< Job 19 >

1 Then Job answered, and said,
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 How long will ye vex my soul, and break me in pieces with words?
“Kodi mudzakhala mukundizunza mpaka liti, ndi kundilasa ndi mawu anuwo?
3 These ten times ye have reproached me. Ye are not ashamed that ye deal hardly with me.
Inuyo mwandinyoza kwambiri; mwanditsutsa mopanda manyazi.
4 And be it indeed that I have erred, my error remains with myself.
Ngati ndi zoona kuti ine ndasochera, cholakwachotu nʼchanga.
5 If indeed ye will magnify yourselves against me, and plead against me my reproach,
Ngati ndithudi mukudziyika nokha pamwamba panga, ndi kugwiritsa ntchito kunyozedwa kwanga polimbana nane,
6 know now that God has subverted me, and has encompassed me with his net.
pamenepa dziwani kuti Mulungu wandilakwira ndipo wandizinga ukonde wake.
7 Behold, I cry out of wrong, but I am not heard. I cry for help, but there is no justice.
“Ngakhale ndifuwule kuti, ‘Akundizunza!’ Palibe wondiyankha; ngakhale ndipemphe thandizo, palibe wondichitira zolungama.
8 He has walled up my way that I cannot pass, and has set darkness in my paths.
Mulungu wanditsekera njira yanga kotero sindingathe kudutsa; waphimba njira zanga ndi mdima.
9 He has stripped me of my glory, and taken the crown from my head.
Iye wandilanda ulemu wanga ndipo wandivula chipewa chaufumu pamutu panga.
10 He has broken me down on every side, and I am gone. And he has plucked up my hope like a tree.
Wandiphwanyaphwanya mbali zonse ndipo ndatheratu; Iye wazula chiyembekezo changa ngati mtengo.
11 He has also kindled his wrath against me. And he considers me to him as his adversaries.
Wandikwiyira ndipo akundiyesa mmodzi mwa adani ake.
12 His troops come on together, and cast up their way against me, and encamp round about my tent.
Ankhondo ake akubwera kwa ine mwamphamvu, akonzekera zodzalimbana nane ndipo azungulira nyumba yanga.
13 He has put my brothers far from me, and my acquaintances are wholly estranged from me.
“Mulungu wandisiyanitsa ndi abale anga; wasandutsa odziwana nane kukhala achilendo kwa ine.
14 My kinsfolk have failed, and my familiar friends have forgotten me.
Abale anga andithawa; abwenzi anga andiyiwala.
15 Those who dwell in my house, and my maids, reckon me for a stranger; I am an alien in their sight.
Anthu odzacheza ku nyumba kwanga ndiponso antchito anga aakazi andisandutsa mlendo; ndasanduka mlendo mʼmaso mwawo.
16 I call to my servant, and he gives me no answer. I entreat him with my mouth.
Ndikayitana wa ntchito wanga, iye sandiyankha, ngakhale ndikapempha ndi pakamwa panga sandichitira kanthu.
17 My breath is strange to my wife, and my supplication to the sons of my own mother.
Mpweya wanga umamunyansa mkazi wanga; ndine chinthu chonyansa kwa abale anga a mimba imodzi.
18 Even young children despise me. If I arise, they speak against me.
Inde, ngakhale ana amandinyoza; akandiona amandinyodola.
19 All my familiar friends abhor me, and those whom I loved are turned against me.
Anzanga onse apamtima amanyansidwa nane; iwo amene ndinkawakonda andiwukira.
20 My bone cleaves to my skin and to my flesh, and I have escaped with the skin of my teeth.
Ndangotsala khungu ndi mafupa okhaokha; ndapulumuka lokumbakumba.
21 Have pity upon me, have pity upon me, O ye my friends, for the hand of God has touched me.
“Mvereni chisoni, inu abwenzi anga, mvereni chisoni, pakuti dzanja la Mulungu landikantha.
22 Why do ye persecute me as God, and are not satisfied with my flesh?
Chifukwa chiyani mukundilondola ngati Mulungu? Kodi simunatope nalo thupi langa?
23 O that my words were now written! O that they were inscribed in a book,
“Aa, achikhala mawu anga analembedwa, achikhala analembedwa mʼbuku,
24 that they were engraved in the rock forever with an iron pen and lead!
akanalembedwa pa mwala ndi chitsulo, akanalembedwa pa thanthwe kuti sangathe kufufutidwa!
25 But as for me I know that my Redeemer lives, and at last he will stand up upon the earth.
Koma ndikudziwa kuti mpulumutsi wanga ali ndi moyo, ndipo pa nthawi yomaliza adzabwera kudzanditeteza.
26 And after my skin, this body, is destroyed, then outside my flesh I shall see God,
Ndipo khungu langa litatha nʼkuwonongeka, mʼthupi langa lomweli ndidzamuona Mulungu.
27 whom I, even I, shall see on my side, and my eyes shall behold, and not as a stranger. My heart is consumed within me.
Ine ndemwe ndidzamuona Iye ndi maso angawa, ineyo, osati wina ayi. Ndithu mtima wanga ukufunitsitsadi!
28 If ye say, How we will persecute him! And that the root of the matter is found in me,
“Koma inu mukuti, ‘Haa! Tingamuzunze bwanji, popeza kuti zonsezi zaoneka chifukwa cha iye yemweyo?’
29 be ye afraid of the sword. For wrath brings the punishments of the sword, that ye may know there is a judgment.
Inu muyenera kuopa lupanga; pakuti mkwiyo wake umalangadi ndi lupanga; zikadzatero muzadziwa kuti chiweruzo chilipo ndithu.”

< Job 19 >