< Masalimo 118 >

1 Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.
Wysławiajcie PANA, bo jest dobry, bo jego miłosierdzie [trwa] na wieki.
2 Israeli anene kuti: “Chikondi chake ndi chosatha.”
Niech powie teraz Izrael, że jego miłosierdzie [trwa] na wieki.
3 Banja la Aaroni linene kuti, “Chikondi chake ndi chosatha.”
Niech powie teraz dom Aarona, że jego miłosierdzie [trwa] na wieki.
4 Iwo amene amaopa Yehova anene kuti: “Chikondi chake ndi chosatha.”
Niech powiedzą teraz ci, którzy się boją PANA, że jego miłosierdzie [trwa] na wieki.
5 Ndili mʼmasautso anga ndinalirira Yehova, ndipo Iye anayankha pondichotsa mʼmasautsowo.
Wzywałem PANA w ucisku; PAN mnie wysłuchał i postawił mnie na miejscu przestronnym.
6 Yehova ali nane; sindidzachita mantha. Munthu angandichite chiyani?
PAN jest ze mną, nie będę się bał; cóż może mi uczynić człowiek?
7 Yehova ali nane; Iye ndiye thandizo langa. Ndidzayangʼana adani anga mwachipambano.
PAN jest ze mną wśród tych, którzy mi pomagają, więc zobaczę [pomstę] nad tymi, którzy mnie nienawidzą.
8 Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova kusiyana ndi kudalira munthu.
Lepiej ufać PANU, niż polegać na człowieku.
9 Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova kusiyana ndi kudalira mafumu.
Lepiej ufać PANU, niż polegać na władcach.
10 Anthu a mitundu yonse anandizinga, koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
Wszystkie narody mnie otoczyły, ale w imię PANA wytępiłem je.
11 Anandizinga mbali zonse, koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
Otoczyły mnie, tak, otoczyły mnie, ale w imię PANA wytępiłem je.
12 Anandizinga ngati njuchi, koma anatha msanga ngati moto wapaminga; mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
Otoczyły mnie jak pszczoły, ale zgasły [jak] ogień z cierni, bo w imię PANA wytępiłem je.
13 Anandikankha uku ndi uko ndipo ndinali pafupi kugwa, koma Yehova anandithandiza.
Pchnąłeś mnie silnie, abym upadł, ale PAN mi pomógł.
14 Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga; Iye wakhala chipulumutso changa.
PAN [jest] moją siłą i pieśnią, on stał się moim zbawieniem.
15 Mfuwu wachimwemwe ndi chipambano ukumveka mʼmatenti a anthu olungama mtima kuti: “Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!
Głos radości i zbawienia w namiotach sprawiedliwych: Prawica PANA działa potężnie;
16 Dzanja lamanja la Yehova latukulidwa mmwamba Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!”
Prawica PANA jest wywyższona, prawica PANA działa potężnie.
17 Sindidzafa koma ndidzakhala ndi moyo ndipo ndidzalalika za ntchito ya Yehova.
Nie umrę, lecz będę żył i opowiadał dzieła PANA.
18 Yehova wandilanga koopsa, koma sanandipereke ku imfa.
PAN ukarał mnie surowo, ale nie wydał mnie na śmierć.
19 Tsekulireni zipata zachilungamo, kuti ndifike kudzayamika Yehova.
Otwórzcie mi bramy sprawiedliwości, a wejdę w nie i będę wysławiał PANA.
20 Ichi ndicho chipata cha Yehova chimene olungama mtima okha adzalowerapo.
To jest brama PANA, którą wchodzą sprawiedliwi.
21 Ndidzakuyamikani chifukwa Inu munandiyankha; mwakhala chipulumutso changa.
Będę cię wysławiać, bo mnie wysłuchałeś i stałeś się moim zbawieniem.
22 Mwala umene amisiri omanga nyumba anawukana wasanduka wapangodya;
Kamień, [który] odrzucili budujący, stał się kamieniem węgielnym.
23 Yehova ndiye wachita zimenezi ndipo nʼzodabwitsa pamaso pathu.
PAN to sprawił i jest to cudowne w naszych oczach.
24 Lero ndiye tsiku limene Yehova walipanga; tiyeni tikondwere ndi kusangalala nalo.
Oto dzień, który PAN uczynił, weselmy się i radujmy się w nim.
25 Inu Yehova, tipulumutseni; Yehova, tipambanitseni.
Proszę, PANIE, wybaw teraz; proszę, PANIE, daj pomyślność.
26 Wodala amene akubwera mʼdzina la Yehova. Tikukudalitsani kuchokera ku nyumba ya Yehova.
Błogosławiony, który przychodzi w imię PANA; błogosławimy wam z domu PANA.
27 Yehova ndi Mulungu, ndipo kuwala kwake kwatiwunikira Ife. Lowani nawo pa mʼdipiti wa ku chikondwerero mutanyamula nthambi mʼdzanja lanu, mpaka ku nyanga za guwa.
Bóg jest PANEM, on nas oświecił; przywiążcie baranki powrozami aż do rogów ołtarza.
28 Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakuyamikani; Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakukwezani.
Ty jesteś moim Bogiem, będę cię wysławiać; mój Boże, będę cię wywyższać.
29 Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.
Wysławiajcie PANA, bo [jest] dobry, bo jego miłosierdzie [trwa] na wieki.

< Masalimo 118 >