuyangʼana dzuwa, ndi kunyezimira mlengalenga, kuwomba kwa mphepo kutachotsa mitambo yonse.
Now men don’t see the light which is bright in the skies, but the wind passes, and clears them.
22 Kuwala kwake kumaonekera cha kumpoto; Mulungu amabwera ndi ulemerero woopsa.
Out of the north comes golden splendor. With God is awesome majesty.
23 Wamphamvuzonse sitingathe kumufikira pafupi ndi wa mphamvu zoposa; pa chiweruzo chake cholungama ndi mʼchilungamo chake chachikulu Iye sapondereza anthu ozunzika.
We can’t reach the Almighty. He is exalted in power. In justice and great righteousness, he will not oppress.
24 Nʼchifukwa chake anthu amamuopa kwambiri, kodi saganizira za onse amene amaganiza kuti ndi anzeru?”
Therefore men revere him. He doesn’t regard any who are wise of heart.”

< Yobu 37 >