< Mateyu 22 >

1 Yesu anayankhula nawonso mʼmafanizo, nati,
A IESUS kotin sapeng o pil karaseras ong irail masani:
2 “Ufumu wakumwamba uli ngati mfumu imene inakonzera phwando mwana wake wamwamuna.
Wein nanlang rasong nanmarki amen, me kamadipe na ol ni ran en a kapapaud.
3 Anatumiza antchito ake kwa amene anayitanidwa kuphwando koma anakana kubwera.
O a kadarala na ladu kan, pwen luke dong kamadip o, me kileledier akan; a re kang kodo.
4 “Kenaka anatumiza antchito ena nati, ‘Awuzeni oyitanidwa kuti phwando lakonzedwa: ndapha ngʼombe yayimuna ndi nyama zina zonenepa ndipo zonse zakonzedwa. Bwerani ku phwando laukwati.’
A pil kadarala akai ladu masani: Kaireki me kileledier akan: Kilang, i kaonopadar ai kamadip o: nai kau ol o man wi kan me kamelar, o karos nikier, ko dong kamadip en kapapaud!
5 “Koma iwo sanalabadire ndipo anachoka; wina anapita ku munda wake ndi wina ku malonda ake.
A irail sota insenoki, ap kowei, amen nan sap we, o amen ko ong dodok.
6 Ndipo otsalawo anagwira antchito ake, nawazunza ndi kuwapha.
A me tei kan saikidi a ladu kan kaloke o kame ir ala.
7 Mfumu inakwiya. Inatumiza asilikali ake ndipo anawononga opha anzawowo ndi kutentha mzinda wawo.
Nanmarki ap makara kidar, kadarala a saunpei kan, kamela me lolap oko o isikedar ar kanim o.
8 “Pamenepo anati kwa antchito ake, ‘Phwando laukwati lakonzedwa, koma amene ndinawayitana sanali oyenera.
A ap indang a ladu kan: Ari, kamadip onoper, a me kileledier akan sota war ong.
9 Pitani ku mphambano za misewu ndipo kayitaneni aliyense amene mukamupeze kuti abwere ku phwando.’
Komail ari kowei nan al akan, a karos me komail diar, en kalua dong kamadip o.
10 Pamenepo antchitowo anapita ku misewu nakasonkhanitsa anthu onse amene anakawapeza, abwino ndi oyipa omwe, ndipo nyumba ya madyerero inadzaza ndi oyitanidwa.
Ladu kan ap kola nani al akan, kapokon pena karos, me irail diaradar, me sued o me mau kan; kamadip ari tounlar.
11 “Koma pamene mfumu inabwera kudzaona oyitanidwawo, inaona munthu amene sanavale zovala zaukwati.
A nanmarki lao pwarado, en kilang toun kamadip, ap diaradar aramas amen, me sota a kapwat,
12 Inamufunsa kuti, ‘Bwenzi walowa bwanji muno wopanda zovala zaukwati?’ Munthuyo anakhala chete.
A ap masani ong i: Kompoke pai, iaduen om kak pedelong, pwe sota om kapwat? I ari sapaimokid.
13 “Pamenepo mfumuyo inawuza otumikira kuti, ‘Mʼmangeni manja ndi miyendo, ndipo muponyeni kunja, ku mdima kumene kudzakhale kulira ndi kukuta mano.’
Nanmarki ap masani ong papa kan: Saliedi i pa o nä akan, ale o kasapokela nan rotorot liki iei wasan maiei o teterok.
14 “Popeza oyitanidwa ndi ambiri koma osankhidwa ndi ochepa.”
Pwe me toto paekeredo, a me malaulau piladar.
15 Kenaka Afarisi anatuluka nakakonza njira zomupezera zifukwa Yesu mʼmawu ake.
Parisär ap pokon pena, kaparok pena duen ar pan kasapunga i sang a masan;
16 Anatumiza ophunzira awo kwa Iye pamodzi ndi Aherodia. Anati, “Aphunzitsi, tidziwa kuti ndinu wangwiro ndi kuti mumaphunzitsa mawu a Mulungu monga mwa choonadi. Simutekeseka ndi anthu, popeza simusamala kuti kodi ndi ndani?
