< Miyambo 29 >

1 Munthu amene amawumitsabe khosi lake atadzudzulidwa kwambiri, adzawonongeka mwadzidzidzi popanda chomuchiritsa.
He, that being often reproved hardeneth his neck, shall suddenly be destroyed, and that without remedy.
2 Anthu olungama akamalamulira mʼdziko anthu amakondwa, koma ngati dziko lilamulidwa ndi anthu oyipa mtima anthu amadandaula.
When the righteous are in authority, the people rejoice: but when the wicked beareth rule, the people mourn.
3 Munthu amene amakonda nzeru amasangalatsa abambo ake, koma woyenda ndi akazi achiwerewere amasakaza chuma chake.
He that loveth wisdom rejoiceth his father: but he that keepeth company with harlots spendeth his substance.
4 Mfumu imalimbitsa dziko poweruza mwachilungamo, koma mfumu imene imawumiriza anthu kuti ayipatse mphatso imawononga dziko.
The king by judgment establisheth the land: but he that exacteth gifts overthroweth it.
5 Munthu woshashalika mnzake, akudziyalira ukonde mapazi ake.
A man that flattereth his neighbour spreadeth a net for his feet.
6 Munthu woyipa amakodwa ndi machimo ake, koma wochita chilungamo amayimba lokoma.
In the transgression of an evil man there is a snare: but the righteous doth sing and rejoice.
7 Munthu wolungama amasamalira anthu osauka, koma woyipa salabadira zimenezi.
The righteous considereth the cause of the poor: but the wicked regardeth not to know it.
8 Anthu onyoza atha kuwutsa ziwawa mu mzinda, koma anthu anzeru amaletsa ukali.
Scornful men bring a city into a snare: but wise men turn away wrath.
9 Ngati munthu wanzeru atsutsana ndi chitsiru, chitsirucho chimachita phokoso ndi kumangoseka ndipo sipakhala mtendere.
If a wise man contendeth with a foolish man, whether he rageth or laugheth, there is no rest.
10 Anthu okhetsa magazi amadana ndi munthu wangwiro koma anthu olungama amasamalira moyo wake.
The bloodthirsty hate the upright: but the just seek his soul.
11 Munthu wopusa amaonetsa mkwiyo wake, koma munthu wanzeru amadzigwira.
A fool uttereth all his mind: but a wise man keepeth it in till afterwards.
12 Ngati wolamulira amvera zabodza, akuluakulu ake onse adzakhala oyipa.
If a ruler hearkeneth to lies, all his servants are wicked.
13 Munthu wosauka ndi munthu wopondereza anzake amafanana pa kuti: Yehova ndiye anawapatsa maso onsewa.
The poor and the deceitful man meet together: the LORD giveth light to both their eyes.
14 Ngati mfumu iweruza osauka moyenera, mpando wake waufumu udzakhazikika nthawi zonse.
The king that faithfully judgeth the poor, his throne shall be established for ever.
15 Ndodo ndi chidzudzulo zimapatsa nzeru koma mwana womulekerera amachititsa amayi ake manyazi.
The rod and reproof give wisdom: but a child left to himself bringeth his mother to shame.
16 Oyipa akamalamulira zoyipa zimachuluka, koma anthu olungama adzaona kugwa kwa anthu oyipawo.
When the wicked are multiplied, transgression increaseth: but the righteous shall see their fall.
17 Umulange mwana wako ndipo adzakupatsa mtendere ndi kusangalatsa mtima wako.
Correct thy son, and he shall give thee rest; yea, he shall give delight to thy soul.
18 Ngati uthenga wochokera kwa Yehova supezeka anthu amangochita zofuna zawo; koma wodala ndi amene amasunga malamulo.
Where there is no vision, the people perish: but he that keepeth the law, happy is he.
19 Munthu wantchito sangalangizidwe ndi mawu okha basi; ngakhale awamvetse mawuwo sadzatha kuchitapo kanthu.
A servant will not be corrected by words: for though he understandeth he will not answer.
20 Ngakhale munthu wa uchitsiru nʼkuti ndiponi popeza chikhulupiriro chilipo kuposa munthu wodziyesa yekha kuti ndi wanzeru poyankhula.
Seest thou a man that is hasty in his words? there is more hope of a fool than of him.
21 Ngati munthu asasatitsa wantchito wake kuyambira ali mwana, potsirizira adzapeza kuti wantchitoyo wasanduka mlowachuma wake.
He that delicately bringeth up his servant from a child shall have him at length become his son.
22 Munthu wamkwiyo amayambitsa mikangano, ndipo munthu waukali amachita zolakwa zambiri.
An angry man stirreth up strife, and a furious man aboundeth in transgression.
23 Kunyada kwa munthu kudzamutsitsa, koma munthu wodzichepetsa amalandira ulemu.
A man’s pride shall bring him low: but honour shall uphold the humble in spirit.
24 Woyenda ndi munthu wakuba ndi mdani wa moyo wake womwe; amalumbira koma osawulula kanthu.
Whoever is partner with a thief hateth his own soul: he heareth cursing, and revealeth it not.
25 Kuopa munthu kudzakhala ngati msampha, koma aliyense amene amadalira Yehova adzatetezedwa.
The fear of man bringeth a snare: but he who putteth his trust in the LORD shall be safe.
26 Anthu ambiri amafunitsitsa kuti wolamulira awakomere mtima, koma munthu amaweruzidwa mwachilungamo ndi thandizo la Yehova basi.
Many seek the ruler’s favour; but every man’s judgment cometh from the LORD.
27 Anthu olungama amanyansidwa ndi anthu achinyengo; koma anthu oyipa amanyansidwa ndi anthu a mtima wowongoka.
An unjust man is an abomination to the just: and he that is upright in the way is abomination to the wicked.

< Miyambo 29 >