< Yoswa 6 >

1 Tsono mzinda wa Yeriko unali utatsekedwa kuti Aisraeli asalowe. Palibe amene amatuluka kapena kulowa.
Torej Jeriha je bila strogo zaprta zaradi Izraelovih otrok. Nihče ni odšel ven in nihče ni prišel noter.
2 Kenaka Yehova anati kwa Yoswa, “Taona ndapereka Yeriko, pamodzi ndi mfumu yake ndi ankhondo ake mʼmanja mwako.
Gospod je rekel Józuetu: »Poglej, v tvojo roko sem izročil Jeriho in njenega kralja in močne junaške može.
3 Tsono iwe pamodzi ndi ankhondo ako onse muzizungulira mzindawu masiku asanu ndi limodzi, kamodzi pa tsiku.
Obdali boste mesto, vsi vi bojevniki in enkrat obhodili mesto. Tako boste počeli šest dni.
4 Ansembe asanu ndi awiri, atanyamula malipenga a nyanga za nkhosa zazimuna, akhale patsogolo pa Bokosi la Chipangano. Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri mudzazungulire mzindawu kasanu ndi kawiri ansembe akuliza malipenga.
Sedem duhovnikov bo pred skrinjo nosilo sedem šofarjev iz ovnovih rogov, in sedmi dan boste sedemkrat obkrožili mesto in duhovniki bodo zatrobili s šofarji.
5 Ansembe adzalize malipenga kosalekeza. Tsono anthu onse akadzamva kuliza kumeneku adzafuwule kwambiri, ndipo makoma a mzindawo adzagwa. Zikadzatero ankhondo adzalowe mu mzindawo.”
In zgodilo se bo, da ko bodo z ovnovim rogom naredili dolgo trobljenje in ko zaslišite zvok šofarja, naj vse ljudstvo zavpije z velikim krikom in mestno obzidje bo plosko padlo dol in ljudstvo se bo povzpelo, vsak človek naravnost pred seboj.«
6 Ndipo Yoswa mwana wa Nuni anayitana ansembe ndipo anawawuza kuti, “Nyamulani Bokosi la Chipangano cha Yehova ndipo ansembe asanu ndi awiri anyamule malipenga. Iwowa akhale patsogolo pake.”
Nunov sin Józue je poklical duhovnike ter jim rekel: »Vzdignite skrinjo zaveze in sedem duhovnikov naj pred Gospodovo skrinjo nosi sedem šofarjev iz ovnovih rogov.«
7 Ndipo analamulira anthu kuti, “Yambani kuyenda! Yendani mozungulira mzinda ndipo ankhondo akhale patsogolo pa Bokosi la Yehova.”
Ljudstvu pa je rekel: »Pojdite naprej in obkrožite mesto in naj tisti, ki je oborožen, gre naprej pred Gospodovo skrinjo.«
8 Mofanana ndi mmene Yoswa anayankhulira kwa anthu aja, ansembe asanu ndi awiri anapita patsogolo pa Bokosi la Chipangano la Yehova akuliza malipenga a nyanga za nkhosa zija, ndipo Bokosi la Chipangano cha Yehova limabwera pambuyo pawo.
Pripetilo se je, ko je Józue govoril ljudstvu, da je sedem duhovnikov, nosečih sedem šofarjev iz ovnovih rogov, šlo naprej pred Gospodom in trobilo s šofarji in skrinja Gospodove zaveze jim je sledila.
9 Ankhondo amayenda patsogolo pa ansembe amene amayimba malipenga, ndiponso gulu lina pambuyo pa Bokosilo. Nthawi yonseyi nʼkuti malipenga akulira.
Oboroženi možje so šli pred duhovniki, ki so trobili na šofarje in zadnja straža je prišla za skrinjo. Duhovniki pa so hodili in trobili s šofarji.
