< Exodus 5 >

1 Then afterwarde Moses and Aaron went and said to Pharaoh, Thus saith the Lord God of Israel, Let my people go, that they may celebrate a feast vnto me in the wildernesse.
Zitachitika izi, Mose ndi Aaroni anapita kwa Farao ndipo anati, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Aloleni anthu anga apite, kuti akachite chikondwerero cha Ine mʼchipululu.’”
2 And Pharaoh saide, Who is the Lord, that I should heare his voyce, and let Israel go? I knowe not the Lord, neither will I let Israel goe.
Koma Farao anati, “Yehova ndani kuti ine ndimumvere ndi kulola Aisraeli kuti apite? Ine Yehova sindikumudziwa ndipo sindilola kuti Aisraeli apite.”
3 And they saide, We worship the God of the Ebrewes: we pray thee, let vs goe three daies iourney in the desert, and sacrifice vnto the Lord our God, least he bring vpon vs the pestilence or sword.
Ndipo iwo anati, “Mulungu wa Ahebri anakumana nafe. Chonde tiloleni tipite ulendo wa masiku atatu ku chipululu kuti tikapereke nsembe kwa Yehova Mulungu wathu, ngati sititero iye adzatipweteka ndi miliri kapena lupanga.”
4 Then saide the King of Egypt vnto them, Moses and Aaron, why cause ye the people to cease from their workes? get you to your burdens.
Koma mfumu ya Igupto inati, “Mose ndi Aaroni, chifukwa chiyani mukuchititsa anthuwa kuti asagwire ntchito zawo? Bwererani ku ntchito zanu!”
5 Pharaoh saide furthermore, Behold, much people is nowe in the lande, and ye make them leaue their burdens.
Ndiponso Farao anati, “Taonani, anthuwa mʼdziko muno alipo ochuluka, ndipo inu mukuwaletsa kugwira ntchito.”
6 Therefore Pharaoh gaue commandement the same day vnto the taskemasters of the people, and to their officers, saying,
Pa tsiku lomwelo Farao analamulira akapitawo a thangata ndi anzawo a Chiisraeli amene ankayangʼanira anthu kuti
7 Ye shall giue the people no more strawe, to make bricke (as in time past) but let them goe and gather them strawe them selues:
“Inu musawapatsenso udzu wopangira njerwa monga mumachitira kale, iwo azipita ndi kukatenga udzu wawo.
8 Notwithstanding lay vpon them the nober of bricke, which they made in time past, diminish nothing thereof: for they be idle, therefore they crie, saying, Let vs go to offer sacrifice vnto our God.
Koma musawachepetsere chiwerengero cha njerwa chomwe munawalamulira kale kuti aziwumba. Iwowa ndi aulesi. Nʼchifukwa chake akulira kuti, ‘Tiloleni tipite tikapereke nsembe kwa Mulungu wathu.’
9 Lay more worke vpon the men, and cause them to do it, and let the not regard vaine words.
Muwakhawulitse ndi ntchito anthu amenewa kuti azitanganidwa, asakhale ndi mpata omvera zabodza.”
10 Then went the taskemasters of the people and their officers out, and tolde the people, saying, Thus saith Pharaoh, I will giue you no more strawe.
Choncho akapitawo a thangata ndi anzawo a Chiisraeli amene ankayangʼanira anthu anapita kwa anthu aja nati, “‘Farao akuti sadzakupatsaninso udzu.
11 Goe your selues, get you strawe where yee can finde it, yet shall nothing of your labour bee diminished.
Mʼmalo mwake mupite mukadzimwetere udzu kulikonse kumene mungawupeze. Komabe ntchito yanu sichepetsedwa.’”
12 Then were the people scattered abroade throughout all the land of Egypt, for to gather stubble in steade of strawe.
Kotero anthuwo anamwazikana mʼdziko lonse la Igupto kukamweta udzu.
13 And the taskemasters hasted them, saying, Finish your dayes worke euery dayes taske, as ye did when ye had strawe.
Akapitawo a thangata aja anawafulumiza anthu aja nati, “Malizani kugwira ntchito yanu ya tsiku ndi tsiku monga mmene zinalili pamene munkapatsidwa udzu.”
14 And the officers of the children of Israel, which Pharaohs taskemasters had set ouer them, were beaten, and demanded, Wherefore haue ye not fulfilled your taske in making bricke yesterday and to daye, as in times past?
Akapitawo a thangata a Farao ankawamenya oyangʼanira anzawo a Chiisraeli aja nawapanikiza kuti, “Chifukwa chiyani lero simunawumbe chiwerengero chovomerezeka cha njerwa monga chakale chija?”
15 Then the officers of the children of Israel came, and cryed vnto Pharaoh, saying, Wherfore dealest thou thus with thy seruants?
Pamenepo oyangʼanira anzawo a Chiisraeli aja anapita kukadandaula kwa Farao kuti, “Chifukwa chiyani mwachitira antchito anu zotere?
16 There is no strawe giuen to thy seruantes, and they say vnto vs, Make bricke: and loe, thy seruants are beaten, and thy people is blamed.
Antchito anu sakupatsidwa udzu, komabe akutiwuza kuti, ‘Umbani njerwa!’ Antchito anu akumenyedwa, koma cholakwa sichili ndi anthu anu.”
17 But he said, Ye are to much idle: therfore ye say, Let vs goe to offer sacrifice to the Lord.
Farao anati, “Ulesi, inu ndinu alesi! Nʼchifukwa chake mukumanena kuti, ‘Mutilole tipite kukapereka nsembe kwa Yehova.’
18 Goe therefore nowe and worke: for there shall no strawe be giuen you, yet shall yee deliuer the whole tale of bricke.
Pitani tsopano kuntchito. Simudzapatsidwanso udzu komabe muyenera kuwumba muyeso wanu wovomerezeka wa njerwa.”
19 Then the officers of the children of Israel sawe them selues in an euill case, because it was saide, Ye shall diminish nothing of your bricke, nor of euery dayes taske.
Oyangʼanira anzawo a Chiisraeli anazindikira kuti ali pa mavuto pamene anawuzidwa kuti, “Musachepetse chiwerengero cha njerwa chimene muyenera kuwumba tsiku lililonse.”
20 And they met Moses and Aaron, which stood in their way as they came out from Pharaoh,
Atachoka pamaso pa Farao, anakumana ndi Mose ndi Aaroni akuwadikira,
21 To whom they said, The Lord looke vpon you and iudge: for yee haue made our sauour to stinke before Pharaoh and before his seruants, in that ye haue put a sword in their hand to slay vs.
ndipo iwo anati, “Yehova akupenyeni ndi kukuweruzani popeza mwachititsa Farao ndi nduna zake kuti anyansidwe nafe ndipo mwayika lupanga mʼmanja mwawo kuti atiphe.”
22 Wherefore Moses returned to the Lord, and saide, Lord, why hast thou afflicted this people? wherefore hast thou thus sent me?
Mose anabwerera kwa Yehova ndipo anati, “Chonde Ambuye, chifukwa chiyani mukuzunza anthu anu? Kodi munanditumira zimenezi?
23 For since I came to Pharaoh to speake in thy Name, he hath vexed this people, and yet thou hast not deliuered thy people.
Chipitireni changa kwa Farao kukamuyankhula mʼdzina lanu, iye wakhala akuzunza anthuwa, ndipo inu simunawapulumutse konse anthu anu.”

< Exodus 5 >