< Masalimo 119 >

1 Odala ndi amene moyo wawo ulibe cholakwa, amene amayenda monga mwa malamulo a Yehova.
Nagasat dagiti awan pakababalawan dagiti wagasna, isuda nga agtultulnog iti linteg ni Yahweh.
2 Odala ndi amene amasunga malamulo ake, amene amafunafuna Iyeyo ndi mtima wawo wonse.
Nagasat dagiti mangsalsalimetmet kadagiti napudno a bilinna, isuda a mangsapsapul kenkuana iti amin a pusoda.
3 Sachita cholakwa chilichonse; amayenda mʼnjira zake.
Saanda nga agar-aramid iti saan a nasaya-at; magmagnada kadagiti wagasna.
4 Inu mwapereka malangizo ndipo ayenera kutsatidwa kwathunthu.
Binilinnakami a mangsalimetmet kadagiti pagannurotam tapno surotenmi a naimbag dagitoy.
5 Aa! Ndikanakonda njira zanga zikanakhala zokhazikika pa kumvera zophunzitsa zanu!
O, tapno maibangonakto a sititibker iti panangaramid kadagiti alagadem!
6 Pamenepo ine sindikanachititsidwa manyazi, poganizira malamulo anu onse.
Ket saanakto a maibabain no panunotek ti maipapan kadagiti amin a bilbilinmo.
7 Ndidzakutamandani ndi mtima wolungama, pamene ndikuphunzira malamulo anu olungama.
Agyamanakto kenka nga addaan iti napudno a puso inton masursurok dagiti nalinteg a bilinmo.
8 Ndidzamvera zophunzitsa zanu; musanditaye kwathunthu.
Tungpalekto dagiti alagadem; saannak a panawan nga agmaymaysa. BETH
9 Kodi mnyamata angathe bwanji kuyeretsa mayendedwe ake? Akawasamala potsata mawu anu.
Kasano a pagtalinaeden ti maysa nga agtutubo a nadalus ti dalanna? Babaen iti panagtulnog iti saom.
10 Ndimakufunafunani ndi mtima wanga wonse; musalole kuti ndisochere kuchoka pa malamulo anu.
Iti amin a pusok ket sapsapulenka; Saanmo nga itulok a maiyaw-awanak manipud kadagiti bilbilinmo.
11 Ndasunga mawu anu mu mtima mwanga kuti ndisakuchimwireni.
Indulinko ti saom ditoy pusok tapno saanak nga agbasol kenka,
12 Mutamandike Inu Yehova; phunzitseni malamulo anu.
Madaydayawka, O Yahweh; isurom kaniak dagiti alagadem.
13 Ndi milomo yanga ndimafotokoza malamulo anu onse amene amachokera pakamwa panu.
Babaen iti ngiwatko inwaragawagko amin dagiti nalinteg a pangngeddeng nga inka impakaammo.
14 Ndimakondwera potsatira malamulo anu monga momwe munthu amakondwera akakhala ndi chuma chambiri.
Ad-adda nga agrag-oak iti wagas dagiti bilbilinmo iti tulagmo ngem iti amin a kinabaknang.
15 Ndimalingalira malangizo anu ndipo ndimaganizira njira zanu.
Utobek dagiti pagannurotam ken ipangagko dagiti wagasmo.
16 Ndimakondwera ndi malamulo anu; sindidzayiwala konse mawu anu.
Agragsakak kadagiti alagadem; Saankonto a malipatan ti saom. GIMEL
17 Chitirani zokoma mtumiki wanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; kuti tsono ndisunge mawu anu.
Paraburam kadi ti adipenmo tapno agbiagak ken matungpalko ti saom.
18 Tsekulani maso anga kuti ndithe kuona zinthu zodabwitsa mʼmalamulo anu.
Lukatam dagiti matak tapno makitak dagiti nakakaskasdaaw a banbanag iti lintegmo.
19 Ine ndine mlendo pa dziko lapansi; musandibisire malamulo anu.
Maysaak a ganggannaet iti daga; saanmo nga illemmeng dagiti bilbilinmo manipud kaniak.
20 Moyo wanga wafowoka polakalaka malamulo anu nthawi zonse.
Naburakda dagiti tarigagayko iti panangkalkalikagom a mangammo kadagiti nalinteg a pangngeddengmo iti amin a tiempo.
21 Inu mumadzudzula onyada, otembereredwa, amene achoka pa malamulo anu.
Babalawem dagiti natangsit, isuda a nailunod, isuda a simmiasi manipud kadagiti bilinmo.
22 Mundichotsere chitonzo ndi mnyozo pakuti ndimasunga malamulo anu.
Isalakannak manipud iti pannakaibabain ken pannakaumsi, gapu ta nagtulnogak kadagiti bilbilinmo iti tulagmo.
23 Ngakhale mafumu akhale pamodzi kundinyoza, mtumiki wanu adzalingalirabe zophunzitsa zanu.
Uray pay no pagpanggepandak iti dakes ken padaksendak dagiti mangiturturay, ut-utuben daytoy adipenmo dagiti alagadem.
