< Nehemias 7 >

1 Da Muren var bygget, lod jeg Portfløjene indsætte, og Dørvogterne, Sangerne og Leviterne blev ansat.
Khoma linamangidwa ndipo zitseko zinayikidwa. Pambuyo pake alonda a Nyumba ya Mulungu, oyimba nyimbo ndiponso Alevi anasankhidwa.
2 Overbefalingen over Jerusalem gav jeg min Broder Hanani og Borgøversten Hananja; thi han var en pålidelig Mand og frygtede Gud som få;
Kenaka ine ndinasankha mʼbale wanga Hanani pamodzi ndi Hananiya woyangʼanira nsanja yankhondo kukhala olamulira Yerusalemu chifukwa iyeyu anali munthu odalirika ndi woopa Mulungu kuposa anthu ena.
3 og jeg sagde til dem: "Jerusalems Porte må ikke åbnes, før Solen står højt på Himmelen; og medens den endnu står der, skal man lukke og stænge Portene og sætte Jerusalems Indbyggere på Vagt, hver på sin Post, hver ud for sit Hus!"
Ine ndinawawuza kuti, “Musalole kuti zipata za Yerusalemu zitsekulidwe mpaka dzuwa litatentha, ndipo alonda asanaweruke aonetsetse kuti atseka zitseko ndi kuzipiringidza. Musankhe alonda pakati pa anthu okhala mu Yerusalemu, ena akhale pa malo pawo ndi ena akhale moyangʼanana ndi nyumba zawo.”
4 Men Byen var udstrakt og stor og dens Indbygere få, og Husene var endnu ikke opbygget.
Tsono mzinda wa Yerusalemu unali wotambasuka ndiponso waukulu koma munali anthu ochepa ndipo nyumba zinali zisanamangidwe.
5 Da skød min Gud mig i Sinde at samle de store, Forstanderne og Folket for at indføre dem i Slægtsfortegnelser. Og da fandt jeg Slægtebogen over dem, der først var draget op, og i den fandt jeg skrevet:
Ndipo Mulungu wanga anayika mu mtima mwanga maganizo oti ndisonkhanitse anthu olemekezeka, akuluakulu ndi anthu onse kuti alembetse mayina mwa mabanja awo. Ndinapeza buku limene munalembedwa mayina a mabanja a iwo amene anayamba kubwera kuchokera ku ukapolo. Izi ndi zimene ndinazipeza zitalembedwa mʼmenemo:
6 Følgende er de Folk fra vor Landsdel, der drog op fra Land flygtigheden og Fangenskabet. Kong Nebukadnezar af Babel havde ført dem bort, men nu vendte de til bage til Jerusalem og Juda, hver til sin By;
Awa ndi anthu a mʼchigawo cha Yuda amene anabwerera kuchokera ku ukapolo amene Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anawatenga ukapolo. Iwo anabwerera ku Yerusalemu ndi ku Yuda, aliyense ku mzinda wa makolo ake.
7 de kom sammen med Zerubbabel, Jesua, Nehemja, Azarja, Ra'amja, Nahamani, Mordokaj, Bilsjan, Misperet, Bigvaj, Nehum og Ba'ana. Tallet på Mændene i Israels Folk var:
Anabwera pamodzi ndi atsogoleri awa: Zerubabeli, Yesuwa, Nehemiya, Azariya, Raamiya, Nahamani, Mordekai, Bilisani, Misipereti, Bigivai, Nehumu ndi Baana. Tsono chiwerengero cha anthu a ku Israeli chinali chotere:
8 Par'osj's Efterkommere 2172,
Zidzukulu za Parosi 2,172
9 Sjefatjas Efterkommere 372,
Zidzukulu za Sefatiya 372
10 Aras Efterkommere 652,
Zidzukulu za Ara 652
11 Pahat-Moabs Efterkommere, Jesuas og Joabs Efterkommere, 2818,
Zidzukulu za Pahati-Mowabu (kudzera mu mʼbado wa Yesuwa ndi Yowabu) 2,818
12 Elams Efterkommere 1254,
Zidzukulu za Elamu 1,254
13 Zattus Efterkommere 845,
Zidzukulu za Zatu 845
14 Zakkajs Efterkommere 760,
Zidzukulu za Zakai 760
15 Binnujs Efterkommere 648,
Zidzukulu za Binuyi 648
16 Bebajs Efterkommere 628,
Zidzukulu za Bebai 628
17 Azgads Efterkommere 2322,
Zidzukulu za Azigadi 2,322
18 Adonikams Efterkommere 667,
Zidzukulu za Adonikamu 667
19 Bigvajs Efterkommere 2067,
Zidzukulu za Abigivai 2,067
20 Adins Efterkommere 655,
Zidzukulu za Adini 655
21 Aters Efterkommere gennem Hizkija 98,
Zidzukulu za Ateri (kudzera mwa Hezekiya) 98
22 Hasjums Efterkommere 328,
Zidzukulu za Hasumu 328
23 Bezajs Efterkommere 324,
Zidzukulu za Bezayi 324
24 Harifs Efterkommere 112,
Zidzukulu za Harifu 112
25 Gibeons Efterkommere 95,
Zidzukulu za Gibiyoni 95.