Irail ap kadaralang i nairail tounpadak kan iangaki ladun Erodes kan, potoan ong: Saunpadak, se asa, ir me kotin melel, o kotin kawewe melel duen al en Kot o re sota kotin kupuroki meamen, pwe re sota kotin kasampwaleki sansal en aramas.
17 Tiwuzeni tsono maganizo anu ndi otani, kodi nʼkololedwa kupereka msonkho kwa Kaisara kapena ayi?”
Ari, re kotin masani ong kit kupur ar. Me pung, en nopwei ong nanmarki de so?
18 Koma Yesu podziwa maganizo awo oyipa anati, “Inu achiphamaso, bwanji mufuna kundipezera chifukwa?
A Iesus lao kotin mangi ar me suet, ap masani: Malaun komail, da me komail kasongesong kin ia?
19 Onetseni ndalama imene mumapereka msonkho.” Iwo anabweretsa dinari,
Kasale dong ia moni en nopwei! Irail ap potoan ong i denar eu.
20 ndipo anawafunsa kuti, “Kodi chithunzi ichi ndi malemba awa ndi za ndani?”
A kotin masani ong irail: Mom en is o inting wet?
21 Iwo anayankha kuti, “Ndi za Kaisara.” Pamenepo anawawuza kuti, “Perekani kwa Kaisara zake za Kaisara, ndi kwa Mulungu zake za Mulungu.”
Irail potoan ong i: En nanmarki, a i kotin masani ong irail: Ari, komail ki ong nanmarki, me nain nanmarki, o ong Kot, me sapwilim en Kot.
22 Atamva izi, anadabwa, ndipo anamusiya Iye, nachoka.
Irail lao rongadar met, rap puriamuiki o muei sang i, o koieilar.
23 Tsiku lomwelo Asaduki amene amati kulibe za kuukanso, anabwera kwa Iye ndi funso.
Ran ota Sadusär akai ko dong i, me kin inda, me dene me melar akan solar pan maureda, ap kalelapok re a.
24 Iwo anati, “Aphunzitsi, Mose anatiwuza kuti munthu akamwalira wosasiya ana, mʼbale wake akuyenera kukwatira mkazi wamasiyeyo kuti amuberekere ana mʼbale wakeyo.
Indada: Saunpadak, Moses masani, ma meamen melar o sota na seri, ri a ol en id paudeki a paud, pwen kaipwi ong ri a kadaudok a.
25 Tsopano panali abale asanu ndi awiri pakati pathu. Woyambayo anakwatira ndipo anamwalira, ndipo popeza analibe ana, mʼbale wake analowa chokolo.
Ari, pwin pirien eu mi re at, ol isimen. Meseni paudeki li amen, ap melar, a sota kadaudok a, ap kakaliki ong ri a ol a paud;
26 Izi zinachitikiranso mʼbale wa chiwiri ndi wachitatu mpaka wachisanu ndi chiwiri.
Pil dueta kariamen o kasilimen kokola lao kaisimen.
27 Pa mapeto pake mkaziyo anamwaliranso.
A ikmuri li o pil melar.
28 Tsopano, kodi akadzaukitsidwa adzakhala mkazi wa ndani mwa asanu ndi awiriwa popeza aliyense anamukwatirapo?”
Ari; ni en me melar akan ar pan iasada, a pan en is a paud ren me isimen, pwe irail karos me paudekidar i?
29 Yesu anayankha kuti, “Inu mukulakwitsa chifukwa simukudziwa malemba kapena mphamvu ya Mulungu.
A Iesus kotin sapeng masani ong irail: Komail meid sapung pwe komail so weweki kisin likau kan de mana en Kot.
