< Psalms 99 >

1 The LORD reigns! Let the peoples tremble. He sits enthroned among the cherubim. Let the earth be moved.
Yehova akulamulira, mitundu ya anthu injenjemere; Iye wakhala pa mpando wake waufumu, pakati pa akerubi, dziko lapansi ligwedezeke.
2 The LORD is great in Zion. He is high above all the peoples.
Mʼziyoni wamkulu ndi Yehova; Iye ndi wokwezeka pamwamba pa mitundu yonse ya anthu.
3 Let them praise your great and awesome name. He is Holy!
Anthu atamande dzina lanu lalikulu ndi loopsa kwambiri, Iye ndi woyera.
4 The King’s strength also loves justice. You establish equity. You execute justice and righteousness in Jacob.
Mfumu yamphamvu, iyo imakonda chilungamo Inu mwakhazikitsa khalidwe losakondera; mwachita zolungama ndi zoyenera mwa Yakobo.
5 Exalt the LORD our God. Worship at his footstool. He is Holy!
Kwezani Yehova Mulungu wathu ndipo mulambireni pa mapazi ake; Iye ndi woyera.
6 Moses and Aaron were among his priests, Samuel was among those who call on his name. They called on the LORD, and he answered them.
Mose ndi Aaroni anali ena mwa ansembe ake, Samueli anali pamodzi ndi iwo amene anayitana pa dzina lake; iwo anayitana Yehova ndipo Iyeyo anawayankha.
7 He spoke to them in the pillar of cloud. They kept his testimonies, the statute that he gave them.
Iye anayankhula nawo kuchokera mʼchipilala cha mtambo; iwo anasunga malamulo ake ndi zophunzitsa zomwe anawapatsa.
8 You answered them, LORD our God. You are a God who forgave them, although you took vengeance for their doings.
Inu Yehova Mulungu wathu, munawayankha iwo; Inu kwa Israeli munali Mulungu wokhululuka, ngakhale munawalanga pa zochita zawo zoyipa.
9 Exalt the LORD, our God. Worship at his holy hill, for the LORD, our God, is holy!
Kwezani Yehova Mulungu wathu ndipo mumulambire pa phiri lake loyera, pakuti Yehova Mulungu wathu ndi woyera.

< Psalms 99 >