< Luka 2 >

1 Mʼmasiku amenewo Kaisara Augusto anapereka lamulo kuti kalembera achitike mʼdziko lonse la Aroma.
Now in those days, a decree went out from Caesar Augustus that all the world should be enrolled.
2 (Uyu ndi kalembera woyamba amene anachitika pamene Kureniyo anali bwanamkubwa wa Siriya).
This was the first enrollment made when Quirinius was governor of Syria.
3 Ndipo aliyense anapita ku mzinda wa kwawo kukalembetsa.
All went to enroll themselves, everyone to his own city.
4 Choncho Yosefe anachoka ku Nazareti ku Galileya kupita ku Yudeya, ku Betelehemu ku mudzi wa Davide, chifukwa anali wa banja ndi fuko la Davide.
Joseph also went up from Galilee, out of the city of Nazareth, into Judea, to David’s city, which is called Bethlehem, because he was of the house and family of David,
5 Iye anapita kumeneko kukalembetsa pamodzi ndi Mariya, amene anapalana naye ubwenzi kuti akwatirane ndipo anali woyembekezera.
to enroll himself with Miriam, who was pledged to be married to him as wife, being pregnant.
6 Ali kumeneko, nthawi inakwana yakuti mwana abadwe,
While they were there, the day had come for her to give birth.
7 ndipo anabereka mwana wake woyamba, wamwamuna. Iye anamukulunga mʼnsalu ndi kumuyika modyera ngʼombe, chifukwa kunalibe malo mʼnyumba ya alendo.
She gave birth to her firstborn son. She wrapped him in bands of cloth and laid him in a feeding trough, because there was no room for them in the inn.
8 Ndipo kunali abusa amene amakhala ku dera lomwelo, kuyangʼanira ziweto zawo usiku.
There were shepherds in the same country staying in the field, and keeping watch by night over their flock.
9 Mngelo wa Ambuye anaonekera kwa iwo ndipo ulemerero wa Ambuye unawala mowazungulira. Iwo anachita mantha.
Behold, an angel of the Lord stood by them, and the glory of the Lord shone around them, and they were terrified.
10 Koma mngeloyo anawawuza kuti, “Musachite mantha. Ine ndakubweretserani Uthenga Wabwino wachimwemwe chachikulu umene udzakhala wa anthu onse.
The angel said to them, “Don’t be afraid, for behold, I bring you good news of great joy which will be to all the people.
11 Lero mʼmudzi wa Davide wakubwadwirani Mpulumutsi; Iye ndi Khristu Ambuye.
For there is born to you today, in David’s city, a Savior, who is Messiah the Lord.
12 Ichi chidzakhala chizindikiro kwa inu: mukapeza mwana wakhanda wokutidwa ndi nsalu atagona modyera ngʼombe.”
This is the sign to you: you will find a baby wrapped in strips of cloth, lying in a feeding trough.”
13 Mwadzidzidzi gulu lalikulu la angelo linaonekera pamodzi ndi mngeloyo, kuyamika Mulungu ndi kumati,
Suddenly, there was with the angel a multitude of the heavenly army praising God and saying,
14 “Ulemerero kwa Mulungu mmwambamwamba, ndi mtendere kwa anthu pa dziko lapansi amene Iye akondwera nawo.”
“Glory to God in the highest, on earth peace, good will toward men.”
15 Angelowo atabwerera kumwamba, abusawo anati kwa wina ndi mnzake, “Tiyeni ku Betelehemu tikaone zinthu zomwe zachitika, zimene Ambuye atiwuza ife.”
When the angels went away from them into the sky, the shepherds said to one another, “Let’s go to Bethlehem, now, and see this thing that has happened, which the Lord has made known to us.”
16 Ndipo iwo anafulumira nyamuka nakapeza Mariya ndi Yosefe ndi mwana wakhanda, amene anagona modyera ngʼombe.
They came with haste and found both Miriam and Joseph, and the baby was lying in the feeding trough.
17 Pamene anamuona Iye, iwo anafotokoza zomwe anawuzidwa za mwanayo,
When they saw it, they publicized widely the saying which was spoken to them about this child.
18 ndipo onse amene anamva zimene abusawa ananena anadabwa.
All who heard it wondered at the things which were spoken to them by the shepherds.
