< Olcueih 16 >

1 Hlang taengah lungbuei kah rhoekbahnah om dae olka hlatnah he BOEIPA lamkah ni.
Zolinga za mu mtima ndi za munthu, koma kwa Yehova ndiye kumachokera yankho.
2 Hlang kah a longpuei boeih he amah mikhmuh ah khui dae, BOEIPA long tah a mueihla ni a khiinglang pah.
Zochita zonse za munthu zimaoneka zabwino pamaso pake, koma Yehova ndiye amasanthula zolinga zako.
3 Na bibi te BOEIPA taengah hal lamtah, na kopoek cikngae bitni.
Pereka ntchito zako zonse mʼmanja mwa Yehova, ndipo zolinga zako zidzachitikadi.
4 Soeprhaep boeih he amah kah a hlatnah ham BOEIPA loh a saii. Te dongah halang pataeng yoethae hnin kah ham a hlun.
Yehova amachita zonse ndi cholinga chake, ngakhale anthu oyipa kuti aone tsiku latsoka.
5 Kut neh kut hlaengtang tih lungbuei aka oek boeih BOEIPA kah a tueilaehkoi la a om dongah hmil mahpawh.
Munthu aliyense wodzikuza amamunyansa Yehova. Koma dziwani izi: Iwo sadzakhala osalangidwa.
6 Sitlohnah neh oltak loh thaesainah a dawth tih, BOEIPA hinyahnah loh boethae lamkah a nong sak.
Chifukwa cha chikondi chosasinthika ndi kukhulupirika, munthu amakhululukidwa machimo ake; chifukwa cha kuopa Yehova munthu amapewa zoyipa.
7 Hlang kah khosing te BOEIPA loh a moeithen vaengah a thunkha rhoek pataeng amah taengah a rhong sak.
Pamene makhalidwe a munthu akondweretsa Yehova, ngakhale adani ake amakhala naye mwa mtendere.
8 Duengnah neh yol mai cakhaw, a tiktam mueh canghum cangpai lakah then.
Kuli bwino kukhala ndi zinthu pangʼono zozipeza mwachilungamo, kusiyana ndi kukhala ndi zinthu zambiri zozipeza popanda chilungamo.
9 Hlang kah lungbuei loh amah longpuei te a moeh tih, BOEIPA loh a khokan a cikngae sak.
Mtima wa munthu umalingalira zochita, koma Yehova ndiye amakhazikitsa njira zake.
10 Manghai ka dongkah bihma tah laitloeknah ham ni, te dongah a ka vikvawk boel saeh.
Mawu a mfumu ali ngati mawu ochokera kwa Mulungu; ndipo pakamwa pake sipalakwa poweruza mlandu.
11 Tiktamnah cooi neh coilung tah BOEIPA taeng lamkah ni, sungsa coilung boeih khaw amah kah a bibi ni.
Miyeso ndi masikelo achilungamo zimachokera kwa Yehova; miyala yonse yoyesera ya mʼthumba anayipanga ndi Yehova.
12 Duengnah loh ngolkhoel a cikngae sak dongah, manghai rhoek loh halangnah a saii ham tah tueilaehkoi la om.
Kuchita zoyipa kumanyansa mafumu, pakuti chilungamo ndiye maziko a ufumu wake.
13 Duengnah hmuilai tah manghai rhoek kah kolonah om tih, a thuem aka thui te a lungnah.
Mawu owona amakondweretsa mfumu. Iyo imakonda munthu woyankhula choonadi.
14 Manghai kah kosi tah dueknah puencawn ni. Te dongah hlang cueih long ni kosi a daeh sak thai eh.
Ukali wa mfumu ndi mthenga wa imfa, koma munthu wanzeru amawupepesa ukaliwo.
15 Manghai kah maelhmai khosae dongah hingnah tih, a kolonah tah tlankhol vaengkah khomai banghui ni.
Kuwala kwa nkhope ya mfumu kumapatsa moyo; ndipo kukoma mtima kwake kuli ngati mitambo ya mvula nthawi ya chilimwe.
16 Cueihnah lai he sui lakah bahoeng then tih, yakmingnah lai he khaw tangka n'tuek lakah then.
Nʼkwabwino kwambiri kupeza nzeru kupambana golide. Kukhala womvetsa bwino zinthu nʼkwabwino kupambana ndi kukhala ndi siliva.
