< 2 Mosebog 37 >

1 Derpå lavede Bezal'el Arken af Akacietræ, halvtredje Alen lang, halvanden Alen bred og halvanden Alen høj,
Bezaleli anapanga Bokosi la Chipangano lamatabwa amtengo wa mkesha. Kutalika kwake kunali masentimita 114, mulifupi mwake munali masentimita 69, msinkhu wake masentimita 69.
2 og overtrak den indvendig og udvendig med purt Guld og satte en gylden Krans rundt om den.
Iye analikuta bokosilo ndi golide wabwino kwambiri mʼkati mwake ndi kunja komwe. Anapanganso mkombero wagolide kuzungulira bokosilo.
3 Derefter støbte han fire Guldringe til den og satte dem på dens fire Fødder, to Ringe på hver Side af den.
Iye anapanga mphete zinayi zagolide ndi kuzimangirira ku miyendo yake inayi ija, mbali ina ziwiri ndi mbali inanso ziwiri.
4 Og han lavede Bærestænger af Akacietræ og overtrak dem med Guld;
Kenaka anapanga mizati yamtengo wa mkesha ndi kuzikuta ndi golide.
5 så stak han Stængerne gennem Ringene på Arkens Sider, for at den kunde bæres med dem.
Ndipo analowetsa nsichizo mʼmphete zija za mbali zonse ziwiri za bokosilo kuti azinyamulira.
6 Derpå lavede han Sonedækket af purt Guld, halvtredje Alen langt og halvanden Alen bredt,
Iye anapanga chivundikiro cha bokosilo cha golide wabwino kwambiri, kutalika kwake masentimita 114, mulifupi mwake masentimita 69.
7 og han lavede to Keruber af Guld, i drevet Arbejde lavede han dem, ved begge Ender af Sonedækket,
Ndipo anapanga Akerubi awiri agolide osula ndi nyundo ndi kuwayika mbali ziwiri za chivundikirocho.
8 den ene Kerub ved den ene Ende, den anden Kerub ved den anden; han lavede Keruberne således, at de var i eet med Sonedækket ved begge Ender.
Iye anapanga kerubi mmodzi mbali ina ndi wina mbali inayo. Akerubiwa anawapangira limodzi ndi chivundikirocho mʼmapeto mwa mbali ziwirizo.
9 Og Keruberne bredte deres Vinger i Vejret, således at de dækkede over Sonedækket med deres Vinger; de vendte Ansigtet mod hinanden; nedad mod Sone, dækket vendte Kerubernes Ansigter.
Mapiko a Akerubiwo anatambasukira pamwamba pa chivundikiro cha bokosilo kuti achiphimbe. Akerubiwo anakhala choyangʼanana, aliyense kuyangʼana chivundikirocho.
10 Derpå lavede han Bordet af Akacietræ, to Alen langt, en Alen bredt og halvanden Alen højt,
Iwo anapanga tebulo la matabwa amtengo wa mkesha, mulitali mwake masentimita 91, mulifupi mwake masentimita 46, msinkhu wake masentimita 69.
11 og overtrak det med purt Guld og satte en gylden Krans rundt om det.
Kenaka analikuta ndi golide wabwino kwambiri, ndipo anapanga mkombero wagolide mʼmbali mwake.
12 Og han satte en Liste af en Hånds Bredde rundt om det og en gylden Krans rundt om Listen.
Iwo anapanga feremu yozungulira tebulo, mulifupi mwake ngati chikhatho cha dzanja, ndipo anayika mkombero wagolide kuzungulira feremuyo.
13 Og han støbte fire Guldringe og satte dem på de fire Hjørner ved dets fire Ben.
Iwo anapanga mphete zinayi zagolide ndipo anazilumikiza ku ngodya zake zinayi, kumene kunali miyendo yake inayi.
14 Lige ved Listen sad Ringene til at stikke Bærestængerne i, så at man kunde bære Bordet.
Mphetezo anaziyika kufupi ndi feremu kuti azikolowekamo nsichi zonyamulira tebuloyo.
15 Og han lavede Bærestængerne at Akacietræ og overtrak dem med Guld, og med dem skulde Bordet bæres.
Anapanga nsichi zamtengo wa mkesha ndi kuzikuta ndi golide kuti azinyamulira tebulolo.
16 Og han lavede af purt Guld de Ting, som hørte til Bordet, Fadene og Kanderne, Skålene og Krukkerne til at udgyde Drikoffer med.