24 Malamulo anu amandikondweretsa; ndiwo amene amandilangiza.
Pakaragsakak dagiti bilbilinmo iti tulagmo, ket isuda dagiti mamagbaga kaniak. DALETH
25 Moyo wanga wakangamira fumbi; tsitsimutseni molingana ndi mawu anu.
Ti biagko ket nakakapet iti tapok! Ikkannak iti biag babaen iti saom.
26 Ndinafotokoza njira zanga ndipo Inu munandiyankha; phunzitseni malamulo anu.
Imbagak kenka dagiti dalanko, ket sinungbatannak; isurom kaniak dagiti alagadem.
27 Mundidziwitse chiphunzitso cha malangizo anu; pamenepo ndidzalingalira zodabwitsa zanu.
Ipakaawatmo kaniak dagiti wagas dagiti pagannurotam, tapno mabalinko nga utuben dagiti nakakaskasdaaw a sursusrom.
28 Moyo wanga wafowoka ndi chisoni; limbikitseni monga mwa mawu anu.
Nalapunosak iti panagladingit! Papigsaennak babaen iti saom.
29 Mundichotse mʼnjira zachinyengo; mundikomere mtima pondiphunzitsa malamulo anu.
Iyadayom kaniak ti dalan ti kinamanangallilaw; sipaparabur nga isurom kaniak ti lintegmo.
30 Ndasankha njira ya choonadi; ndayika malamulo anu pa mtima panga.
Pinilik ti dalan ti kinapudno; kankanayonko a tinungtungpal ti nalinteg a bilinmo.
31 Ndagwiritsitsa umboni wanu, Inu Yehova; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
Kumpetak kadagiti bilbilinmo iti tulagmo; O Yahweh, saanmo koma nga itulok a maibabainak.
32 Ndimathamanga mʼnjira ya malamulo anu, pakuti Inu mwamasula mtima wanga.
Agtarayak iti dalan dagiti bilbilinmo, ta padpadakkelem ti pusok a mangaramid iti dayta. HE
33 Yehova, phunzitseni kutsatira zophunzitsa zanu; ndipo ndidzazisunga mpaka kumapeto.
Isurom kaniak, O Yahweh, ti wagas dagiti alagadem, ket tungpalek dagitoy agingga iti panungpalan.
34 Mundipatse mtima womvetsa zinthu ndipo ndidzasunga malamulo anu ndi kuwamvera ndi mtima wanga wonse.
Ikkannak iti pannakaawat, ket tungpalek ti lintegmo; aramidekto daytoy iti amin a pusok.
35 Munditsogolere mʼnjira ya malamulo anu, pakuti mʼmenemo ndimapezamo chikondwerero changa.
Iwanwannak iti dalan dagiti bilbilinmo, ta pagragsakak ti magna iti daytoy.
36 Tembenuzani mtima wanga kuti uzikonda malamulo anu, osati chuma.
Iturongmo ti pusok kadagiti bilbilinmo iti tulagmo ken iyadayum manipud iti kinaagum.
37 Tembenuzani maso anga kuchoka ku zinthu zachabechabe; sungani moyo wanga monga mwa mawu anu.
Ilisim dagiti matak iti panangmingming kadagiti awan serserbina a banbanag; paregtaennak kadagiti wagasmo.
38 Kwaniritsani lonjezo lanu kwa mtumiki wanu, kuti Inu muopedwe.
Ipatungpalmo iti adipenmo ti inkarim nga inaramiden kadagiti agdaydayaw kenka.
39 Mundichotsere chipongwe chimene ndikuchiopa, pakuti malamulo anu ndi abwino.
Ikkatem ti pagbutbutngak a pakaibabainan, ta nasayaat dagiti nalinteg a pangngeddengmo.
40 Taonani, ndimalakalakatu malangizo anu! Sungani moyo wanga mʼchilungamo chanu.
Adtoy, kalkalikagumak dagiti pagannurotam; pagtalinaedennak a sibibiag babaen iti nalinteg a panangwayawayam. VAV.
41 Chikondi chanu chosasinthika chibwere kwa ine, Inu Yehova, chipulumutso chanu monga mwa lonjezo lanu;
O Yahweh, ipaaymo kaniak ti saan nga agbalbaliw nga ayatmo— ti panangisalakanmo, sigun iti karim,
42 ndipo ndidzayankha amene amandinyoza, popeza ndimadalira mawu anu.
Ket addanto isungbatko iti manglalais kaniak, ta agtalekak iti saom.
43 Musakwatule mawu a choonadi mʼkamwa mwanga, pakuti ndakhazikitsa chiyembekezo changa mʼmalamulo anu.
Saanmo nga ikkaten ti sao ti kinapudno iti ngiwatko, gapu ta inurayko dagiti nalinteg a bilbilinmo.
44 Ndidzasunga malamulo anu nthawi zonse, ku nthawi za nthawi.
Agtultuloyto a tungpalek ti lintegmo, iti agnanayon nga awan patinggana.
45 Ndidzayendayenda mwaufulu, chifukwa ndinafunafuna malangizo anu.
Magnaak a sitatalged, ta sinapulko dagiti pamagbagam.
