< Salme 138 >

1 (Af David.) Jeg vil prise dig HERRE, at hele lovsynge dig for Guderne;
Salimo la Davide. Ndidzakuyamikani Yehova ndi mtima wanga wonse; ndidzayimba nyimbo zokutamandani pamaso pa “milungu.”
2 jeg vil tilbede, vendt mod dit hellige Tempel, og mere end alt vil jeg prise dit Navn for din Miskundheds og Trofastheds Skyld; thi du har herliggjort dit Ord.
Ndidzagwada kuyangʼana ku Nyumba yanu yoyera ndipo ndidzayamika dzina lanu chifukwa cha chikondi chanu ndi kukhulupirika kwanu, pakuti Inu mwakuza dzina lanu ndi mawu anu kupambana zinthu zonse.
3 Den Dag jeg råbte, svared du mig, du gav mig Mod, i min Sjæl kom Styrke.
Pamene ndinayitana, munandiyankha; munandisandutsa wamphamvu ndi wolimba mtima.
4 Alle Jordens Konger skal prise dig, HERRE, når de hører din Munds Ord,
Mafumu onse a dziko lapansi akuyamikeni Yehova, pamene amva mawu a pakamwa panu.
5 og synge om HERRENs Veje; thi stor er HERRENs Ære,
Iwo ayimbe za njira za Yehova, pakuti ulemerero wa Yehova ndi waukulu.
6 thi HERREN er ophøjet, ser til den ringe, han kender den stolte i Frastand.
Ngakhale kuti Yehova ngokwezeka, amasamalira odzichepetsa, koma anthu onyada amawadziwira chapatali.
7 Går jeg i Trængsel, du værger mig Livet, mod Fjendernes Vrede udrækker du Hånden, din højre bringer mig Frelse.
Ngakhale ndiyende pakati pa masautso, mumasunga moyo wanga; mumatambasula dzanja lanu kutsutsana ndi mkwiyo wa adani anga, mumandipulumutsa ndi dzanja lanu lamanja.
8 HERREN vil føre det igennem for mig, din Miskundhed, HERRE, varer evindelig. Opgiv ej dine Hænders Værk!
Yehova adzakwaniritsa cholinga chake pa ine; chikondi chanu chosasinthika Yehova, ndi chosatha musasiye ntchito ya manja anu.

< Salme 138 >