< Masalimo 34 >

1 Salimo la Davide. Pamene iye ananyengezera misala pamaso pa Abimeleki, amene anamupirikitsa, iyeyo nʼkuchoka. Ndidzayamika Yehova nthawi zonse; matamando ake adzakhala pa milomo yanga nthawi zonse.
Von David. Als er seine Gebärde verstellte vor Abimelech und dieser ihn von sich trieb und er hinwegging. Ich will den HERRN allezeit preisen, sein Lob soll immerdar in meinem Munde sein.
2 Moyo wanga udzanyadira Yehova; anthu osautsidwa amve ndi kukondwera.
Meine Seele rühme sich des HERRN; die Elenden sollen es hören und sich freuen.
3 Lemekezani Yehova pamodzi ndi ine; tiyeni pamodzi tikuze dzina lake.
Preiset mit mir den HERRN, und lasset uns miteinander seinen Namen erhöhen!
4 Ine ndinafunafuna Yehova ndipo Iye anandiyankha; anandilanditsa ku mantha anga onse.
Da ich den HERRN suchte, antwortete er mir und errettete mich aus aller meiner Furcht.
5 Iwo amene amayangʼana kwa Iye, nkhope zawo zimanyezimira; nkhope zawo sizikhala zophimbidwa ndi manyazi.
Die auf ihn blicken, werden strahlen, und ihr Angesicht wird nicht erröten.
6 Munthu wosauka uno anayitana, ndipo Yehova anamumva; Yehova anamupulumutsa ku mavuto ake onse.
Da dieser Elende rief, hörte der HERR und half ihm aus allen seinen Nöten.
7 Mngelo wa Yehova amatchinjiriza amene amakonda Iye ndi kuwalanditsa.
Der Engel des HERRN lagert sich um die her, so ihn fürchten, und errettet sie.
8 Lawani ndipo onani kuti Yehova ndi wabwino; wodala munthu amene amathawira kwa Iye.
Schmecket und sehet, wie freundlich der HERR ist; wohl dem, der auf ihn traut!
9 Wopani Yehova inu oyera mtima ake, pakuti iwo amene amaopa Iye sasowa kanthu.
Fürchtet den HERRN, ihr seine Heiligen; denn die ihn fürchten, haben keinen Mangel.
10 Mikango itha kulefuka ndi kumva njala koma iwo amene amafunafuna Yehova sasowa kanthu kalikonse kabwino.
Junge Löwen leiden Not und Hunger; aber die den HERRN suchen, müssen nichts Gutes entbehren.
11 Bwerani ana anga, mundimvere; ndidzakuphunzitsani kuopa Yehova.
Kommt her, ihr Kinder, hört mir zu; ich will euch die Furcht des HERRN lehren!
12 Aliyense wa inu amene amakonda moyo wake ndi kukhumba kuti aone masiku abwino ambiri,
Wer hat Lust zum Leben und möchte gern gute Tage sehen?
13 asunge lilime lake ku zoyipa ndi milomo yake kuti isayankhule zonama.
Behüte deine Zunge vor Bösem und deine Lippen, daß sie nicht trügen;
14 Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino; funafuna mtendere ndi kuwulondola.
weiche vom Bösen und tue Gutes, suche Frieden und jage ihm nach!
15 Maso a Yehova ali pa olungama ndipo makutu ake ali tcheru kumva kulira kwawo;
Die Augen des HERRN achten auf die Gerechten und seine Ohren auf ihr Schreien;
16 nkhope ya Yehova ikutsutsana ndi amene amachita zoyipa, kuwachotsa kuti asawakumbukirenso pa dziko lapansi.
das Antlitz des HERRN steht wider die, so Böses tun, daß er ihr Gedächtnis von der Erde vertilge.
17 Olungama amafuwula, ndipo Yehova amawamva; Iye amawalanditsa ku mavuto awo onse.
Als jene schrieen, hörte der HERR und rettete sie aus aller ihrer Not.
18 Yehova ali pafupi kwa osweka mtima ndipo amapulumutsa iwo amene asweka mu mzimu.
Der HERR ist nahe denen, die zerbrochenen Herzens sind, und hilft denen, deren Geist zerschlagen ist.
19 Munthu wolungama atha kukhala ndi mavuto ambiri, Koma Yehova amamulanditsa ku mavuto onsewo,
Der Gerechte muß viel leiden; aber der HERR rettet ihn aus dem allem.
20 Iye amateteza mafupa ake onse, palibe limodzi la mafupawo limene lidzathyoledwa.
Er bewahrt ihm alle seine Gebeine, daß nicht eines derselben zerbrochen wird.
21 Choyipa chidzapha anthu oyipa; adani a olungama adzapezeka olakwa.
Den Gottlosen wird die Bosheit töten, und die den Gerechten hassen, müssen es büßen.
22 Yehova amawombola atumiki ake; aliyense amene amathawira kwa Iye sadzapezeka wolakwa.
Der HERR erlöst die Seele seiner Knechte, und alle, die auf ihn vertrauen, werden es nicht zu büßen haben.

< Masalimo 34 >