< Hebrews 6 >

1 Therefore, interrupting an explanation of the basics of Christ, let us consider what is more advanced, not presenting again the fundamentals of repentance from dead works, and of faith toward God,
Tsono tiyeni tisangoyima pa maphunziro oyambirira enieni a Khristu koma tipitirire kuti mukule msinkhu. Tisaphunzitsenso zinthu zomwe zili ngati maziko, monga za kutembenuka mtima kusiya ntchito zosapindulitsa pa moyo wosatha, za kukhulupirira Mulungu,
2 of the doctrine of baptism, and also of the imposition of hands, and of the resurrection of the dead, and of eternal judgment. (aiōnios g166)
za maubatizo, za kusanjika manja, za kuuka kwa akufa ndi za chiweruzo chotsiriza. (aiōnios g166)
3 And we shall do this, if indeed God permits it.
Ndipo Mulungu akalola, tidzaterodi.
4 For it is impossible for those who were once illuminated, and have even tasted of the heavenly gift, and have become sharers in the Holy Spirit,
Nʼkosatheka kuwabwezanso anthu amene nthawi ina anawunikiridwa. Iwowa analawapo mphatso yochokera kumwamba, nʼkulandira nawo Mzimu Woyera.
5 who, despite having tasted the good Word of God and the virtues of the future age, (aiōn g165)
Analawa kukoma kwa mawu a Mulungu ndi mphamvu za nthawi ikubwera. (aiōn g165)
6 have yet fallen away, to be renewed again to penance, since they are crucifying again in themselves the Son of God and are still maintaining pretenses.
Popeza anabwerera mʼmbuyo, nʼkosatheka kuti atembenukenso mtima chifukwa akupachikanso Mwana wa Mulungu ndi kumunyozetsa poyera.
7 For the earth accepts a blessing from God, by drinking in the rain that often falls upon it, and by producing plants that are useful to those by whom it is cultivated.
Nthaka yolandira mvula kawirikawiri nʼkubala mbewu zopindulitsa oyilima, Mulungu amayidalitsa.
8 But whatever brings forth thorns and briers is rejected, and is closest to what is accursed; their consummation is in combustion.
Koma nthaka yobereka minga ndi nthula ndi yopanda phindu ndipo ili pafupi kutembereredwa. Matsiriziro ake idzatenthedwa mʼmoto.
9 But from you, most beloved, we are confident that there will be things better and closer to salvation; even though we speak in this way.
Okondedwa anga, ngakhale tikuyankhula zimenezi, ife tikudziwa kuti muli nazo zinthu zabwino zomwe zimabwera pamodzi ndi chipulumutso.
10 For God is not unjust, such that he would forget your work and the love that you have shown in his name. For you have ministered, and you continue to minister, to the saints.
Mulungu ndi wolungama, sangayiwale ntchito zanu ndi chikondi chanu chimene munamuonetsa pothandiza anthu ake monga mmene mukuchitirabe tsopano.
11 Yet we desire that each one of you display the same solicitude toward the fulfillment of hope, even unto the end,
Ife tikufuna kuti aliyense wa inu aonetse changu chomwechi mpaka kumapeto, kuti zichitikedi zomwe mukuyembekezera.
12 so that you may not be slow to act, but instead may be imitators of those who, through faith and patience, shall inherit the promises.
Ife sitikufuna kuti inu mukhale aulesi, koma mutsatire anthu amene, pokhulupirira ndi kupirira, akulandira zimene zinalonjezedwa.
13 For God, in making promises to Abraham, swore by himself, (because he had no one greater by whom he might swear),
Pamene Mulungu ankamulonjeza Abrahamu, popeza panalibe wamkulu womuposa, amene akanamutchula ndikulumbira mwa Iye, analumbira mwa Iye yekha kuti,
14 saying: “Blessing, I shall bless you, and multiplying, I shall multiply you.”
“Ine ndidzakudalitsa ndithu, ndipo ndidzakupatsa zidzukulu zambiri.”
15 And in this way, by enduring patiently, he secured the promise.
Ndipo Abrahamu atayembekezera mofatsa, analandira zimene anamulonjezazo.
16 For men swear by what is greater than themselves, and an oath as confirmation is the end of all their controversy.
Anthu amalumbira mʼdzina la wina amene akuwaposa, ndipo lumbiro lotere limatsimikizira zomwe zayankhulidwa ndi kuthetsa mikangano yonse.
17 In this matter, God, wanting to reveal more thoroughly the immutability of his counsel to the heirs of the promise, interposed an oath,
Momwemonso Mulungu pofuna kutsimikizira anthu amene adzalandire lonjezo, kuti Iye sangasinthe maganizo, anatsimikiza lonjezo lakelo ndi lumbiro.
18 so that by two immutable things, in which it is impossible for God to lie, we may have the strongest solace: we who have fled together so as to hold fast to the hope set before us.
Mulungu anachita zinthu ziwiri, lonjezo ndi lumbiro, zimene sizingathe kusintha ndipo Mulungu sangathe kunama. Choncho Mulungu akutilimbikitsa mtima ife amene tinathawira kwa Iye kuti tichigwiritsitse chiyembekezo chimene tinalandira.
19 This we have as an anchor of the soul, safe and sound, which advances even to the interior of the veil,
Chiyembekezo chimenechi tili nacho ngati nangula wa moyo wathu. Nʼchokhazikika ndi chosagwedezeka ndipo chimalowa mʼkatikati mwa malo opatulika, kuseri kwa chinsalu chotchinga.
20 to the place where the forerunner Jesus has entered on our behalf, so as to become the High Priest for eternity, according to the order of Melchizedek. (aiōn g165)
Yesu anatitsogolera kupita kumeneko, nalowako mʼmalo mwathu. Iye anasanduka Mkulu wa ansembe onse wamuyaya, monga mwa dongosolo la unsembe wa Melikizedeki. (aiōn g165)

< Hebrews 6 >