< 1 Samuel 10 >

1 Then Samuel tooke a viole of oyle and powred it vpon his head, and kissed him, and saide, Hath not the Lord anointed thee to be gouernour ouer his inheritance?
Ndipo Samueli anatenga botolo la mafuta nathira mafutawo pa mutu wa Sauli ndipo anapsompsona nati, “Yehova wakudzoza kuti ukhale mtsogoleri wa anthu ake, Aisraeli. Iwe udzalamulira anthu a Yehova ndiponso udzawapulumutsa mʼmanja mwa adani awo owazungulira. Chizindikiro chakuti Yehova wakudzoza kuti ukhale mtsogoleri wa anthu ake ndi ichi:
2 When thou shalt depart from me this day, thou shalt finde two men by Rahels sepulchre in the border of Beniamin, euen at Zelzah, and they will say vnto thee, The asses which thou wentest to seeke, are founde: and lo, thy father hath left the care of the asses, and soroweth for you, saying, What shall I doe for my sonne?
Ukachoka pano lero lino, udzakumana ndi amuna awiri kufupi ndi manda a Rakele ku Zeliza mʼmalire mwa dziko la Benjamini ndipo adzakuwuza kuti, ‘Abulu amene munkafunafuna aja apezeka. Ndipo tsopano abambo ako asiya kuganiza za abulu ndipo akudera nkhawa za iwe.’ Iwo akufunsa kuti, ‘Kodi ndidzachita chiyani mmene mwana wanga sakuoneka?’”
3 Then shalt thou go forth from thence and shalt come to the plaine of Tabor, and there shall meete thee three men going vp to God to Bethel: one carying three kiddes, and an other carying three loaues of bread, and another carying a bottle of wine:
“Ndipo udzapyola pamenepo ndi kufika ku mtengo wa thundu wa ku Tabori. Kumeneko udzakumana ndi anthu atatu akupita kukapereka nsembe ku Nyumba ya Mulungu ku Beteli. Mmodzi adzakhala atanyamula ana ambuzi atatu, wina atanyamula malofu atatu a buledi, ndi winayo atanyamula thumba la vinyo.
4 And they will aske thee if all be well, and will giue thee the two loaues of bread, which thou shalt receiue of their handes.
Adzakupatsa moni ndi kukupatsa malofu awiri a buledi. Iwe udzalandire bulediyo.
5 After that shalt thou come to the hill of God, where is the garisons of the Philistims: and when thou art come thither to the citie, thou shalt meete a companie of Prophets comming downe from the hie place with a viole, and a tymbrell, and a pipe, and an harpe before them, and they shall prophecie.
“Pambuyo pake, udzafike ku Gibeyati-Elohimu, kumene kuli gulu la ankhondo la Afilisti. Pamene ukuyandikira mzindawo, udzakumana ndi gulu la aneneri akutsika kuchokera ku phiri, akuyimba zeze, ngʼoma, zitoliro ndi pangwe, ndiponso akulosera.
6 Then the Spirit of the Lord will come vpon thee, and thou shalt prophecie with them, and shalt be turned into another man.
Kenaka Mzimu wa Yehova udzabwera pa iwe ndi mphamvu, ndipo udzayamba kulosera nawo pamodzi. Ndipo udzasinthika kukhala munthu wina.
7 Therefore when these signes shall come vnto to thee, doe as occasion shall serue: for God is with thee.
Zizindikiro izi zikakachitika, dzachite chilichonse manja ako angathe kuchita, pakuti Mulungu ali nawe.
8 And thou shalt goe downe before me to Gilgal: and I also will come downe vnto thee to offer burnt offerings, and to sacrifice sacrifices of peace. Tary for me seuen dayes, till I come to thee and shewe thee what thou shalt doe.
“Tsono tsogola kupita ku Giligala. Ine ndidzabwera ndithu kudzapereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano. Koma ukandidikire masiku asanu ndi awiri mpaka ine nditabwera kuti ndidzakuwuze zomwe udzachite.”
9 And when he had turned his backe to goe from Samuel, God gaue him another heart: and all those tokens came to passe that same day.
Sauli akutembenuka kusiyana ndi Samueli, Mulungu anasintha mtima wa Sauli, ndipo zinthu zonsezi zinakwaniritsidwa tsiku lomwelo.
10 And when they came thither to the hill, beholde, the companie of Prophets meete him, and the Spirit of God came vpon him, and he prophecied among them.
Atafika ku Gibeya, anakumana ndi gulu la aneneri. Mzimu wa Mulungu unabwera pa iye mwamphamvu, nayamba kulosa nawo.
11 Therefore all the people that knewe him before, when they saw that he prophecied among the Prophets, saide eche to other, What is come vnto the sonne of Kish? is Saul also among the Prophets?
Pamene onse amene ankamudziwa kale anamuona akulosera pamodzi ndi aneneri, anafunsana wina ndi mnzake. “Kodi nʼchiyani chachitika ndi mwana wa Kisi? Kodi Sauli alinso mʼgulu la aneneri?”
12 And one of the same place answered, and said, But who is their father? Therefore it was a prouerbe, Is Saul also among the Prophets?