46 Ndidzayankhula za umboni wanu pamaso pa mfumu ndipo sindidzachititsidwa manyazi,
Saritaek dagiti napudno a bilinmo iti sangoanan dagiti ar-ari ket saanak a mabain.
47 popeza ndimakondwera ndi malamulo anu chifukwa ndimawakonda.
Pakaragsakak dagiti bilbilinmo, nga ay-ayatek unay.
48 Ndikweza manja anga ku malamulo anu, ku malamulo amene ndimawakonda, ndipo ndimalingalira malangizo anu.
Itag-ayko dagiti imak kadagiti bilbilinmo, nga ay-ayatek; Utubek dagiti alagadem. ZAYIN.
49 Kumbukirani mawu anu kwa mtumiki wanu, popeza mwandipatsa chiyembekezo.
Laglagipem ti karim iti adipenmo gapu ta inikkannak iti namnama.
50 Chitonthozo changa pa masautso anga ndi ichi: lonjezo lanu limasunga moyo wanga.
Daytoy ti liwliwak iti pannakaparigatko: a pinagtalinaednak a sibibiag ti karim.
51 Odzikuza amandinyoza popanda chowaletsa, koma sindichoka pa malamulo anu.
Inuyawdak dagiti natangsit, ngem saanak a timmallikod iti lintegmo.
52 Ndimakumbukira malamulo anu Yehova akalekale, ndipo mwa iwo ndimapeza chitonthozo.
Napanunotko ti maipanggep kadagiti nalinteg a pangngeddengmo manipud idi un-unana a tiempo, O Yahweh, ket maliwliwaak.
53 Ndayipidwa kwambiri chifukwa cha oyipa amene ataya malamulo anu.
Simged ti pungtotko gapu kadagiti nadangkes a manglaklaksid iti lintegmo.
54 Zophunzitsa zanu ndi mitu ya nyimbo yanga kulikonse kumene ndigonako.
Dagiti alagadem ti nagbalin a kankantak iti balay a pagnanaedak a saan nga agpaut.
55 Usiku ndimakumbukira dzina lanu Yehova, ndipo ndidzasunga malamulo anu.
Panpanunotek ti maipanggep iti naganmo bayat iti rabii, O Yahweh, ken tungtungpalek ti lintegmo.
56 Ichi ndicho ndakhala ndikuchita: ndimasunga malangizo anu.
Daytoy ti kanayon nga inar-aramidko gapu ta tinungpalko dagiti pagannurotam. HETH.
57 Yehova, Inu ndiye gawo langa; ndalonjeza kumvera mawu anu.
Ni Yahweh iti bingayko; inkeddengko nga aramidek dagiti sasaom.
58 Ndimafunafuna nkhope yanu ndi mtima wanga wonse; mundikomere mtima monga mwa lonjezo lanu.
Sipapasnekko a dawdawaten ti paraburmo iti amin a pusok; maasika kaniak, kas inkarim iti saom.
59 Ndinalingalira za njira zanga ndipo ndatembenuza mayendedwe anga kutsatira umboni wanu.
Inutobko dagiti wagasko ket inturongko dagiti sakak kadagiti bilbilinmo iti tulagmo.
60 Ndidzafulumira ndipo sindidzazengereza kumvera malamulo anu.
Agdardarasak ket saanko nga itantan a tungpalen dagiti bilbilinmo.
61 Ngakhale oyipa andimange ndi zingwe, sindidzayiwala lamulo lanu.
Siniluandak dagiti tali dagiti nadangkes; saanko a nalipatan ti lintegmo.
62 Ndimadzuka pakati pa usiku kuyamika Inu chifukwa cha malamulo anu olungama.
Iti tengnga ti rabii bumangonak nga agyaman kenka gapu kadagiti nalinteg a pangngeddengmo.
63 Ine ndine bwenzi la onse amene amakukondani, kwa onse amene amatsatira malangizo anu.
Kaduadak dagiti amin a mangdaydayaw kenka, kadagiti amin nga agtungtungpal kadagiti pagannurotam.
64 Dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chanu chosasinthika, phunzitseni malamulo anu.
Ti daga, O Yahweh, ket napnoan iti kinapudnom iti katulagam; isurom kaniak dagiti alagadem. TETH.
65 Inu Yehova, chitirani chabwino mtumiki wanu molingana ndi mawu anu.
Nangaramidka kadagiti nasayaat iti adipenmo, O Yahweh, babaen iti saom.
66 Phunzitseni nzeru ndi chiweruzo chabwino, pakuti ndimakhulupirira malamulo anu.
Isurom kaniak ti umno a pannakaammo ken pannakaawat, gapu ta namatiak kadagiti bilbilinmo.
67 Ndisanayambe kuzunzika ndinasochera, koma tsopano ndimamvera mawu anu.
Naiyaw-awanak idi sakbay a naparigatak, ngem ita tungtungpalek ti saom.
68 Inu ndinu abwino ndipo zimene mumachita ndi zabwino; phunzitseni malamulo anu.
Nagimbagka, ket sika ti mangar-aramid iti naimbag; isurom kaniak dagiti alagadem.
