< Salme 29 >

1 (En salme af David.) Giver HERREN, I Guds Sønner, giver Herren Ære og Pris,
Salimo la Davide. Perekani kwa Yehova, inu anthu amphamvu, perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu.
2 giver HERREN hans Navns Ære; tilbed HERREN i helligt Skrud!
Perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake, pembedzani Yehova mwa kukongola kwa chiyero chake.
3 HERRENs Røst er over Vandene, Ærens Gud lader Tordenen rulle, HERREN, over de vældige Vande!
Liwu la Yehova lili pamwamba pa madzi; Mulungu waulemerero abangula, Yehova abangula pamwamba pa madzi amphamvu.
4 HERRENs Røst med Vælde, HERRENs Røst i Højhed,
Liwu la Yehova ndi lamphamvu; liwu la Yehova ndi laulemerero.
5 HERRENs Røst, den splintrer Cedre, HERREN splintrer Libanons Cedre,
Liwu la Yehova limathyola mikungudza; Yehova amathyolathyola mikungudza ya ku Lebanoni.
6 får Libanon til at springe som en Kalv og Sirjon som den vilde Okse!
Iye amachititsa Lebanoni kulumphalumpha ngati mwana wangʼombe, Siriyoni ngati mwana wa njati:
7 HERRENs Røst udslynger Luer.
Liwu la Yehova limakantha ngati kungʼanima kwa mphenzi.
8 HERRENs Røst får Ørk til at skælve, HERREN får Kadesj's Ørk til at skælve!
Liwu la Yehova limagwedeza chipululu; Yehova amagwedeza chipululu cha Kadesi.
9 HERRENs Røst får Hind til at føde, og den gør lyst i Skoven. Alt i hans Helligdom råber: "Ære!"
Liwu la Yehova limapindapinda mibawa ndi kuyeretsa nkhalango. Ndipo mʼNyumba mwake onse amafuwula kuti, “Ulemerero!”
10 HERREN tog Sæde og sendte Vandfloden, HERREN tog Sæde som Konge for evigt.
Yehova amakhala pamwamba pa madzi osefukira, Yehova ndiye mfumu kwamuyaya.
11 HERREN give Kraft til sit Folk, HERREN velsigne sit Folk med Fred!
Yehova amapereka mphamvu kwa anthu ake; Yehova amadalitsa anthu ake ndi mtendere.

< Salme 29 >