< Ezra 5 >

1 Men Profeterne Haggaj og Zakarias, Iddos Søn, profeterede for Jøderne i Juda og Jerusalem i Israels Guds Navn, som var over dem.
Nthawi imeneyo aneneri Hagai ndi Zekariya, mwana wa Ido, ankayankhula kwa Ayuda okhala mʼdziko la Yuda ndi mu Yerusalemu mʼdzina la Mulungu wa Israeli, amene anali nawo.
2 Da tog Zerubbabel, Sjealtiels Søn, og Jesua, Jozadaks Søn, fat og begyndte at bygge på Guds Hus i Jerusalem sammen med Guds Profeter, som støttede dem.
Pambuyo pake Zerubabeli mwana wa Sealatieli ndi Yesuwa mwana wa Yozadaki ananyamuka nakayambanso kumanga Nyumba ya Mulungu mu Yerusalemu. Ndipo aneneri a Mulungu anali nawo pamodzi, kuwathandiza.
3 Men på den Tid kom Tattenaj, Statholderen hinsides Floden, Sjetar-Bozenaj og deres Embedsbrødre til dem og sagde: "Hvem har givet eder Lov til at bygge dette Tempel og genopføre denne Helligdom,
Pa nthawi imeneyo Tatenai, bwanamkubwa wa chigawo cha patsidya pa Yufurate pamodzi ndi Setari-Bozenai ndi anzawo anapita kwa iwo ndi kukawafunsa kuti, “Anakulolani ndani kuti mumangenso Nyumba imeneyi ndi kutsiriza khoma lake?”
4 og hvad er Navnene på de Mænd, der bygger denne Bygning?
Anawafunsanso kuti, “Kodi anthu amene akumanga nyumbayi mayina awo ndani?”
5 Men over Jødernes Ældste vågede deres Guds Øje, så de ikke standsede dem i Arbejdet, før Sagen var forelagt Darius og der var kommet Svar derpå.
Koma Mulungu wawo amayangʼanira atsogoleri Ayuda, motero kuti anthu aja anaganiza kuti asawaletse kumanga Nyumbayo mpaka atalembera mfumu Dariyo kalata ndi kulandira yankho lake.
6 Afskrift af det Brev, som Tattenaj, Statholderen hinsides Floden, Sjetar-Bozenaj og hans Embedsbrødre, Afarsekiterne hinsides Floden, sendte Kong Darius;
Iyi ndi kalata imene Tatenai bwanamkubwa wa dera la patsidya pa Yufurate, ndiponso Setari-Bozenai ndi anzake, akazembe amene anali mʼchigawo cha patsidya pa Yufurate, anatumiza kwa mfumu Dariyo
7 de sendte ham en Skrivelse, hvori der stod: Kong Darius ønsker vi al Fred!
Analemba kalatayo motere: Kwa mfumu Dariyo: Mukhale ndi mtendere wonse.
8 Det være Kongen kundgjort, at vi begav os til Landsdelen Judæa til den store Guds Hus; det bliver bygget af Kvadersten, der lægges Bjælker i Muren, og Arbejdet udføres med Omhu og skyder frem under deres Hænder.
Amfumu mudziwe kuti ife tinapita ku dziko la Yuda ku Nyumba ya Mulungu wamkulu. Nyumbayo ikumangidwa ndi miyala ikuluikulu ndipo akuyala matabwa pa makoma. Ntchitoyi ikugwiridwa mwachangu ndipo ikuyenda bwino kwambiri mwautsogoleri wawo.
9 Vi spurgte da de Ældste der og talte således til dem: "Hvem har givet eder Lov til at, bygge dette Tempel og opføre denne Helligdom?
Ndipo tinawafunsa atsogoleriwo kuti, “Anakulolezani kuti mumangenso Nyumbayi ndi kutsiriza makoma ake ndani?”
10 Vi spurgte dem også om deres Navne for at lade dig dem vide, og vi opskrev Navnene på de Mænd, der står i Spidsen for dem.