69 Ngakhale odzikuza andipaka mabodza, ine ndimasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.
Pinulagidandak dagiti napalangguad kadagiti inuulbod, ngem tungtungpalek dagiti pagannurotam iti amin a pusok.
70 Mitima yawo ndi yowuma ndi yosakhudzidwa, koma ine ndimakondwera ndi malamulo anu.
Timmangken dagiti pusoda, ngem pagragsakak iti lintegmo.
71 Ndi bwino kuti ndinasautsidwa kuti ndithe kuphunzira malamulo anu.
Pagsayaatak a nagsagabaak tapno masursurok dagiti alagadem.
72 Lamulo lochokera mʼkamwa mwanu limandikomera kwambiri kuposa ndalama zambirimbiri za siliva ndi golide.
Napatpateg kaniak ti pamagbaga nga agtaud iti ngiwatmo ngem kadagiti rinibribu a pidaso iti balitok ken pirak. YOD.
73 Manja anu anandilenga ndi kundiwumba; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ndiphunzire malamulo anu.
Inaramid ken binukelnak dagiti imam; ikkannak iti pannakaawat tapno masursurok dagiti bilbilinmo.
74 Iwo amene amakuopani akondwere akandiona, chifukwa chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Maragsakanto dagiti mangdaydayaw kenka inton makitadak gapu ta nakasarakak ti namnama iti saom.
75 Ine ndikudziwa, Inu Yehova, kuti malamulo anu ndi olungama ndipo mwandizunza chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
Ammok, O Yahweh, a dagiti bilbilinmo ket nalinteg, ken pinarigatannak gapu iti kinapudno,
76 Chikondi chanu chosasinthika chikhale chitonthozo changa, molingana ndi lonjezo lanu kwa mtumiki wanu.
Liwliwaennak koma ti kinapudnom iti tulagmo, kas inkarim iti adipenmo.
77 Chifundo chanu chindifikire kuti ndikhale ndi moyo, popeza malamulo anu ndiye chikondwerero changa.
Kaasiannak tapno agbiagak, ta pakaragsakak ti lintegmo.
78 Odzikuza achititsidwe manyazi chifukwa cha kundilakwira popanda chifukwa; koma ine ndidzalingalira malangizo anu.
Maibabain koma dagiti natangsit, gapu ta pinadpadakesdak; ngem utubek dagiti pagannurotam.
79 Iwo amene amakuopani atembenukire kwa ine, iwo amene amamvetsetsa umboni wanu.
Agsubli koma kaniak dagiti agdaydayaw kenka, dagiti makaammo kadagiti bilbilinmo iti tulagmo.
80 Mtima wanga ukhale wopanda cholakwa pa chiphunzitso chanu kuti ndisachititsidwe manyazi.
Agbalin koma ti pusok nga awan mulitna no maipapan kadagiti alagadem tapno saanak a maibabain. KAPH.
81 Moyo wanga wafowoka ndi kufunafuna chipulumutso chanu, koma chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Aglusdoyak gapu ti panangkalkalikagumko nga ispalennak! Addaanak iti namnama iti saom.
82 Maso anga alefuka pofunafuna lonjezo lanu; Ine ndikuti, “Kodi mudzanditonthoza liti?”
Matektekan unay dagiti matak a makita ti karim; kaanonak a liwliwaen?
83 Ngakhale ndili ngati thumba lachikopa la vinyo pa utsi sindiyiwala zophunzitsa zanu.
Ta nagbalinak a kasla supot ti arak a maas-asukan; saanko a malipatan dagiti alagadem.
84 Kodi mtumiki wanu ayenera kudikira mpaka liti? Kodi mudzawalanga liti amene amandizunza?
Kasano kabayag nga ibturan ti adipenmo daytoy; kaanonto nga ukomem dagiti a mangparparigat kaniak?
85 Anthu osalabadira za Mulungu, odzikuza amandikumbira dzenje motsutsana ndi malamulo anu.
Nagkali dagiti natangsit kadagiti abut a para kaniak, salsalungasingenda ti lintegmo.
86 Malamulo anu onse ndi odalirika; thandizeni, pakuti anthu akundizunza popanda chifukwa.
Mapagtalkan dagiti amin a bilbilinmo; sibibiddut nga idaddadanesdak dagiti tattao; tulongannak.
87 Iwo anatsala pangʼono kundichotsa pa dziko lapansi koma sindinataye malangizo anu.
Dandanida kinittel ti biagko ditoy rabaw iti daga, ngem saanko nga ilaklaksid dagiti pagannurotam.
88 Sungani moyo wanga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo ndidzamvera umboni wa pakamwa panu.
Pagtalinaedennak a sibibiag, kas inkari iti kinapudnom iti katulagam, tapno matungpalko dagiti bilbilinmo iti tulagmo nga inka sinarita. LAMEDH.
89 Mawu anu Yehova ndi amuyaya; akhazikika kumwambako.
O Yahweh, mataginayon nga awan patinggana ti saom; ti saom ket sititibker a naisaad sadi langit.