26 Mændene fra Betlehem og Netofa 188,
Anthu a ku Betelehemu ndi Netofa 188
27 Mændene fra Anatot 128,
Anthu a ku Anatoti 128
28 Mændene fra Bet-Azmavet 42,
Anthu a ku Beti-Azimaveti 42
29 Mændene fra Hirjat-Jearim, Kefra og Be'erot 743;
Anthu a ku Kiriati Yeyarimu Kefira ndi Beeroti 743
30 Mændene fra Rama og Geba 621,
Anthu a ku Rama ndi Geba 621
31 Mændene fra Mikmas 122,
Anthu a ku Mikimasi 122
32 Mændene fra Betel og Aj 123,
Anthu a ku Beteli ndi Ai 123
33 Mændene fra det andet Nebo 52,
Anthu a ku Nebo winayo 52
34 det andet Elams Efterkommere 1254,
Ana a Elamu wina 1,254
35 Harims Efterkommere 320,
Zidzukulu za Harimu 320
36 Jerikos Efterkommere 345,
Zidzukulu za Yeriko 345
37 Lods, Hadids og Onos Efterkommere 721,
Zidzukulu za Lodi, Hadidi ndi Ono 721
38 Sena'as Efterkommere 3930.
Zidzukulu za Senaya 3,930.
39 Præsterne var: Jedajas Efterkommere af Jesuas Hus 973,
Ansembe anali awa: A banja la Yedaya (ndiye kuti zidzukulu za Yesuwa) 973
40 Immers Efterkommere 1052,
Zidzukulu za Imeri 1,052
41 Pasjhurs Efterkommere 1247,
Zidzukulu za Pasi-Huri 1,247
42 Harims Efterkommere 1017.
Zidzukulu za Harimu 1,017.
43 Leviterne var: Jesuas og Kadmiels Efterkommere af Hodavjas Efterkommere 74.
Alevi anali awa: A banja la Yesuwa ndi Kadimieli, ndiye kuti zidzukulu za Hodaviya 74.
44 Tempelsangerne var: Asafs Efterkommere 148.
Anthu oyimba: Zidzukulu za Asafu 148.
45 Dørvogterne var: Sjallums, Aters, Talmons, Akkubs, Hatitas og Sjobajs Efterkommere 138.
Alonda a ku Nyumba ya Mulungu anali awa: Zidzukulu za Salumu, Ateri, Talimoni, Hatita ndi Sobai 138.
46 Tempeltrællene var: Zihas, Hasufas, Tabbaots,
Anthu ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu anali awa: Zidzukulu za Ziha, zidzukulu za Hasufa, zidzukulu za Tabaoti,
47 Keros's, Si'as, Padons,
Zidzukulu Kerosi, zidzukulu za Siya, zidzukulu za Padoni
48 Lebanas, Hagabas, Salmajs,
Zidzukulu za Lebana za Hagaba, ndi za Salimayi,
49 Hanans, Giddels, Gahars,
Zidzukulu za Hanani, zidzukulu za Gideli, zidzukulu za Gahari,
50 Reajas, Rezins, Nekodas,
Zidzukulu za Reyaya, zidzukulu za Rezini, zidzukulu za Nehoda,
51 Gazzams, Uzzas, Paseas,
Zidzukulu za Gazamu, zidzukulu za Uza, zidzukulu za Paseya,
52 Besajs, Me'uniternes, Nefusiternes,
Zidzukulu za Besai, zidzukulu za Meunimu, zidzukulu za Nefusimu,
53 Bakbuks, Hakufas, Harhurs,
Zidzukulu za Bakibuku, zidzukulu za Hakufa, zidzukulu za Harihuri,
54 Bazluts, Mehidas, Harsjas,
Zidzukulu za Baziliti, zidzukulu za Mehida, zidzukulu za Harisa,
55 Barkos's, Siseras, Temas,
Zidzukulu za Barikosi, zidzukulu za Sisera, zidzukulu za Tema
56 Nezias og Hatifas Efterkommere.
Zidzukulu za Neziya, ndi zidzukulu za Hatifa.
57 Efterkommerne af Salomos Trælle var: Sotajs, Soferets, Peridas,
Zidzukulu za antchito a Solomoni: Zidzukulu za Sotai, zidzukulu za Sofereti, zidzukulu za Perida
58 Ja'alas, Darkons, Giddels,
zidzukulu za Yaala, zidzukulu za Darikoni, zidzukulu za Gideli,
59 Sjefatjas, Hattils, Pokeret-Hazzebajims og Amons Efterkommere.
zidzukulu za Sefatiya, zidzukulu za Hatilu zidzukulu za Pokereti-Hazebaimu ndi zidzukulu Amoni.
