< Masalimo 23 >

1 Salimo la Davide. Yehova ndiye mʼbusa wanga, sindidzasowa kanthu.
A psalm of David. Yahweh is my shepherd; I will lack nothing.
2 Amandigoneka pa msipu wobiriwira, amanditsogolera ku madzi akumwa abwino,
He makes me to lie down in green pastures; he leads me beside tranquil water.
3 amatsitsimutsa moyo wanga. Amanditsogolera mʼnjira zachilungamo chifukwa cha dzina lake.
He brings back my life; he guides me along right paths for his name's sake.
4 Ngakhale ndiyende mʼchigwa cha mdima wakuda bii, sindidzaopa choyipa, pakuti Inu muli ndi ine; chibonga chanu ndi ndodo yanu zimanditonthoza.
Even though I walk through a valley of darkest shadow, I will not fear harm since you are with me; your rod and your staff comfort me.
5 Mumandikonzera chakudya adani anga akuona. Mumadzoza mutu wanga ndi mafuta; chikho changa chimasefukira.
You prepare a table before me in the presence of my enemies; you have anointed my head with oil; my cup runs over.
6 Zoonadi, zokoma ndi chikondi chosasinthika zidzanditsata masiku onse a moyo wanga, ndipo ndidzakhala mʼNyumba ya Yehova kwamuyaya.
Surely goodness and covenant faithfulness will pursue me all the days of my life; and I will live in the house of Yahweh for a very long time!

< Masalimo 23 >