Ndipo anapanga ziwiya za pa tebulolo zagolide wabwino, mbale ndi zipande, mitsuko ndi mabeseni zogwiritsa ntchito popereka nsembe za chakumwa.
17 Derpå lavede han Lysestagen af purt Guld, i drevet Arbejde lavede han Lysestagen, dens Fod og selve Stagen, således at dens Blomster med Bægere og Kroner var i eet med den;
Iwo anapanga choyikapo nyale chagolide wabwino kwambiri. Tsinde lake ndi mphanda zake zinasulidwa ndi nyundo. Zikho zake zokhala ndi mphukira ndi maluwa ake zinapangidwa kumodzi.
18 seks Arme udgik fra Lysestagens Sider, tre fra den ene og tre fra den anden Side.
Mʼmbali mwake munali mphanda zisanu ndi imodzi, zitatu mbali iliyonse.
19 På hver af Armene, der udgik fra Lysestagen, var der tre mandelblomstlignende Blomster med Bægere og Kroner,
Zikho zitatu zokhala ngati za maluwa amtowo, mphukira ndi duwa zinali pa mphanda yoyamba. Pa mphanda yachiwiri panalinso zikho zitatu zokhala ngati za maluwa amtowo, mphukira ndi duwa. Ndipo mphanda zonse zisanu ndi imodzi zinali chimodzimodzi ndipo zinatuluka mʼchoyikapo nyalecho.
20 men på selve Stagen var der fire mandelblomstlignende Blomster med Bægere og Kroner,
Pa choyikapo nyalecho panali zikho zinayi zokhala ngati maluwa amtowo, mphukira ndi maluwa ake.
21 et Bæger under hvert af de tre Par Arme, der udgik fra den.
Mphukira yoyamba inali mʼmunsi mwa nthambi ziwiri zoyamba za pa choyikapo nyale. Mphukira yachiwiri inali mʼmunsi mwa nthambi ziwiri zinazo. Mphukira yachitatu inali mʼmunsi mwa nthambi zina ziwirinso. Zonse pamodzi zinali nthambi zisanu ndi imodzi
22 Bægrene og Armene var i eet med den, så at det hele udgjorde eet drevet Arbejde af purt Guld.
Mphukira ndi nthambi zonse zinasulidwa kumodzi ndi choyikapo nyalecho ndi golide wabwino kwambiri.
23 Derpå lavede han de syv Lamper til den, Lampesaksene og Bakkerne af purt Guld.
Iwo anapanga nyale zisanu ndi ziwiri, mbaniro ndi zowolera phulusa, zonse zinali zagolide wabwino kwambiri.
24 En Talent purt Guld brugte han til den og til alt dens Tilbehør.
Iwo anapanga choyikapo nyale ndi zipangizo zake zonse zagolide wabwino kwambiri wolemera makilogalamu 34.
25 Derpå lavede han Røgelsealteret af Akacietræ, en Alen langt og en Alen bredt, i Firkant, og to Alen højt, og dets Horn var i eet med det.
Iwo anapanga guwa lamatabwa amtengo wa mkesha lofukizirapo lubani. Linali lofanana mbali zonse, mulitali masentimita 46, mulifupi masentimita 46, ndipo msinkhu masentimita 91, ndipo nyanga zake zinapangidwa kumodzi ndi guwalo.
26 Og han overtrak det med purt Guld, både Pladen og Siderne hele Vejen rundt og Hornene, og satte en Guldkrans rundt om;
Iwo anakuta guwa lonse ndi golide wabwino kwambiri, pamwamba pake, mbali zonse ndi nyanga zake, ndipo anapanga mkombero wagolide kuzungulira guwalo.
27 og han satte to Guldringe under Kransen på begge Sider til at stikke Bærestængerne i, for at det kunde bæres med dem;
Anapanga mphete ziwiri pansi pa mkomberowo ndi kulumikiza ku mbali zonse ziwiri kuti apisemo nsichi zonyamulira.
28 Bærestængerne lavede han af Akacietræ og overtrak dem med Guld.
Anapanga mizati yamtengo wa mkesha ndipo anayikuta ndi golide.
29 Han tilberedte også den hellige Salveolie og den rene, vellugtende Røgelse, som Salveblanderne laver den.
Iwo anapanganso mafuta opatulika odzozera ndi zofukiza za fungo lokoma kwambiri. Iyi inali ntchito ya mʼmisiri waluso lopanga zonunkhiritsa.

< 2 Mosebog 37 >