90 Kukhulupirika kwanu kumakhala mpaka ku mibado yonse; Inu munakhazikitsa dziko lapansi ndipo lilipobe.
Ti kinapudnom ket mataginayon kadagiti amin a henerasion; inaramidmo ti daga, ket nagtalinaed daytoy.
91 Malamulo anu alipobe mpaka lero lino, pakuti zinthu zonse zimatumikira Inu.
Agtultuloy amin a banbanag agingga kadagitoy nga aldaw, kas imbagam kadagiti nalinteg a pangngeddengmo, ta adipenmo dagiti amin a banbanag.
92 Malamulo anu akanapanda kukhala chikondwerero changa, ndikanawonongeka mʼmasautso anga.
No saan a ti lintegmo ti paggappoan ti ragsakko, mabalin a napukawak koman iti pannakaparparigatko.
93 Ine sindidzayiwala konse malangizo anu, pakuti ndi malangizo anuwo munasunga moyo wanga.
Saankonto a pulos a lipaten dagiti pagannurotam, ta babaen kadagitoy ket pinagtalinaednak a sibibiag.
94 Ndine wanu, ndipulumutseni; pakuti ndasamala malangizo anu.
Kukuanak; isalakannak, ta birbirukek dagiti pagannurotam.
95 Anthu oyipa akudikira kuti andiwononge, koma ndidzalingalira umboni wanu.
Agsagsagana dagiti nadangkes a mangdadael kaniak, ngem ikagumaak nga awaten dagiti bilbilinmo iti tulagmo.
96 Ndadziwa kuti zinthu zonse zili ndi malire, koma malamulo anu alibe malire konse.
Nakitak nga adda pagpatinggaanna dagiti amin a banbanag, ngem nalawa dagiti bilbilinmo, awan patinggana. MEM
97 Ndithu, ine ndimakonda malamulo anu! Ndimalingaliramo tsiku lonse.
O anian nga ay-ayatek ti lintegmo! Agmalmalem nga ut-utubek daytoy.
98 Malamulo anu amachititsa kuti ndikhale wanzeru kuposa adani anga, popeza malamulowo ali ndi ine nthawi zonse.
Pagbalbalinennak a nasirsirib dagiti bilbilinmo ngem dagiti kabusorko, ta kanayon nga adda kaniak dagiti bilbilinmo.
99 Ndimamvetsa zinthu kwambiri kuposa aphunzitsi anga onse popeza ndimalingalira umboni wanu.
Ad-adda ti panakaawatko ngem dagiti amin a manursurok, ta ut-utubek dagiti bilbilinmo iti tulagmo.
100 Ndili ndi nzeru zochuluka zomvetsera zinthu kuposa anthu okalamba, popeza ndimamvera malangizo anu.
Ad-adda a maawatak ngem kadagiti natataengan ngem siak; gapu ta tinungpalko dagiti pagannurotam.
101 Ndimaletsa miyendo yanga kuyenda mʼnjira iliyonse yoyipa kuti ndithe kumvera mawu anu.
Inlisik dagiti sakak iti tunggal dakes a dalan tapno maaramidko ti saom.
102 Sindinapatuke kuchoka pa malamulo anu, pakuti Inu mwini munandiphunzitsa.
Saanak nga immadayo kadagiti nalinteg a pangngeddengmo, ta binilbilinnak.
103 Mawu anu ndi otsekemera ndikawalawa, otsekemera kuposa uchi mʼkamwa mwanga!
Anian a nagsam-it dagiti sasaom iti panagramanko, wen, nasamsam-it ngem diro iti ngiwatko!
104 Ndimapeza nzeru zodziwira zinthu kuchokera mʼmalangizo anu; kotero ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
Babaen kadagiti pagannurotam, nakagun-odak iti pannakaammo; ngarud, kagurak amin a palso a wagas. NUN.
105 Mawu anu ndi nyale ya kumapazi kwanga ndi kuwunika kwa pa njira yanga.
Ti saom ket silaw dagiti sakak ken lawag ti dalanko.
106 Ndalumbira ndipo ndatsimikiza, kuti ndidzatsatira malamulo anu olungama.
Insapatak, ken pinasingkedak daytoy, a tungpalek dagiti bilbilinmo.
107 Ndazunzika kwambiri; Inu Yehova, sungani moyo wanga molingana ndi mawu anu.
Maparparigatak unay; pagtalenaedennak a sibibiag, O Yahweh, kas inkarim iti saom.
108 Inu Yehova, landirani matamando aufulu ochokera pakamwa panga, ndipo ndiphunzitseni malamulo anu.
O Yahweh, pangngaasim ta awatem ti situtulok a daton ti ngiwatko, ket isurom kaniak dagiti nalinteg a pangngeddengmo.
109 Ngakhale moyo wanga umakhala mʼzoopsa nthawi ndi nthawi, sindidzayiwala malamulo anu.
Kankayon nga adda iti peggad ti biagko, ngem saanko a malipatan ti lintegmo.
110 Anthu oyipa anditchera msampha, koma sindinasochere kuchoka pa malangizo anu.
Nangisagana dagiti nadangkes iti palab-og para kaniak, ngem saanak nga immadayo manipud kadagiti pagannurotam.
