< 1 Peter 4 >

1 Since Christ has suffered in the flesh, you also should be armed with the same intention. For he who suffers in the flesh desists from sin,
Popeza kuti Khristu anamva zowawa mʼthupi lake, mukhale nawonso mtima omwewo, chifukwa iye amene wamva zowawa mʼthupi lake walekana nawo uchimo.
2 so that now he may live, for the remainder of his time in the flesh, not by the desires of men, but by the will of God.
Chifukwa cha ichi, iwo sakhalanso moyo wawo akuchita zofuna za matupi awo, koma amachita chifuniro cha Mulungu.
3 For the time that has passed is sufficient to have fulfilled the will of the Gentiles, those who have walked in luxuries, lusts, intoxication, feasting, drinking, and the illicit worship of idols.
Pakuti mwataya kale nthawi yambiri mʼmbuyomu pochita zimene anthu osapembedza amachita, moyo wokhumba zonyansa, zilakolako zoyipa kuledzera, zochitika zoyipa za pa phwando, mapokoso ndi kupembedza mafano onyansa.
4 About this, they wonder why you do not rush with them into the same confusion of indulgences, blaspheming.
Anthu osapembedza amadabwa pamene simuthamangira nawo kuchita zoyipitsitsazi, nʼchifukwa chake amakuchitani chipongwe.
5 But they must render an account to him who is prepared to judge the living and the dead.
Koma adzafotokoza okha mlandu wawo kwa Mulungu amene wakonzeka kuweruza amoyo ndi akufa.
6 For because of this, the Gospel was also preached to the dead, so that they might be judged, certainly, just like men in the flesh, yet also, so that they might live according to God, in the Spirit.
Pa chifukwa chimenechi, Uthenga Wabwino unalalikidwa ngakhale kwa iwo amene tsopano ndi akufa, kuti adzaweruzidwe monga anthu ku thupi, koma adzakhale ndi moyo monga mwa Mulungu mu mzimu.
7 But the end of everything draws near. And so, be prudent, and be vigilant in your prayers.
Chimaliziro cha zinthu zonse chili pafupi. Choncho khalani maso ndi odziletsa kuti muthe kupemphera.
8 But, before all things, have a constant mutual charity among yourselves. For love covers a multitude of sins.
Koposa zonse muzikondana wina ndi mnzake kwambiri, chifukwa chikondi chimaphimba machimo ambiri.
9 Show hospitality to one another without complaining.
Muzisamalirana wina ndi mnzake osamanyinyirika.
10 Just as each of you has received grace, minister in the same way to one another, as good stewards of the manifold grace of God.
Aliyense agwiritse ntchito mokhulupirika mphatso iliyonse imene anayilandira potumikira ena ngati adindo ogwiritsa bwino ntchito mphatso za Mulungu za mitundumitundu.
11 When anyone speaks, it should be like words of God. When anyone ministers, it should be from the virtue that God provides, so that in all things God may be honored through Jesus Christ. To him is glory and dominion forever and ever. Amen. (aiōn g165)
Ngati wina ayankhula, ayankhuledi mawu enieni a Mulungu. Ngati wina atumikira, atumikire ndi mphamvu imene Mulungu amapereka, kuti pa zonse Mulungu alemekezedwe mwa Yesu Khristu. Kwa Iye kukhale ulemerero ndi mphamvu mpaka muyaya, Ameni. (aiōn g165)
12 Most beloved, do not choose to sojourn in the passion which is a temptation to you, as if something new might happen to you.
Abale okondedwa musadabwe ndi mayesero owawa amene mukukumana nawo ngati kuti china chake chachilendo chakuchitikirani.
13 But instead, commune in the Passion of Christ, and be glad that, when his glory will be revealed, you too may rejoice with exultation.
Koma kondwerani popeza mukumva zowawa pamodzi ndi Khristu, kuti mudzakondwere kwakukulu pamene ulemerero wake udzaonekera.
14 If you are reproached for the name of Christ, you will be blessed, because that which is of the honor, glory, and power of God, and that which is of his Spirit, rests upon you.
Ngati akuchitani chipongwe chifukwa cha dzina la Khristu, ndinu odala, ndiye kuti Mzimu waulemerero wa Mulungu uli pa inu.
15 But let none of you suffer for being a murderer, or a thief, or a slanderer, or one who covets what belongs to another.
Ngati mumva zowawa, zisakhale chifukwa cha kupha munthu, kapena kuba, kapena kuchita choyipa, kapena kulowerera za anthu ena,
16 But if one of you suffers for being a Christian, he should not be ashamed. Instead, he should glorify God in that name.
koma ngati mumva zowawa chifukwa ndinu Mkhristu, musachite manyazi, koma muyamike Mulungu chifukwa cha dzinalo.
17 For it is time that judgment begin at the house of God. And if it is first from us, what shall be the end of those who do not believe the Gospel of God?
Pakuti nthawi yafika kuti chiweruzo chiyambe mʼnyumba ya Mulungu, ndipo ngati chiyamba ndi ife nanga podzafika kwa osamvera Uthenga Wabwino wa Mulungu, chidzakhala chotani?
18 And if the just man will scarcely be saved, where will the impious and the sinner appear?
Monga Malemba akuti, “Ngati kuli kovuta kuti olungama apulumuke, nanga munthu wochimwa, wosasamala za Mulungu adzatani?”
19 Therefore, too, let those who suffer according to the will of God commend their souls by good deeds to the faithful Creator.
Nʼchifukwa chake, iwo amene akumva zowawa monga mwa chifuniro cha Mulungu, adzipereke okha mʼmanja mwa Mlengi wawo wokhulupirika ndi kumapitiriza kuchita zabwino.

< 1 Peter 4 >