19 Koma Mariya anasunga zonsezi mu mtima mwake ndi kumazilingalira.
But Miriam kept all these sayings, pondering them in her heart.
20 Abusa anabwerera, akulemekeza ndi kuyamika Mulungu chifukwa cha zonse anazimva ndi kuziona, zomwe zinali monga anawuzidwira ndi angelo aja.
The shepherds returned, glorifying and praising God for all the things that they had heard and seen, just as it was told them.
21 Pa tsiku lachisanu ndi chitatu, tsiku loti amuchite mdulidwe anamutcha Yesu, dzina limene mngelo anamupatsa asanabadwe.
When eight days were fulfilled for the circumcision of the child, his name was called Yeshua, which was given by the angel before he was conceived in the womb.
22 Nthawi yoyeretsedwa kwawo itatha, monga mwa lamulo la Mose, Yosefe ndi Mariya anapita naye ku Yerusalemu kukamupereka kwa Ambuye.
When the days of their purification according to the Torah of Moses were fulfilled, they brought him up to Jerusalem to present him to the Lord
23 (Monga mmene zinalembedwera mu lamulo la Ambuye kuti, “Muzikapereka kwa Ambuye mwana aliyense wamwamuna woyamba kubadwa”),
(as it is written in the Torah of the Lord, “Every male who opens the womb shall be called holy to the Lord”),
24 ndi kupereka nsembe posunga zimene zinanenedwa mulamulo la Ambuye: “Njiwa ziwiri kapena mawunda ankhunda awiri.”
and to offer a sacrifice according to that which is said in the Torah of the Lord, “A pair of turtledoves, or two young pigeons.”
25 Ndipo taonani, mu Yerusalemu munali munthu wotchedwa Simeoni, amene anali wolungama ndi wodzipereka. Iye ankadikira chitonthozo cha Israeli, ndipo Mzimu Woyera anali pa iye.
Behold, there was a man in Jerusalem whose name was Simeon. This man was righteous and devout, looking for the consolation of Israel, and the Holy Spirit was on him.
26 Mzimu Woyera anamuwululira kuti sadzafa asanaone Khristu wa Ambuye.
It had been revealed to him by the Holy Spirit that he should not see death before he had seen the Lord’s Messiah.
27 Motsogozedwa ndi Mzimu Woyera, iye anapita ku bwalo la Nyumba ya Mulungu. Makolo ake a Yesu atabwera naye kuti achite naye mwambo malingana ndi malamulo,
He came in the Spirit into the temple. When the parents brought in the child, Yeshua, that they might do concerning him according to the requirement of the Torah,
28 Simeoni anamunyamula mʼmanja mwake nayamika Mulungu, nati:
then he received him into his arms and blessed God, and said,
29 “Ambuye waulamuliro, monga munalonjeza, tsopano lolani kuti mtumiki wanu apite mu mtendere.
“Now you are releasing your servant, Master, according to your word, in peace;
30 Pakuti maso anga aona chipulumutso chanu,
for my eyes have seen your salvation,
31 chimene Inu munakonza pamaso pa anthu onse,
which you have prepared before the face of all peoples;
32 kuwala kowunikira anthu a mitundu ina ndi kwa ulemerero kwa anthu anu Aisraeli.”
a light for revelation to the nations, and the glory of your people Israel.”
33 Abambo ndi amayi a Mwanayo anadabwa chifukwa cha zimene zinanenedwa za Iye.
Joseph and his mother were marveling at the things which were spoken concerning him.
34 Kenaka Simeoni anawadalitsa ndipo anati kwa Mariya amayi ake: “Mwana uyu wakonzedwa kukhala kugwa ndi kudzuka kwa ambiri mu Israeli, ndi kukhala chizindikiro chimene adzayankhula motsutsana nacho,
Simeon blessed them, and said to Miriam, his mother, “Behold, this child is appointed for the falling and the rising of many in Israel, and for a sign which is spoken against.
35 kotero kuti malingaliro a mitima ya ambiri adzawululidwa. Ndipo lupanga lidzabaya moyo wakonso.”
Yes, a sword will pierce through your own soul, that the thoughts of many hearts may be revealed.”
