< Mudre Izreke 24 >

1 Ne zavidi opakim ljudima niti želi da budeš s njima.
Usachitire nsanje anthu oyipa, usalakalake kuti uzikhala nawo,
2 Jer im srce smišlja nasilje i usne govore o nedjelu.
pakuti mitima yawo imalingalira chiwawa, ndipo pakamwa pawo pamayankhula zoyambitsa mavuto.
3 Mudrošću se zida kuća i razborom utvrđuje,
Nyumba imamangidwa ndi anthu anzeru, ndipo imakhazikika ndi anthu odziwa zinthu;
4 i po znanju se pune klijeti svakim blagom dragocjenim i ljupkim.
Munthu wodziwa zinthu angathe kudzaza zipinda zake ndi chuma chamtengowapatali ndiponso chabwino.
5 Bolji je mudar od jakoga i čovjek razuman od silne ljudine.
Munthu wodziwa zinthu ali ndi mphamvu yayikulu kuposa munthu wanyonga zambiri, ndipo munthu wachidziwitso amaposa munthu wamphamvu.
6 Jer s promišljanjem se ide u boj i pobjeda je u mnoštvu savjetnika.
Pafunika malangizo kuti ukamenye nkhondo. Pakakhala aphungu ambiri kupambana kumakhalapo.
7 Previsoka je bezumnomu mudrost: zato na sudu ne otvara usta svojih!
Nzeru ndi chinthu chapatali kwambiri kwa chitsiru; chilibe choti chiyankhule pabwalo la milandu pa chipata.
8 Tko smišlja zlo zove se učitelj podmukli.
Amene amakonzekera kuchita zoyipa adzatchedwa mvundulamadzi.
9 Ludost samo grijeh snuje, i podrugljivac je mrzak ljudima.
Kukonzekera kuchita za uchitsiru ndi tchimo, ndipo munthu wonyoza amanyansa anthu.
10 Kloneš li u dan bijede, bijedna je tvoja snaga.
Ngati utaya mtima nthawi ya mavuto ndiye kuti mphamvu yako ndi yochepadi!
11 Izbavi one koje vode u smrt; i spasavaj one koji posrćući idu na stratište.
Uwapulumutse amene akutengedwa kuti akaphedwe; uwalanditse amene akuyenda movutika kupita kokaphedwa.
12 Ako kažeš: “Nismo za to znali”, ne razumije li onaj koji ispituje srca? I ne znade li onaj koji ti čuva dušu? I ne plaća li on svakomu po njegovim djelima?
Ukanena kuti, “Koma ife sitinadziwe kanthu za izi,” kodi Iye amene amasanthula mtima sazindikira zimenezi? Kodi Iye amene amateteza moyo wako sazidziwa zimenezi? Kodi Iye sadzalipira munthu malingana ndi ntchito zake?
13 Jedi med, sine moj, jer je dobar, i saće je slatko nepcu tvome.
Mwana wanga, uzidya uchi popeza ndi wabwino; uchi wochokera mʼchisa cha njuchi ndi wokoma ukawulawa.
14 Takva je, znaj, i mudrost tvojoj duši: ako je nađeš, našao si budućnost i nada tvoja neće propasti.
Udziwe kuti nzeru ndi yoteronso pa moyo wako; ngati uyipeza nzeruyo, zinthu zidzakuyendera bwino mʼtsogolo, ndipo chiyembekezo chako sichidzapita pachabe.
15 Ne postavljaj, opaki, zasjede stanu pravednikovu, ne čini nasilja boravištu njegovu;
Usachite zachifwamba nyumba ya munthu wolungama ngati munthu woyipa. Usachite nayo nkhondo nyumba yake;
16 jer padne li pravednik i sedam puta, on ustaje, a opaki propadaju u nesreći.
paja munthu wolungama akagwa kasanu nʼkawiri amadzukiriranso. Koma woyipa adzathedwa tsoka likadzawafikira.
17 Ne veseli se kad padne neprijatelj tvoj i ne kliči srcem kada on posrće,
Usamakondwera ndi kugwa kwa mdani wako. Mtima wako usamasangalale iye akapunthwa.