111 Umboni wanu ndiye cholowa changa kwamuyaya; Iwo ndiye chimwemwe cha mtima wanga.
Tagikuaek dagiti bilbilinmo iti tulagmo kas tawidko iti agnanayon, ta dagitoy dagiti pakaragsakan ti pusok.
112 Mtima wanga wakhazikika pa kusunga zophunzitsa zanu mpaka kumapeto kwenikweni.
Nakasagana ti pusok nga agtulnog kadagiti alagadem iti agnanayon inggana iti panungpalan. SAMEKH.
113 Ndimadana ndi anthu apawiripawiri, koma ndimakonda malamulo anu.
Kagurak dagiti agduadua, ngem ay-ayatek ti lintegmo.
114 Inu ndinu pothawirapo panga ndi chishango changa; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Sika ti paglemmengak ken kalasagko; Mangnamnamaak iti saom.
115 Chokani kwa ine, inu anthu ochita zoyipa, kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga!
Umadayokayo kaniak, dakayo nga agar-aramid iti kinadakes, tapno matungpalko dagiti bilbilin ti Diosko.
116 Mundichirikize molingana ndi lonjezo lanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; musalole kuti chiyembekezo changa chipite pachabe.
Papigsaennak babaen kadagiti sasaom tapno agbiagak ken saan a mapabainan ti namnamak.
117 Gwirizizeni, ndipo ndidzapulumutsidwa; nthawi zonse ndidzasamalira zophunzitsa zanu.
Saranayennak, ket natalgedakto; kanayonto nga utubek dagiti alagadem.
118 Inu mumakana onse amene amasochera kuchoka pa zophunzitsa zanu, pakuti chinyengo chawo ndi chopanda phindu.
Ilaksidmo amin dagiti immadayo manipud kadagiti alagadem, ta manangallilaw ken saan a mapagtalkan dagidiay a tattao.
119 Anthu onse oyipa a pa dziko lapansi mumawayesa ngati zinthu zakudzala; nʼchifukwa chake ndimakonda umboni wanu.
Ikkatem amin dagiti nadangkes iti daga a kasla ragas; ayatek ngarud dagiti pagannurotam.
120 Thupi langa limanjenjemera chifukwa cha kuopa Inu; ndimachita mantha ndi malamulo anu.
Agpigerger ti bagik iti panagbuteng kenka, ket agbutengak kadagiti nalinteg a pangngeddengmo. AYIN.
121 Ndachita zolungama ndi zabwino; musandisiye mʼmanja mwa ondizunza.
Aramidek no ania ti nalinteg ken umno; saannak a panawan kadagiti mangidadanes kaniak.
122 Onetsetsani kuti mtumiki wanu akukhala bwino, musalole kuti anthu odzikuza andipondereze.
Patalgedam ti pagimbagan ti adipenmo; saanmo nga itulok nga idadanesdak dagiti natangsit.
123 Maso anga alefuka, kufunafuna chipulumutso chanu, kufunafuna lonjezo lanu lolungama.
Mabanbanogen dagiti matak nga agur-uray iti panagisalakanmo ken iti nalinteg a saom.
124 Muchite naye mtumiki wanu molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
Ipakitam iti adipenmo ti kinapudnom iti tulagmo, ken isurom kaniak dagiti alagadem.
125 Ine ndine mtumiki wanu; patseni mzimu wondizindikiritsa, kuti ndimvetsetse umboni wanu.
Siak ket adipenmo; ikkannak iti pannakaawat tapno maammoak dagiti bilbilinmo iti tulagmo.
126 Yehova, ndi nthawi yoti muchitepo kanthu; malamulo anu akuswedwa.
Panawenen nga agtignay ni Yahweh, ta linabsing dagiti tattao ti lintegmo.
127 Chifukwa choti ndimakonda malamulo anu kuposa golide, kuposa golide woyengeka bwino,
Pudno nga ay-ayatek dagiti bilbilinmo a nalablabes ngem balitok, nalablabes ngem puro a balitok.
128 ndiponso chifukwa choti ndimaona kuti malangizo anu onse ndi wowongoka, ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
Ngarud, tungpalek a nasayaat dagiti amin a pagannurotam, ket guraek ti tunggal dalan ti kinapalso. PE.
129 Maumboni anu ndi odabwitsa nʼchifukwa chake ndimawamvera.
Nakakaskasdaaw dagiti paglintegam, isu't gapuna a tungtungpalek ida.
130 Mawu anu akamaphunzitsidwa amapereka kuwunika; ngakhale anthu wamba amamvetsetsa.
Ti panangsukimat kadagiti sasaom ket mangmangted iti lawag; mangmangted daytoy iti pannakaawat kadagiti saan a nakasursuro.
131 Ndimatsekula pakamwa panga ndi kupuma wefuwefu, kufunafuna malamulo anu.
Agnganga ken agal-al-alak, ta mailiwak kadagiti bilbilinmo.
132 Tembenukirani kwa ine ndipo mundichitire chifundo, monga mumachitira nthawi zonse kwa iwo amene amakonda dzina lanu.
Talliawennak ken maasika kaniak, a kas kanayon nge ar-aramidem kadagiti mangay-ayat iti naganmo.