10 Koma Yoswa nʼkuti atalamulira anthu kuti, “Musafuwule, musakweze mawu anu kapena kuyankhula mpaka tsiku limene ndidzakuwuzani kuti mufuwule. Pamenepo mudzafuwule!”
Józue je zapovedal ljudstvu, rekoč: »Ne boste kričali niti naredili nobenega hrupa z vašim glasom niti ne bo nobena beseda izšla iz vaših ust do dneva, ko vam zapovem kričati; potem boste kričali.«
11 Ansembe onyamula Bokosi la Chipangano la Yehova anazungulira mzindawo kamodzi. Kenaka anthu anabwerera ku msasa wawo kukagona.
Tako je Gospodova skrinja obkrožila mesto, ga enkrat obhodila in prišli so v tabor in prenočili v taboru.
12 Yoswa anadzuka mmawa tsiku linalo ndipo ansembe ananyamula Bokosi la Yehova.
Józue je vstal zgodaj zjutraj in duhovniki so dvignili Gospodovo skrinjo.
13 Ansembe asanu ndi awiri onyamula malipenga asanu ndi awiri anakhala patsogolo pa Bokosi la Yehova akuyimba malipenga. Ankhondo anali patsogolo pawo ndipo gulu lina linatsatira Bokosi la Yehova. Apa nʼkuti malipenga akulira.
Sedem duhovnikov, ki so pred Gospodovo skrinjo nosili sedem šofarjev iz ovnovih rogov, je nenehno hodilo naprej in trobilo s šofarji in oboroženi možje so šli pred njimi, toda zadnja straža je prišla za Gospodovo skrinjo, duhovniki hodeč naprej in trobeč s šofarji.
14 Tsiku lachiwiri anazunguliranso mzinda kamodzi ndi kubwerera ku misasa. Iwo anachita izi kwa masiku asanu ndi limodzi.
Drugi dan so enkrat obkrožili mesto in se vrnili v tabor. Tako so počeli šest dni.
15 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri, anadzuka mʼbandakucha ndipo anazungulira mzindawo kasanu ndi kawiri. Ndi pa tsiku lokhali limene anazungulira mzindawu kasanu ndi kawiri.
Na sedmi dan se je pripetilo, da so vstali zgodaj, ob jutranjem svitanju in na isti način sedemkrat obkrožili mesto. Samo ta dan so mesto obkrožili sedemkrat.
16 Pomwe amazungulira kachisanu ndi chiwiri, ansembe akuliza malipenga mokweza, Yoswa analamulira anthu kuti “Fuwulani pakuti Yehova wakupatsani mzindawu!
Pripetilo se je sedmič, ko so duhovniki zatrobili s šofarji, da je Józue rekel ljudstvu: »Kričite, kajti Gospod vam je dal mesto.
17 Mzindawu ndi zonse zimene zili mʼmenemo muziwononge. Rahabe yekha, mayi wadama, ndi aliyense amene ali pamodzi naye mʼnyumba mwake asaphedwe, chifukwa anabisa anthu odzazonda, amene ife tinawatuma
Mesto bo prekleto Gospodu, celó to in vse, kar je v njem. Samo pocestnica Rahába bo živela, ona in vsi, ki so z njo v hiši, ker je skrila poslanca, ki smo ju poslali.
18 Koma musatenge kanthu kalikonse koyenera kuwonongedwa. Mukadzangotenga kanthu kalikonse koyenera kuwonongedwa, mudzaputa mavuto, misasa ya Israeli idzawonongedwa.
Vi pa se zagotovo zadržite pred prekleto stvarjo, da se ne bi naredili preklete, ko vzamete od preklete stvari in naredite tabor Izraelcev prekletstvo in ga vznemirite.
19 Zonse za siliva ndi golide, ziwiya zamkuwa ndi zachitsulo, ndi zake za Yehova ndipo ziyenera kukasungidwa mosungiramo chuma chake.”
