< Masalimo 135 >

1 Tamandani Yehova. Tamandani dzina la Yehova; mutamandeni, inu atumiki a Yehova,
Alleluia. Laudate nomen Domini, laudate servi Dominum:
2 amene mumatumikira mʼnyumba ya Yehova, mʼmabwalo a nyumba ya Mulungu wathu.
Qui statis in domo Domini, in atriis domus Dei nostri.
3 Tamandani Yehova, pakuti Yehova ndi wabwino; imbani nyimbo zotamanda dzina lake, pakuti nʼkokoma kutero,
Laudate Dominum, quia bonus Dominus: psallite nomini eius, quoniam suave.
4 Pakuti Yehova wasankha Yakobo kuti akhale wake, Israeli kuti akhale chuma chake chapamtima.
Quoniam Iacob elegit sibi Dominus Israel in possessionem sibi.
5 Ndikudziwa kuti Yehova ndi wamkulu, kuti Ambuye athu ndi wamkulu kuposa milungu yonse.
Quia ego cognovi quod magnus est Dominus, et Deus noster præ omnibus diis.
6 Yehova amachita chilichonse chimene chimamukomera, kumwamba ndi dziko lapansi, ku nyanja zazikulu ndi ku malo ake onse akuya.
Omnia quæcumque voluit, Dominus fecit in cælo, in terra, in mari, et in omnibus abyssis.
7 Iye amatulutsa mitambo kuchokera ku malekezero a dziko lapansi, amatumiza zingʼaningʼani pamodzi ndi mvula ndipo amatulutsa mphepo ku malo ake osungiramo.
Educens nubes ab extremo terræ: fulgura in pluviam fecit. Qui producit ventos de thesauris suis:
8 Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto, ana oyamba kubadwa a anthu ndi nyama.
qui percussit primogenita Ægypti ab homine usque ad pecus.
9 Iye anatumiza zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa pakati pako, iwe Igupto, kutsutsana ndi Farao pamodzi ndi atumiki ake onse.
Et misit signa, et prodigia in medio tui Ægypte: in Pharaonem, et in omnes servos eius.
10 Iye anakantha mitundu yambiri ya anthu ndi kupha mafumu amphamvu:
Qui percussit gentes multas: et occidit reges fortes:
11 Sihoni mfumu ya Aamori, Ogi mfumu ya Basani, ndi maufumu onse a ku Kanaani;
Sehon regem Amorrhæorum, et Og regem Basan, et omnia regna Chanaan.
12 ndipo anapereka dziko lawo ngati cholowa, cholowa cha anthu ake Aisraeli.
Et dedit terram eorum hereditatem, hereditatem Israel populo suo.
13 Dzina lanu, Inu Yehova, ndi losatha mpaka muyaya, mbiri yanu, Inu Yehova, idziwika mibado yonse.
Domine nomen tuum in æternum: Domine memoriale tuum in generationem et generationem.
14 Pakuti Yehova adzaonetsa kuti anthu ake ngosalakwa, ndipo adzachitira chifundo atumiki ake.
Quia iudicabit Dominus populum suum: et in servis suis deprecabitur.
15 Mafano a mitundu ya anthu ndi siliva ndi golide, opangidwa ndi manja a anthu.
Simulacra Gentium argentum, et aurum, opera manuum hominum.
16 Pakamwa ali napo koma sayankhula maso ali nawo, koma sapenya;
Os habent, et non loquentur: oculos habent, et non videbunt.
17 makutu ali nawo, koma sakumva ndipo mʼkamwa mwawo mulibe mpweya uliwonse.
Aures habent, et non audient: neque enim est spiritus in ore ipsorum.
18 Iwo amene amapanga mafanowo adzakhala ngati mafanowo, chimodzimodzinso iwo amene amadalira mafanowo.
Similes illis fiant qui faciunt ea: et omnes, qui confidunt in eis.
19 Inu nyumba ya Israeli, tamandani Yehova; inu nyumba ya Aaroni, tamandani Yehova;
Domus Israel benedicite Domino: domus Aaron benedicite Domino.
20 Inu nyumba ya Levi, tamandani Yehova; Inu amene mumaopa Iye, tamandani Yehova.
Domus Levi benedicite Domino: qui timetis Dominum, benedicite Domino.
21 Wodalitsika ndi Yehova kuchokera mʼZiyoni, amene amakhala mu Yerusalemu. Tamandani Yehova.
Benedictus Dominus ex Sion, qui habitat in Ierusalem.

< Masalimo 135 >