36 Panalinso mneneri wamkazi, dzina lake Ana, mwana wa Fanuelo, wa fuko la Aseri. Anali wokalamba kwambiri; anakhala ndi mwamuna wake zaka zisanu ndi ziwiri atakwatiwa,
There was one Hannah, a prophetess, the daughter of Penuel, of the tribe of Asher (she was of a great age, having lived with a husband seven years from her virginity,
37 ndipo kenaka anakhala wamasiye mpaka pamene anali ndi zaka 84. Iye sanachoke mʼNyumba ya Mulungu koma ankapembedza usiku ndi usana, kusala kudya ndi kupemphera.
and she had been a widow for about eighty-four years), who didn’t depart from the temple, worshiping with fastings and petitions night and day.
38 Pa nthawiyo pamene ankapita kwa iwo, iye anayamika Mulungu ndi kuyankhula za Mwanayo kwa onse amene ankayembekezera chipulumutso cha Yerusalemu.
Coming up at that very hour, she gave thanks to the Lord, and spoke of him to all those who were looking for redemption in Jerusalem.
39 Yosefe ndi Mariya atachita zonse zimene zinkafunikira ndi lamulo la Ambuye, anabwerera ku Galileya ku mudzi wa Nazareti.
When they had accomplished all things that were according to the Torah of the Lord, they returned into Galilee, to their own city, Nazareth.
40 Ndipo Mwanayo anakula nakhala wamphamvu; Iye anadzazidwa ndi nzeru, ndipo chisomo cha Mulungu chinali pa Iye.
The child was growing, and was becoming strong in spirit, being filled with wisdom, and the grace of God was upon him.
41 Chaka chilichonse makolo ake ankapita ku Yerusalemu ku phwando la Paska.
His parents went every year to Jerusalem at the feast of the Passover.
42 Iye ali ndi zaka khumi ndi ziwiri, anapita ku phwando, monga mwa mwambo.
When he was twelve years old, they went up to Jerusalem according to the custom of the feast;
43 Phwando litatha, pamene makolo ake ankabwerera kwawo, mnyamata Yesu anatsalira ku Yerusalemu, koma iwo sanadziwe zimenezi.
and when they had fulfilled the days, as they were returning, the boy Yeshua stayed behind in Jerusalem. Joseph and his mother didn’t know it,
44 Poganiza kuti anali nawo mʼgulu lawo, anayenda tsiku limodzi. Kenaka anayamba kumufunafuna pakati pa abale awo ndi anzawo.
but supposing him to be in the company, they went a day’s journey; and they looked for him among their relatives and acquaintances.
45 Atalephera kumupeza, anabwerera ku Yerusalemu kukamufuna.
When they didn’t find him, they returned to Jerusalem, looking for him.
46 Patatha masiku atatu anamupeza ali mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu, atakhala pakati pa aphunzitsi, akumvetsera ndi kuwafunsa mafunso.
After three days they found him in the temple, sitting in the middle of the teachers, both listening to them and asking them questions.
47 Aliyense amene anamumva Iye anadabwa ndi chidziwitso chake ndi mayankho ake.
All who heard him were amazed at his understanding and his answers.
48 Makolo ake atamuona, anadabwa. Amayi ake anati kwa Iye, “Mwanawe, watichitira zimenezi chifukwa chiyani? Abambo ako ndi ine takhala tili ndi nkhawa kukufunafuna Iwe.”
When they saw him, they were astonished; and his mother said to him, “Son, why have you treated us this way? Behold, your father and I were anxiously looking for you.”
49 Iye anawafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mumandifunafuna? Kodi simukudziwa kuti ndikuyenera kukhala mʼnyumba ya Atate anga?”
He said to them, “Why were you looking for me? Didn’t you know that I must be in my Father’s house?”
50 Koma iwo sanazindikire chomwe Iye amatanthauza.
They didn’t understand the saying which he spoke to them.
51 Kenaka anapita nawo ku Nazareti ndipo anawamvera iwo. Koma amayi ake anasunga zinthu zonsezi mu mtima mwawo.
And he went down with them and came to Nazareth. He was subject to them, and his mother kept all these sayings in her heart.
52 Ndipo Yesu anakula mu nzeru, msinkhu ndi chisomo cha Mulungu ndi anthu.
And Yeshua increased in wisdom and stature, and in favor with God and men.

< Luka 2 >