30 Anthu akadzaukitsidwa, sadzakwatira kapena kukwatiwa; adzakhala ngati angelo kumwamba.
Pwe me mauredar akan solar pan papaud de kapapaud, pwe irail dueta tounlang en Kot akan, me mimi nanlang.
31 Koma za kuukitsidwa kwa akufa, kodi simunawerenge zimene Mulungu ananena kwa inu kuti,
Komail saik doropwe duen en melar akan ar pan maureda, me lolok ong komail sang ren Kot, me kotin masani:
32 ‘Ine ndine Mulungu wa Abrahamu, Mulungu wa Isake ndi Mulungu wa Yakobo?’ Iyeyo si Mulungu wa akufa koma wa amoyo.”
Ngai Kot en Apraam o en Isaak o en Iakop? A kaidin Kot en me melar akan, pwe en me maur akan.
33 Magulu a anthu atamva zimenezi, anazizwa ndi chiphunzitso chake.
A pokon o lao rongadar met, irail ap puriamuiki a padak.
34 Pakumva kuti Yesu anawakhalitsa chete Asaduki, Afarisi anasonkhana pamodzi.
A Parisär akan lao rongadar, me a kotin kadukiedier Sadusär akan, ap pokon pena.
35 Mmodzi wa iwo, katswiri wa malamulo anamuyesa Iye ndi funso ndipo anati,
Amen irail, saunkawewe men, kasongesong i potoan ong:
36 “Aphunzitsi, kodi lamulo lalikulu koposa mu malamulo ndi liti?”
Saunpadak, kusoned da me lapalap nan kapung o?
37 Yesu anayankha kuti, “Uzikonda Yehova Mulungu wako ndi mtima wako wonse ndi moyo wako wonse ndi nzeru zako zonse.
A Iesus kotin masani ong i: Koe en pokeki ong Kot om Kaun mongiong om unsok, o ngen om unsok, o om lamelam unsok.
38 Ili ndi lamulo loyamba ndi loposa onse.
Iei met me moa en kusoned akan.
39 Ndipo lachiwiri ndi lofanana nalo: ‘Konda mnansi wako monga iwe mwini.’
O me kariau me dueta: Koe en pok ong men imp om dueta ong pein koe.
40 Malamulo onse ndi aneneri zakhazikika pa malamulo awiriwa.”
Kusoned riau met me audepan kapung o saukop akan.
41 Afarisi atasonkhana pamodzi, Yesu anawafunsa kuti,
Ni en Parisär akan ar momod pena, Iesus ap kotin kainoma re’rail.
42 “Kodi mukuganiza bwanji za Khristu? Ndi Mwana wa ndani?” Iwo anayankha kuti, “Mwana wa Davide.”
Masani: Da me komail lamelame duen Kristus, nain is i? Re potoan ong: Sapwilim en Dawid.
43 Iye anawawuza kuti, “Nanga zikutheka bwanji kuti Davide poyankhula mwa Mzimu Woyera amatchula Iye ‘Ambuye?’ Pakuti akuti,
A kotin masani ong irail: A iaduen da me Dawid kaadaneki i Kaun reng Ngen ni a masani:
44 “Ambuye anati kwa Ambuye wanga: ‘Khala pa dzanja langa lamanja mpaka ndiyike adani ako pansi pa mapazi ako.’
Kaun o kotin masani ong ai Kaun, mondi ong ni pali maun i, lao I pan wia kida om imwintiti utipan nä om?
45 Ngati tsono Davide amamutchula ‘Ambuye,’ zingatheke bwanji kukhala mwana wake?”
A iaduen, ma Dawid kaadaneki i Kaun, a pil pan kak na ol?
46 Panalibe wina anatha kuyankha, ndipo kuchokera pamenepo, panalibe wina anayerekeza kumufunsa funso.
A sota amen, me kak sapengki i meakot, o solar me idok meakot re a kokolata.

< Mateyu 22 >