Toda vse srebro, zlato in posode iz brona in železa so posvečeni Gospodu. Pridejo naj v Gospodovo zakladnico.«
20 Ansembe analiza malipenga. Anthu atamva kulira kwa malipenga, anafuwula kwambiri ndipo makoma a Yeriko anagwa. Choncho ankhondo anabwera ku mzinda uja nawulanda.
Tako je ljudstvo zakričalo, ko so duhovniki zatrobili s šofarji in pripetilo se je, ko je ljudstvo zaslišalo zvok šofarja in je ljudstvo zavpilo z velikim krikom, da je obzidje plosko padlo dol, tako da je ljudstvo odšlo gor v mesto, vsak mož naravnost pred seboj in zavzeli so mesto.
21 Iwo analowa mu mzindawo nawononga ndi lupanga chilichonse chamoyo kuyambira amuna, akazi, ana ndi akulu, ngʼombe, nkhosa ndi abulu.
Popolnoma so uničili vse, kar je bilo v mestu, tako moškega kakor žensko, mladega, starega, vola, ovco in osla, z ostrino meča.
22 Yoswa anawuza anthu awiri amene anakazonda dziko aja kuti, “Pitani ku nyumba ya mkazi wadama uja ndipo mukamutulutse iye pamodzi ndi onse amene ali naye ndipo mukabwere nawo kuno, munamulumbirira.”
Toda Józue je rekel dvema možema, ki sta ogledovala deželo: »Pojdita v hišo pocestnice in od tam privedita žensko in vse, kar ima, kakor sta ji prisegla.«
23 Choncho iwo anapita nakatenga Rahabe, abambo ake ndi amayi ake, abale ake ndi onse amene anali naye. Iwo anatulutsa banja lake lonse ndipo analiyika kuseri kwa msasa wa Aisraeli.
Mladeniča, ki sta bila oglednika, sta vstopila in privedla ven Rahábo, njenega očeta, njeno mater, njene brate in vse, kar je imela in ven sta privedla vse njeno sorodstvo in jih pustila zunaj tabora Izraelcev.
24 Kenaka iwo anawotcha mzinda wonse ndi chilichonse chimene chinali mʼmenemo, kupatulapo zasiliva ndi zagolide pamodzi ndi ziwiya zamkuwa ndi zachitsulo zimene anakaziyika mʼnyumba yosungiramo chuma cha Yehova.
Mesto pa so požgali z ognjem in vse, kar je bilo v njem. Samo srebro, zlato in posode iz brona in iz železa, so dali v zakladnico Gospodove hiše.
25 Koma Yoswa sanaphe Rahabe, mkazi wadamayo pamodzi ndi banja lake ndi onse amene anali naye, chifukwa anabisa anthu amene iye anawatuma kukazonda Yeriko. Zidzukulu zake za Rahabeyo zikukhala pakati pa Aisraeli mpaka lero.
Józue je rešil pocestnico Rahábo živo in družino njenega očeta in vse, kar je imela. V Izraelu prebiva do današnjega dne, ker je skrila poslanca, ki ju je Józue poslal, da ogledata Jeriho.
26 Pa nthawi imeneyo Yoswa anapereka chenjezo motemberera kuti, “Akhale wotembereredwa pamaso pa Yehova munthu amene adzamangenso mzinda uwu wa Yeriko: “Aliyense amene adzayike maziko ake, mwana wake wamwamuna wachisamba adzafa, aliyense womanga zipata zake mwana wake wamngʼono adzafa.”
Ob tistem času jih je Józue zaprisegel, rekoč: »Preklet bodi mož pred Gospodom, ki dvigne in pozida to mesto Jeriho. Njen temelj bo položil v svojem prvorojencu in v njegovem najmlajšem sinu bo postavil njena velika vrata.«
27 Motero Yehova anali ndi Yoswa, ndipo mbiri yake inafalikira dziko lonse.
Tako je bil Gospod z Józuetom in njegova slava je bila razglašena po vsej deželi.

< Yoswa 6 >