18 da ne bi vidio Jahve i za zlo uzeo i obratio srdžbu svoju od njega.
Kuopa kuti Yehova ataziona zimenezi nayipidwa nazo, angaleke kukwiyira mdaniyo.
19 Nemoj se srditi zbog zločinaca, nemoj zavidjeti opakima,
Usavutike mtima chifukwa cha anthu ochita zoyipa kapena kuchitira nsanje anthu oyipa,
20 jer zao čovjek nema budućnosti, svjetiljka opakih gasi se.
paja munthu woyipa alibe tsogolo. Moyo wa anthu oyipa adzawuzimitsa ngati nyale.
21 Boj se Jahve, sine moj, i kralja: i ne buni se ni protiv jednoga ni protiv drugoga.
Mwana wanga, uziopa Yehova ndi mfumu, ndipo usamagwirizana ndi anthu owachitira mwano,
22 Jer iznenada provaljuje nesreća njihova i tko zna kad će doći propast njihova.
awiri amenewa amagwetsa tsoka mwadzidzidzi. Ndani angadziwe mavuto amene angagwetse?
23 I ovo je od mudraca: Ne valja biti pristran na sudu.
Malangizo enanso a anthu anzeru ndi awa: Kukondera poweruza mlandu si chinthu chabwino:
24 Tko opakomu veli: “Pravedan si”, proklinju ga narodi i kunu puci;
Aliyense amene amawuza munthu wolakwa kuti, “Iwe ndi munthu wosalakwa,” anthu a mitundu yonse adzamutemberera, ndi mitundu ya anthu idzayipidwa naye.
25 a oni koji ga ukore nalaze zadovoljstvo, i na njih dolazi blagoslov sreće.
Koma olanga anthu oyipa zinthu zidzawayendera bwino ndipo madalitso ochuluka adzakhala pa iwo.
26 U usta ljubi tko odgovara pošteno.
Woyankhula mawu owona ndiye amaonetsa chibwenzi chenicheni.
27 Svrši svoj posao vani i uredi svoje polje, potom i kuću svoju zidaj.
Ugwiriretu ntchito zako zonse, makamaka za ku munda ndipo pambuyo pake uyambe kumanga nyumba.
28 Ne svjedoči lažno na bližnjega svoga: zar ćeš varati usnama svojim?
Usakhale mboni yotsutsa mnzako popanda chifukwa, kapena kugwiritsa ntchito pakamwa pako kunena zachinyengo.
29 Ne reci: “Kako je on meni učinio, tako ću i ja njemu; platit ću tom čovjeku po djelu njegovu!”
Usanene kuti, “Ine ndidzamuchitira iye monga momwe wandichitira ine; ndidzamubwezera munthu ameneyo zimene anandichitira.”
30 Prolazio sam mimo polje nekog lijenčine i mimo vinograd nekog luđaka,
Ndinkayenda mʼmbali mwa munda wa munthu waulesi ndinadutsa munda wamphesa wa munthu wopanda nzeru.
31 i gle, sve bijaše zaraslo u koprive, i sve pokrio čkalj, i kamena ograda porušena.
Ndinapeza kuti paliponse mʼmundamo munali mutamera minga, mʼnthaka imeneyo munali mutamera khwisa, ndipo mpanda wake wamiyala unali utawonongeka.
32 Vidjeh to i pohranih u srcu, promotrih i uzeh pouku:
Tsono nditaona ndinayamba kuganizira mu mtima mwanga ndipo ndinatolapo phunziro ili:
33 “Još malo odspavaj, još malo odrijemaj, još malo podvij ruke za počinak,
Ukati, “Bwanji ndigone pangʼono,” kapena “Ndiwodzereko pangʼono,” kapenanso “Ndipinde manja pangʼono kuti ndipumule,”
34 i doći će tvoje siromaštvo kao skitač i oskudica kao oružanik!”
umphawi udzafika pa iwe ngati mbala ndipo usiwa udzakupeza ngati munthu wachifwamba.

< Mudre Izreke 24 >