133 Tsogolerani mayendedwe anga molingana ndi mawu anu; musalole kuti tchimo lizindilamulira.
Iturongmo dagiti addangko babaen iti saom; saanmo nga itulok nga iturayannak iti aniaman a basol.
134 Ndiwomboleni mʼdzanja la anthu ondizunza, kuti ndithe kumvera malangizo anu.
Subbotennak manipud iti panangidadanes dagiti tattao tapno matungpalko dagiti pagannurotam.
135 Nkhope yanu iwalire mtumiki wanu ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
Agraniag koma ti rupam iti adipenmo, ken isurom kaniak dagiti alagadem.
136 Mitsinje ya misozi ikuyenda kuchoka mʼmaso mwanga, chifukwa anthu sakumvera malamulo anu.
Agarubos dagiti luluak a kasla karayan manipud kadagiti matak gapu ta saan a tungtungpalen dagiti tattao ti lintegmo. TSADHE
137 Yehova ndinu wolungama, ndipo malamulo anu ndi abwino.
Nalintegka, O Yahweh, ket awan idumduma dagiti bilbilinmo.
138 Maumboni amene munatipatsa ndi olungama; ndi odalirika ndithu.
Intedmo dagiti bilbilinmo iti tulagmo a sililinteg ken sipupudno.
139 Ndikusautsidwa kwambiri mʼkati mwanga chifukwa adani anu amanyalanyaza mawu anu.
Dinadaelnak ti pungtot gapu ta nalipatan dagiti kabusorko dagiti sasaom.
140 Mawu anu ndi woyera kwambiri nʼchifukwa chake mtumiki wanune ndimawakonda.
Pudno unay dagiti sasaom, ket ay-ayaten daytoy ti adipenmo.
141 Ngakhale ndili wamngʼono ndi wonyozeka, sindiyiwala malangizo anu.
Saanak a napateg ken maum-umsiak, ngem saanko latta a malipatan dagiti pagannurotam.
142 Chilungamo chanu nʼchamuyaya, ndipo malamulo anu nʼchoona.
Agnanayon nga umno ti panangukommo, ken mapagtalkan ti lintegmo.
143 Mavuto ndi masautso zandigwera, koma ndimakondwera ndi malamulo anu.
Uray no masarakannak ti rigat ken tuok, pakaragsakak latta dagiti bilbilinmo.
144 Umboni wanu ndi wabwino nthawi zonse; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ine ndikhale ndi moyo.
Agnanayon a nalinteg dagiti bilbilinmo iti tulagmo; ikkannak iti pannakaawat tapno agbiagak. QOPH.
145 Ndimayitana ndi mtima wanga wonse; ndiyankheni Inu Yehova, ndipo ndidzamvera zophunzitsa zanu.
Immawagak iti amin a pusok, “Sungbatannak, O Yahweh, salimetmetak dagiti alagadem.
146 Ndikuyitana kwa Inu; pulumutseni ndipo ndidzasunga umboni wanu.
Umawagak kenka; isalakannak, ket tungpalek dagiti bilbilinmo iti tulagmo.
147 Ndimadzuka tambala asanalire kuti ndipemphe thandizo; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Bumangonak sakbay nga aglawag iti agsapa ket dumawatak iti tulong. Mangnamnamaak kadagiti sasaom.
148 Maso anga amakhala chipenyere nthawi yonse ya usiku, kuti ndithe kulingalira malonjezo anu.
Silulukat dagiti matak iti agpatpatnag tapno mabalinko nga utuben ti saom.
149 Imvani mawu anga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika; Yehova sungani moyo wanga, molingana ndi malamulo anu.
Denggem ti timekko gapu iti kinapudnom iti tulagmo, pagtalinaedennak a sibibiag, O Yahweh, a kas inkarim kadagiti nalinteg a pangngeddengmo.
150 Iwo amene amakonza njira zoyipa andiyandikira, koma ali kutali ndi malamulo anu.
Umas-asideg dagiti mangparparigat kaniak, ngem adayoda kadagiti lintegmo.
151 Koma Inu Yehova muli pafupi, malamulo anu onse ndi woona.
Asidegka, O Yahweh, ket mapagtalkan dagiti amin a bilbilinmo.
152 Ndinaphunzira kalekale kuchokera mʼmaumboni anu kuti maumboni amene munakhazikitsawo ndi amuyaya.
Idi un-unana, naadalko kadagiti bilbilinmo iti tulagmo nga insaadmo dagitoy iti agnanayon. RESH.
153 Yangʼanani masautso anga ndipo mundipulumutse, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
Kitaem ti pannakaparigatko ket tulongannak, ta saanko a malipatan ti lintegmo.
154 Mundiyimirire pa mlandu wanga ndi kundiwombola; sungani moyo wanga molingana ndi lonjezo lanu.
Ikanawanak ken subbotennak; saluadannak, kas inkarim iti saom.
155 Chipulumutso chili kutali ndi anthu oyipa, pakuti iwowo safunafuna zophunzitsa zanu.
Adayo ti pannakaisalakan kadagiti nadangkes, ta saanda nga ay-ayaten dagiti alagadem.
