< Deuteronomy 29 >

1 These are the wordes of the couenant which the Lord commanded Moses to make with the children of Israel in the lande of Moab beside the couenant which hee had made with them in Horeb.
Awa ndiwo mawu a mʼpangano limene Yehova analamula Mose kuti achite ndi Aisraeli ku Mowabu, powonjezera pa pangano limene anapangana nawo ku Horebu.
2 And Moses called all Israel, and said vnto them, Ye haue seene all that the Lord did before your eyes in the lande of Egypt vnto Pharaoh and vnto all his seruantes, and vnto all his lande,
Mose anayitanitsa Aisraeli onse nati kwa iwo: Inu munaona zonse zimene Yehova anachita kwa Farao, nduna zake ndi dziko lake lonse ku Igupto.
3 The great tentations which thine eyes haue seene, those great miracles and wonders:
Ndi maso anu munaona mayesero onse aja, zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa zazikulu zija.
4 Yet the Lord hath not giuen you an heart to perceiue, and eyes to see, and eares to heare, vnto this day.
Koma mpaka lero Yehova sanakupatseni mtima wozindikira kapena maso openya kapena makutu akumva.
5 And I haue led you fourty yere in the wildernesse: your clothes are not waxed olde vpon you, neyther is thy shooe waxed olde vpon thy foote.
Mʼzaka makumi anayi zimene ndinakutsogolerani mʼchipululu, zovala zanu ndiponso nsapato za ku mapazi anu sizinangʼambike.
6 Ye haue eaten no bread, neither drunke wine, nor strong drinke, that ye might know how that I am the Lord your God.
Inu simunadye buledi ndi kumwa vinyo kapena chakumwa chilichonse choledzeretsa. Ndinachita izi kuti mudziwe kuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
7 After, ye came vnto this place, and Sihon King of Heshbon, and Og King of Bashan came out against vs vnto battell, and we slewe them,
Pamene munafika malo ano, Sihoni mfumu ya ku Hesiboni ndi Ogi mfumu ya ku Basani anabwera kudzamenyana nafe koma tinawagonjetsa iwo.
8 And tooke their lande, and gaue it for an inheritance vnto the Reubenites, and to the Gadites, and to the halfe tribe of Manasseh.
Tinatenga dziko lawo ndi kulipereka ngati cholowa cha fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase.
9 Keepe therefore the wordes of this couenant and doe them, that ye may prosper in all that ye shall doe.
Tsatirani mosamalitsa mawu a mʼpangano ili kuti zinthu zizikuyenderani bwino pa zochitika zanu zonse.
10 Ye stand this day euery one of you before the Lord your God: your heads of your tribes, your Elders and your officers, eue al ye me of Israel:
Lero lino nonse mukuyima pamaso pa Yehova Mulungu wanu, atsogoleri a mafuko anu, akuluakulu ndi nduna zanu, ndi amuna ena onse a mu Israeli,
11 Your children, your wiues, and thy stranger that is in thy campe from the hewer of thy wood, vnto the drawer of thy water,
pamodzi ndi ana ndi akazi anu, kudzanso alendo amene akukhala pakati panu omwe amakuwazirani nkhuni ndi kukutungirani madzi.
12 That thou shouldest passe into the couenant of the Lord thy God, and into his othe which the Lord thy God maketh with thee this day,
Mukuyimirira pano kuti mulowe mʼpangano ndi Yehova Mulungu wanu, pangano limene Yehova akuchita ndi inu lero ndi kulisindikiza ndi malumbiro,
13 For to establish thee this day a people vnto him selfe, and that he may be vnto thee a God, as he hath said vnto thee, and as he hath sworne vnto thy fathers, Abraham, Izhak, and Iaakob.
kukukhazikitsani lero lino ngati anthu ake, ndi kuti Iye akhale Mulungu wanu monga anakulonjezani inu ndiponso monga analumbira kwa makolo anu Abrahamu, Isake ndi Yakobo.
14 Neither make I this couenant, and this othe with you onely,
Ndikupanga pangano ili ndi malumbiro ake osati kwa inu nokha,
15 But aswel with him that standeth here with vs this day before the Lord our God, as with him that is not here with vs this day.
amene muli pano pamaso pa Yehova Mulungu wathu, koma ndi iwonso amene sali pano lero.
16 For ye knowe, how we haue dwelt in the land of Egypt, and how we passed thorowe the middes of the nations, which ye passed by.
Inu nomwe mukudziwa mmene tinkakhalira ku Igupto ndi mmene tinadutsira mayiko pa ulendo wobwera kuno.
17 And ye haue seene their abominations and their idoles (wood, and stone, siluer and golde) which were among them,
Ife tinaona pakati pawo mafanizo ndi mafano awo onyansa, amtengo ndi amiyala, asiliva ndi agolide.