17 Boethae lamloh aka nong hamla a thuem longpuei om tih, a hinglu aka ngaithuen loh a longpuei a kueinah.
Msewu wa munthu wowongoka mtima umapewa zoyipa; wopenyetsetsa kumene akupita amasunga moyo wake.
18 Pocinah kah a hmaiah hoemdamnah om tih, cungkunah kah a hmaiah ah mueihla oeknah a lamhma pah.
Kunyada kumafikitsa ku chiwonongeko, ndipo munthu wodzikuza adzagwa.
19 Thinthah neh kutbuem n'tael lakah kodo mangdaeng neh mueihla kunyun te then.
Nʼkwabwino kukhala ndi mtima wodzichepetsa pakati pa anthu oponderezedwa, kusiyana ndi kugawana zolanda ndi anthu onyada.
20 Olka neh aka cangbam long tah hnothen a dang tih, BOEIPA dongah aka pangtung tah a yoethen pai.
Munthu womvera malangizo zinthu zimamuyendera bwino, ndipo wodala ndi amene amadalira Yehova.
21 Lungbuei aka cueih te aka yakming la a khue uh tih, hmuilai dongkah olding loh rhingtuknah a thap.
A mtima wanzeru amatchedwa ozindikira zinthu, ndipo mawu ake okoma amawonjezera nzeru.
22 Lungmingnah te a kungmah la aka khueh long tah hingnah thunsih la om tih, aka ang rhoek kah thuituennah tah anglat la poeh.
Kumvetsa zinthu ndi kasupe wa moyo kwa iwo amene ali nako, koma uchitsiru umabweretsa chilango kwa zitsiru.
23 Aka cueih kah lungbuei tah a ka a cangbam tih, a hmuilai dongah rhingtuknah a thap.
Mtima wanzeru umathandiza munthu kuyankhula mwa nzeru, ndipo mawu ake amawonjezera nzeru.
24 Ol then tah, hinglu ham khoitui khoitak bangla didip tih, rhuh hamla hoeihnah la om.
Mawu okometsera ali ngati chisa cha njuchi, amakoma mu mtima ndipo amalimbitsa thupi.
25 Hlang mikhmuh ah longpuei te thuem dae a hmailong ah dueknah longpuei la om.
Pali njira ina yooneka ngati yowongoka kwa munthu koma kumatsiriziro kwake ndi imfa.
26 Thakthaekung kah a hinglu loh amah hamla thakthae tih a ka te a kamcah sak.
Njala ya munthu wantchito imamuthandiza kulimbikira; njalayo imamukakamiza kuchitapo kanthu.
27 Hlang muen loh boethae a vueh tih, a hmuilai dongah hmai bangla rhangto.
Munthu wopanda pake amakonzekera kuchita zoyipa ndipo mawu ake ali ngati moto wopsereza.
28 Calaak hlang loh olpungkacan a haeh tih, hlang aka thet loh boeihlum a pamhma sak.
Munthu woyipa mtima amayambitsa mikangano, ndipo miseche imalekanitsa anthu okondana kwambiri.
29 Kuthlahnah hlang loh a hui a hloeh tih, longpuei a then pawt la a caeh puei.
Munthu wandewu amakopa mnansi wake, ndipo amamuyendetsa njira imene si yabwino.
30 Calaak te moeh hamla a mik aka him tih, a hmui saibaeh loh boethae a cung sak.
Amene amatsinzinira maso ake amalingalira zinthu zokhota; amene amachita msunamo amakonzeka kuchita zoyipa.
31 Sampok he boeimang rhuisam la om tih, duengnah longpuei kah aka om loh a dang.
Imvi zili ngati chipewa chaufumu chaulemerero; munthu amazipeza akakhala moyo wolungama.
32 Thintoek aka ueh tah hlangrhalh lakah, a mueihla aka taem khaw khopuei aka ta lakah then.
Munthu wosapsa mtima msanga amaposa munthu wankhondo, munthu wowugwira mtima wake amaposa amene amalanda mzinda.
33 A rhang dongah hmulung khoh cakhaw a laitloeknah boeih tah BOEIPA lamkah ni a om.
Maere amaponyedwa pa mfunga, koma ndiye Yehova amene amalongosola zonse.

< Olcueih 16 >