156 Chifundo chanu Yehova nʼchachikulu; sungani moyo wanga molingana ndi malamulo anu.
Naindaklan ti kinamanangngaasim, O Yahweh; pagtalinaedennak a sibibiag, kas kankanayon nga ar-aramidem.
157 Adani amene akundizunza ndi ambiri, koma ine sindinatembenuke kuchoka pa umboni wanu.
Adu dagiti mangidadanes ken kabusorko, ngem saanko latta a tinallikudan dagiti bilbilinmo iti tulagmo.
158 Ndimawayangʼana monyansidwa anthu opanda chikhulupiriro, popeza samvera mawu anu.
Kitkitaek dagiti manangallilaw nga addaan rurod gapu ta saanda a tungtungpalen ti saom.
159 Onani momwe ndimakondera malangizo anu; sungani moyo wanga, Inu Yehova, molingana ndi chikondi chanu chosanthika.
Kitaem no kasano ti panagayatko kadagiti pagannurotam; pagtalinaedennak a sibibiag, O Yahweh, kas inkarim iti kinapudnom iti tulagmo.
160 Mawu anu onse ndi owona; malamulo anu onse olungama ndi amuyaya.
Naan-anay ti kinapudno ti saom; tunggal bilinmo ket agpa-ut iti agnanayon. SHIN
161 Olamulira amandizunza popanda chifukwa, koma mtima wanga umanjenjemera ndi mawu anu.
Parparigatendak dagiti prinsipe nga awan gapgapuna; agkebba-kebba ti pusok, mabuteng a manglabsing iti saom.
162 Ine ndimakondwa ndi lonjezo lanu, ngati munthu amene wapeza chuma chambiri.
Agrag-oak iti saom a kasla maysa a tao a nakasarak iti nawadwad a kinabaknang.
163 Ndimadana ndi chinyengo, kwambiri ndimanyansidwa nacho, koma ndimakonda malamulo anu.
Kagurak ken umsiek ti kinapalso, ngem ay-ayatek ti lintegmo.
164 Ndimakutamandani kasanu ndi kawiri pa tsiku pakuti malamulo anu ndi olungama.
Maminpito iti maysa nga aldaw a daydayawenka gapu kadagiti nalinteg a pangngeddengmo.
165 Amene amakonda malamulo anu ali ndi mtendere waukulu, ndipo palibe chimene chingawapunthwitse
Naindaklan a kapia ti adda kadakuada; dagiti mangay-ayat iti lintegmo; awan iti makaitibkol kadakuada.
166 Ndikudikira chipulumutso chanu, Inu Yehova, ndipo ndimatsatira malamulo anu.
Ur-urayek ti panangisalakanmo, O Yahweh, ket agtulnogak kadagiti bilbilinmo.
167 Ndimamvera umboni wanu pakuti ndimawukonda kwambiri.
Tungtungpalek dagiti napudno a bilbilinmo, ket ay-ayatek unay dagitoy.
168 Ndimamvera malangizo anu ndi umboni wanu, pakuti njira zanga zonse ndi zodziwika pamaso panu.
Tungtungpalek dagiti pagannurotam ken dagiti npudno a bilbilinmo, ta ammom amin dagiti ar-aramidek. TAV.
169 Kulira kwanga kufike pamaso panu Yehova; patseni nzeru zomvetsa zinthu molingana ndi mawu anu.
Denggem ti un-unnoyko a dumawdawat iti tulong, O Yahweh, ikkannak iti pannakaawat iti saom.
170 Kupempha kwanga kufike pamaso panu; pulumutseni molingana ndi lonjezo lanu.
Dumanon koma ti pakaasik iti sangoanam; tulongannak, a kas inkarim iti saom.
171 Matamando asefukire pa milomo yanga, pakuti Inu mumandiphunzitsa malamulo anu.
Mangibuyat koma iti panagdayaw dagiti bibigko, ta insurom kaniak dagiti alagadem.
172 Lilime langa liyimbe mawu anu, popeza malamulo anu onse ndi olungama.
Agkanta koma ti dilak maipanggep iti saom, ta umno amin dagiti bilbilinmo.
173 Dzanja lanu likhale lokonzeka kundithandiza pakuti ndasankha malangizo anu.
Tulongannak koma dagiti imam, ta pinilik dagiti pagannurotam.
174 Ndikufunitsitsa chipulumutso chanu Yehova, ndipo ndimakondwera ndi malamulo anu.
Kalkalikagumak ti panangispalmo, O Yahweh, ket pakaragsakak ti lintegmo.
175 Loleni kuti ndikhale ndi moyo kuti ndikutamandeni, ndipo malamulo anu andichirikize.
Mataginayonak koma nga agbiag ken agdayaw kenka, ket tulongannak koma dagiti nalinteg a pangngeddengmo.
176 Ndasochera ngati nkhosa yotayika, funafunani mtumiki wanu, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
Naiyaw-awanak a kasla napukaw a karnero; birukem ti adipenmo, ta saanko a nalipatan dagiti bilbilinmo.

< Masalimo 119 >