60 Alle Tempeltrælle og Efferkommerne af Salomos Trælle var tilsammen 392.
Anthu onse ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu pamodzi ndi zidzukulu za antchito a Solomoni analipo 392.
61 Følgende, som drog op fra Tel-Mela, Tel-Harsja, Kerub-Addon og Immer, kunde ikke opgive, hvorvidt deres Fædrenehuse og Slægt hørte til Israeliterne:
Ali munsiwa anachokera ku Teli-Mela, Teri-Harisa, Kerubi, Adoni, ndi Imeri, koma sanathe kunena mwa tchutchutchu kuti makolo awo kapena mafuko awo analidi Aisraeli kapena ayi.
62 Delajas, Tobijas og Nekodas Efterkommere 642.
Zidzukulu za Delaya, zidzukulu za Tobiya ndi zidzukulu za Nekoda 642.
63 Og følgende Præster: Habajas, Hakoz's og Barzillajs Efterkommere; denne sidste havde ægtet en af Gileaditen Barzillajs Døtre og var blevet opkaldt efter dem.
Ndiponso ena pakati pa ansembe anali awa: zidzukulu za Hobiya, zidzukulu za Hakozi ndi zidzukulu za Barizilai (munthu amene anakwatira mwana wamkazi wa Barizilai wa ku Giliyadi ndipo amatchedwa dzina limenelo).
64 De ledte efter deres Slægtebøger, men kunde ikke finde dem; derfor blev de som urene udelukket fra Præstestanden.
Iwowa anafufuzafufuza mayina awo mʼbuku la mibado ya mabanja awo ndipo sanapeze mayina awo kotero anachotsedwa pa unsembe nawerengedwa ngati odetsedwa pa chipembedzo.
65 Statholderen forbød dem at spise af det højhellige, indtil der fremstod en Præst med Urim og Tummim.
Choncho bwanamkubwa anawawuza anthuwo kuti asamadye nawo chakudya china chilichonse choperekedwa kwa Mulungu mpaka patapezeka wansembe wodziwa kugwiritsa bwino ntchito ya Urimu ndi Tumimu.
66 Hele Menigheden udgjorde 42360
Chiwerengero chonse cha anthuwa chinali 42,360.
67 foruden deres Trælle og Trælkvinder, som udgjorde 7337, hvor til kom 245 Sangere og Sangerinder.
Kuwonjezera pamenepa panali antchito awo aamuna ndi aakazi 7,337 ndiponso anthu aamuna ndi aakazi oyimba nyimbo okwanira 245.
68 Deres Heste udgjorde 736, deres Mulddyr 245,
Panali akavalo 736, abulu angʼonoangʼono 245.
69 deres Kameler 435 og deres Æsler 6720.
Ngamira zawo zinalipo 435 ndipo abulu analipo 6,720.
70 En Del af Fædrenehusenes Overhoveder ydede Tilskud til Byggearbejdet. Statholderen gav til Byggesummen 1000 Drakmer Guld, 50 Skåle og 30 Præstekjortler.
Atsogoleri ena a mabanja anapereka mphatso zothandizira ntchito. Bwanamkubwa anapereka ku thumba losungira chuma, ndalama zagolide za makilogalamu asanu ndi atatu, mabeseni makumi asanu ndi zovala za ansembe 530.
71 Af Fædrenehusenes Overhoveder gav nogle til Byggesummen 20.000 Drakmer Guld og 2.200 Miner Sølv.
Atsogoleri ena amabanja anapereka ku thumba losungira chuma ndalama zagolide zokwana makilogalamu 168, ndiponso ndalama za siliva zokwana makilogalamu 1,250.
72 Og hvad det øvrige Folk gav, løb op til 20.000 Drakmer Guld, 2.000 Miner Sølv og 67 Præstekjortler.
Anthu ena onse otsala anapereka ndalama zagolide zokwana makilogalamu 168, ndalama za siliva zokwana makilogalamu 140, ndiponso zovala za ansembe 67.
73 Derpå bosatte Præsterne, Leviterne og en Del af Folket sig i Jerusalem og dets Område, men Sangerne, Dørvogterne og hele det øvrige Israel i deres Byer.
Choncho ansembe, Alevi, alonda a Nyumba ya Mulungu, anthu oyimba nyimbo, ena mwa anthu wamba, ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu pamodzi ndi Aisraeli ena onse ankakhala mʼmizinda yawo. Pofika mwezi wachisanu ndi chiwiri Aisraeli onse anali atakhazikika mʼmizinda yawo.

< Nehemias 7 >