Tinawafunsanso mayina a atsogoleri awo, kuti tikalemba mayina atsogoleriwo tidzakudziwitseni kuti muwadziwe.
11 Og Svaret, de gav os, lød således: Vi er Himmelens og Jordens Guds Tjenere, og vi bygger det Tempel, som blev bygget for mange År siden, da en stor Konge i Israel byggede og opførte det.
Yankho limene anatipatsa ndi ili: “Ife ndife atumiki a Mulungu wa kumwamba ndi wa dziko lapansi, ndipo tikumanganso Nyumba imene mfumu ina yamphamvu ya Israeli inamanga ndi kuyitsiriza zaka zambiri zapitazo.
12 Da imidlertid vore Fædre vakte Himmelens Guds Vrede, gav han dem i Babels Konges, Kaldæeren Nebukadnezars, Hånd, og han nedbrød dette Tempel og førte Folket i Landflygtighed til Babel.
Koma chifukwa chakuti makolo athu anakwiyitsa Mulungu wakumwamba, Iye anawapereka kwa Nebukadinezara Mkalideya, mfumu ya Babuloni, amene anawononga Nyumbayi ndi kutenga anthu onse kupita nawo ku ukapolo ku Babuloni.
13 Men i sit første Regeringsår gav Kong Kyros af Babel Befaling til at genopbygge dette Gudshus;
“Komabe chaka choyamba cha Koresi, mfumu ya ku Babuloni, mfumu Koresiyo anapereka lamulo lakuti Nyumba ya Mulunguyi imangidwenso.
14 og Kong Kyros lod tillige de til Gudshusef hørende Guld- og Sølvkar, som Nebukadnezar havde borttaget fra Helligdommen i Jerusalem og ført til sin Helligdom i Babel, tage ud af Helligdommen i Babel, og de overgaves til en Mand ved Navn Sjesjbazzar, som han havde indsat til Statholder;
Ndipo ziwiya zagolide ndi zasiliva za ku Nyumba ya Mulungu zimene Nebukadinezara anazitenga mʼNyumba ya Mulungu ku Yerusalemu ndi kukaziyika mʼnyumba ya milungu ya ku Babuloni, anakazichotsa ku nyumba ya milungu ya ku Babuloniko ndi kuzipereka kwa Sesibazara, amene mfumu inamusankha kukhala bwanamkubwa.
15 og han sagde til ham: "Tag disse Kar og drag ben og lad dem få deres Plads i Helligdommen i Jerusalem og lad Gudshuset blive genopbygget på sin gamle Plads!"
Tsono mfumuyo inamuwuza kuti, ‘Tenga ziwiyazi ukaziyike mʼNyumba ya Mulungu ku Yerusalemu. Ndipo Nyumba ya Mulunguyo ikamangidwenso pa maziko ake akale.’
16 Så kom denne Sjesjbazzar og lagde Grunden til Gudshuset i Jerusalem, og siden den Tid er der bygget derpå, men det er ikke færdigt.
“Choncho Sesibazarayo anabwera ndi kumanga maziko a Nyumba ya Mulunguyo mu Yerusalemu. Kuyambira tsiku limenelo mpaka lero yakhala ikumangidwa ndipo sinathebe.”
17 Hvis derfor Kongen synes, så lad der blive set efter i det kongelige Skatkammer ovre i Babel, om det har sig således, at der af Kong Kyros er givet Befaling til at bygge dette Gudshus i Jerusalem; og Kongen give os så sin Vilje i denne Sag til Kende!"
Nʼchifukwa chake ngati chingakukomereni amfumu, pachitike kafukufuku mʼnyumba yaufumu mosungira chuma ndi mabuku okhudza mbiri ya Babuloni kuti tione ngati mfumu Koresi inalamuladi za kumanganso Nyumba ya Mulungu mu Yerusalemu. Kenaka amfumu mutiwuze zomwe zikukondweretsani kuti mugamule pa nkhani imeneyi.

< Ezra 5 >