Munthu wina wa kumeneko anayankha kuti, “Nanga enawa abambo awo ndani?” Kotero kunayambika mwambi wakuti, “Kodi Saulinso ali mʼgulu la aneneri?”
13 And when he had made an ende of prophecying, he came to the hie place.
Sauli atasiya kuloserako, anapita ku kachisi ku phiri.
14 And Sauls vncle saide vnto him, and to his seruant, Whither went ye? And he saide, To seeke the asses: and when we sawe that they were no where, we came to Samuel.
Tsono amalume ake a Sauli anamufunsa ndi mnyamata wake kuti, “Munapita kuti?” Iye anayakha, “Timakafunafuna abulu koma titaona kuti sakupezeka, tinapita kwa Samueli.”
15 And Sauls vncle saide, Tell me, I pray thee, what Samuel said vnto you.
Amalume ake a Sauli anati, “Chonde, ndifotokozereniko zimene Samueli wakuwuzani.”
16 Then Saul saide to his vncle, He tolde vs plainely that the asses were founde: but concerning the kingdome whereof Samuel spake, tolde he him not.
Sauli anati, “Iye anatitsimikizira kuti abulu anapezeka.” Koma sanawawuze amalume akewo za nkhani ija ya ufumu imene Samueli anamuwuza.
17 And Samuel assembled the people vnto the Lord in Mizpeh,
Samueli anayitana Aisraeli onse kuti asonkhane pamaso pa Yehova ku Mizipa.
18 And he saide vnto the children of Israel, Thus saith ye Lord God of Israel, I haue brought Israel out of Egypt, and deliuered you out of the hand of the Egyptians, and out of the handes of all kingdomes that troubled you.
Ndipo anawuza Aisraeli onse kuti, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ine ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto ndi kukupulumutsani mʼdzanja la Igupto ndi mʼdzanja la mafumu onse amene ankakuzunzani.’
19 But ye haue this day cast away your God, who onely deliuereth you out of all your aduersities and tribulations: and ye said vnto him, No, but appoint a King ouer vs. Nowe therefore stand ye before the Lord according to your tribes, and according to your thousands.
Koma lero mwamukana Mulungu wanu amene amakupulumutsani mʼmavuto anu onse ndi mʼzowawa zanu. Ndipo mukuti, ‘Ayi, koma mutipatse mfumu yotilamulira.’ Tsopanotu sonkhanani pamaso pa Yehova mwa mafuko ndi mabanja anu.”
20 And when Samuel had gathered together all the tribes of Israel, the tribe of Beniamin was taken.
Samueli atasonkhanitsa mafuko onse a Israeli, fuko la Benjamini linasankhidwa.
21 Afterwarde he assembled the tribe of Beniamin according to their families, and the familie of Matri was taken. So Saul the sonne of Kish was taken, and when they sought him, he coulde not be found.
Anasonkhanitsa fuko la Benjamini banja ndi banja. Pomaliza anasonkhanitsa banja la Matiri mmodzimmodzi ndipo Sauli mwana wa Kisi anasankhidwa. Koma atamufunafuna, sanamupeze.
22 Therefore they asked the Lord againe, if that man should yet come thither. And the Lord answered, Beholde, he hath hid himselfe among the stuffe.
Tsono anthu anafunsanso kwa Yehova kuti, “Kodi munthuyu wabwera kale kuno?” Ndipo Yehova anayankha kuti, “Inde wabisala pakati pa katundu.”
23 And they ranne, and brought him thence: and when he stoode among the people, he was hier then any of the people from the shoulders vpwarde.
Iwo anathamanga ndi kukamutenga kumeneko. Atayimirira pakati pa anthu anapezeka kuti anali wamtali kuposa anthu ena mwakuti ankamulekeza mʼmapewa.
24 And Samuel saide to all the people, See ye not him, whom the Lord hath chosen, that there is none like him among all the people? and all the people shouted and saide, God saue the King.
Samueli anafunsa anthu onse kuti, “Kodi mukumuona munthu amene Yehova wasankha? Palibe wofanana naye pakati pa anthu onse.” Kenaka anthu onse anafuwula kuti, “Mfumu ikhale ndi moyo wautali!”
25 Then Samuel tolde the people the duetie of the kingdome, and wrote it in a booke, and laied it vp before the Lord, and Samuel sent all the people away euery man to his house.
Samueli anafotokozera anthu ntchito ndi udindo wa mfumu. Pambuyo pake analemba mʼbuku zonse zokhudza ntchito ndi udindo wa mfumu, ndipo bukulo analiyika pamaso pa Yehova. Kenaka Samueli analola aliyense kuti abwerere kupita kwawo.
26 Saul also went home to Gibeah, and there followed him a bande of men, whose heart God had touched,
Sauli anapitanso ku mudzi kwawo ku Gibeya, pamodzi ndi anthu amphamvu amene Mulungu anawafewetsa mitima.
27 But the wicked men saide, Howe shall hee saue vs? So they despised him, and brought him no presents: but he held his tongue.
Koma anthu ena achabechabe anati, “Kodi munthu uyu angathe bwanji kutipulumutsa?” Iwo anayamba kumunyoza Sauliyo, ndipo sankamupatsa ngakhale mphatso. Koma iye sanalabadireko.

< 1 Samuel 10 >