18 That there should not be among you man nor woman, nor familie, nor tribe, which should turne his heart away this day from the Lord our God, to goe and serue the gods of these nations, and that there shoulde not be among you any roote that bringeth forth gall and wormewood,
Onetsetsani kuti pasapezeke mwamuna kapena mkazi, banja kapena fuko pakati panu lero amene mtima wawo udzapandukira Yehova Mulungu wanu ndi kupita kukapembedza milungu ya mitundu iyo. Onetsetsani kuti pasapezeke muzu pakati panu wotulutsa mankhwala akupha otere.
19 So that when he heareth the words of this curse, he blesse him selfe in his heart, saying, I shall haue peace, although I walke according to the stubburnes of mine owne heart, thus adding drunkennesse to thirst.
Munthu wotere akamva mawu a lumbiro ili, asadzidalitse yekha mʼmaganizo mwake namati, “Ine ndidzapulumuka ngakhale nditapitiriza kuyenda njira yanga.” Zoterezi zidzadzetsa masautso pa nthaka ya chinyontho ndi yowuma yomwe.
20 The Lord will not be mercifull vnto him, but then the wrath of the Lord and his ielousie shall smoke against that man, and euery curse that is written in this booke, shall light vpon him, and the Lord shall put out his name from vnder heauen,
Yehova sadzamukhululukira. Mkwiyo ndi nsanje ya Yehova zidzamuyakira munthuyo. Matemberero onse wolembedwa mʼbukuli adzamugwera iye ndipo Yehova adzafafaniza dzina lake pa dziko lapansi.
21 And the Lord shall separate him vnto euil out of all the tribes of Israel, according vnto all the curses of the couenant, that is written in the booke of this Lawe.
Yehova adzasankha pakati pa Aisraeli anthu oyenera masautso monga mwa matemberero onse a mʼpangano olembedwa Mʼbuku la Malamulo.
22 So that the generatio to come, euen your children, that shall rise vp after you, and the stranger, that shall come from a farre lande, shall say, when they shall see the plagues of this lande, and the diseases thereof, wherewith the Lord shall smite it:
Ana anu a mibado yakutsogolo ndi alendo amene adzachokera kutali adzaona matsoka amene adzakugwerani mʼdziko muno ndiponso matenda amene Yehova adzabweretsa pa dzikoli.
23 (For all that land shall burne with brimstone and salt: it shall not be sowen, nor bring forth, nor any grasse shall growe therein, like as in the ouerthrowing of Sodom, and Gomorah, Admah, and Zeboim, which the Lord ouerthrewe in his wrath and in his anger)
Dziko lonse lidzasanduka nthaka ya mchere ndi ya sulufule. Simudzadzalamo kanthu, simudzakhala chomera chilichonse, ndi mbewu yomera mʼmenemo. Dziko lanu lidzakhala lowonongeka ngati Sodomu ndi Gomora, Adima ndi Zeboimu, mizinda imene Yehova anayiwononga ndi mkwiyo wake waukulu.
24 Then shall all nations say, Wherefore hath the Lord done thus vnto this lande? how fierce is this great wrath?
Mitundu yonse ya anthu idzafunsa kuti, “Kodi chifukwa chiyani Yehova anachita zotere mʼdziko lake? Kodi chifukwa chiyani anaonetsa mkwiyo woopsa wotere?”
25 And they shall answere, Because they haue forsaken the couenant of the Lord God of their fathers, which he had made with them, when he brought them out of the land of Egypt,
Ndipo yankho la mafunso amenewa lidzakhala lakuti, “Chifukwa chakuti anthu awa aphwanya pangano la Yehova Mulungu wa makolo awo, pangano limene Iye anapangana nawo pamene anawatulutsa ku Igupto.
26 And went and serued other gods and worshipped them: euen gods which they knewe not, and which had giuen them nothing,
Iwo anachoka ndi kukatumikira milungu ina ndi kuyipembedza, milungu imene sanayidziwe, milungu imene sanawapatse.
27 Therefore the wrath of the Lord waxed hot against this land, to bring vpon it euery curse that is written in this booke.
Choncho Yehova anakwiyira dziko lino, kotero anabweretsa matemberero onse amene analembedwa mʼbuku lino.
28 And ye Lord hath rooted them out of their land in anger, and in wrath, and in great indignation, and hath cast them into another land, as appeareth this day.
Ndi mkwiyo komanso ukali wake woopsa Yehova anawazula mʼdziko lawo ndi kuwaponyera mʼdziko lina, monga mmene zilili lero lino.”
29 The secret things belong to the Lord our God, but the things reueiled belong vnto vs, and to our children for euer, that we may doe all the wordes of this Lawe.
Zinsinsi ndi za Yehova Mulungu wathu koma zinthu zimene zaululidwa ndi zathu ndi ana athu kwamuyaya, kuti titsatire mawu onse a mʼmalamulowa.

< Deuteronomy 29 >