< Exodus 6 >

1 Then the Lord sayd vnto Moses, Nowe shalt thou see, what I will doe vnto Pharaoh: for by a strong hand shall he let them goe, and euen be constrained to driue them out of his land.
Yehova anawuza Mose kuti, “Tsopano udzaona zimene ndimuchite Farao: Chifukwa cha dzanja langa lamphamvu adzalola anthu anga kuti atuluke. Chifukwa cha dzanja langa lamphamvu adzawatulutsa mʼdziko lake.”
2 Moreouer God spake vnto Moses, and sayd vnto him, I am the Lord,
Mulungu anatinso kwa Mose, “Ine ndine Yehova.
3 And I appeared vnto Abraham, to Izhak, and to Iaakob by the Name of Almightie God: but by my Name Iehouah was I not knowen vnto the.
Ndinaonekera kwa Abrahamu, kwa Isake ndi kwa Yakobo monga Mulungu Wamphamvuzonse, koma sindinawadziwitse dzina langa kuti ndine Yehova.
4 Furthermore as I made my couenant with them to giue them ye land of Canaan, the land of their pilgrimage, wherein they were strangers:
Ndinakhazikitsa pangano langa ndi iwo kuwalonjeza kuti ndidzawapatsa dziko la Kanaani kumene anakhalako kale ngati alendo.
5 So I haue also hearde the groning of the children of Israel, whom the Egyptians keepe in bondage, and haue remembred my couenant.
Ndamvanso kubuwula kwa Aisraeli, amene Aigupto awayesa akapolo ndipo ndakumbukira pangano langa.”
6 Wherefore say thou vnto the children of Israel, I am the Lord, and I will bring you out from the burdens of the Egyptians, and will deliuer you out of their bondage, and will redeeme you in a stretched out arme, and in great iudgements.
“Nʼchifukwa chake nena kwa Aisraeli kuti, ‘Ine ndine Yehova, ndipo ndidzakutulutsani mʼgoli la Aigupto. Ndidzakumasulani mu ukapolo, ndidzakuwombolani ndi dzanja langa lotambasuka ndi kuchita ntchito zachiweruzo.
7 Also I will take you for my people, and will be your God: then ye shall knowe that I the Lord your God bring you out from the burdens of the Egyptians.
Ndidzakutengani kukhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wanu. Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu amene ndinakutulutsani mʼgoli la Aigupto.
8 And I will bring you into the land which I sware that I woulde giue to Abraham, to Izhak, and to Iaakob, and I will giue it vnto you for a possession: I am the Lord.
Ndipo ndidzakufikitsani ku dziko limene ndinalumbira kuti ndidzalipereka kwa Abrahamu, kwa Isake ndi kwa Yakobo. Ndidzakupatsani dziko limenelo kuti likhale lanu. Ine ndine Yehova.’”
9 So Moses told the children of Israel thus: but they hearkened not vnto Moses, for anguish of spirit and for cruel bondage.
Mose anawafotokozera Aisraeli zimenezi, koma iwo sanamumvere chifukwa cha kukhumudwa ndi goli lankhanza.
10 Then the Lord spake vnto Moses, saying,
Kenaka Yehova anati kwa Mose,
11 Go speak to Pharaoh King of Egypt, that he let the children of Israel goe out of his land.
“Pita ukawuze Farao mfumu ya Igupto kuti awalole Aisraeli atuluke mʼdziko lake.”
12 But Moses spake before the Lord, saying, Beholde, the children of Israel hearken not vnto me, howe then shall Pharaoh heare mee, which am of vncircumcised lippes?
Koma Mose ananena kwa Yehova kuti, “Ngati Aisraeli sanandimvere, Farao akandimvera chifukwa chiyani, pajatu sinditha kuyankhula bwino?”
13 Then the Lord spake vnto Moses and vnto Aaron, and charged them to goe to the children of Israel and to Pharaoh King of Egypt, to bring the children of Israel out of the lande of Egypt.
Ndipo Yehova analamula Mose ndi Aaroni kuti awuze Aisraeli ndi Farao mfumu ya Igupto kuti Aisraeli ayenera kutuluka mʼdziko la Igupto.
14 These bee the heades of their fathers houses: the sonnes of Reuben the first borne of Israel are Hanoch and Pallu, Hezron and Carmi: these are ye families of Reuben.
Atsogoleri a mafuko awo anali awa: Ana a Rubeni mwana wachisamba wa Israeli anali Hanoki, Palu, Hezironi ndi Karimi. Awa anali mafuko a Rubeni.
15 Also the sonnes of Simeon: Iemuel and Iamin, and Ohad, and Iachin, and Zoar, and Shaul the sonne of a Canaanitish woman: these are the families of Simeon.
Ana a Simeoni anali Yemueli, Yamini, Ohadi, Yakini, Zohari ndi Saulo mwana wa kwa mkazi wa Chikanaani. Awa anali mafuko a Simeoni.
16 These also are the names of the sonnes of Leui in their generations: Gershon and Kohath and Merari (and the yeres of the life of Leui were an hundreth thirtie and seuen yere)
Mayina a ana a Levi pamodzi ndi zidzukulu zawo anali awa: Geresoni, Kohati ndi Merari. Levi anakhala ndi moyo kwa zaka 137.
17 The sonnes of Gershon were Libni and Shimi by their families.
Ana a Geresoni, mwa mafuko awo, anali Libini ndi Simei.
18 And the sonnes of Kohath, Amram and Izhar, and Hebron, and Vzziel. (and Kohath liued an hundreth thirtie and three yeere)
Ana a Kohati anali Amramu, Izihari, Hebroni ndi Uzieli. Kohati anakhala ndi moyo zaka 133.
19 Also the sonnes of Merari were Mahali and Mushi: these are ye families of Leui by their kinreds.
Ana a Merari anali Mali ndi Musi. Awa anali mafuko a Levi monga mwa mibado yawo.
20 And Amram tooke Iochebed his fathers sister to his wife, and shee bare him Aaron and Moses (and Amram liued an hundreth thirtie and seuen yeere)
Amramu anakwatira Yokobedi mlongo wa abambo ake, amene anabereka Aaroni ndi Mose. Amramu anakhala ndi moyo kwa zaka 137.
21 Also the sonnes of Izhar: Korah, and Nepheg, and Zichri.
Ana a Izihari anali Kora, Nefegi ndi Zikiri.
22 And the sonnes of Vzziel: Mishael, and Elzaphan, and Sithri.
Ana a Uzieli anali Misaeli, Elizafani ndi Sitiri.
23 And Aaron tooke Elisheba daughter of Amminadab, sister of Nahashon to his wife, which bare him Nadab, and Abihu, Eleazar and Ithamar.
Aaroni anakwatira Eliseba, mwana wamkazi wa Aminadabu, mlongo wa Nasoni ndipo Iye anabereka Nadabu, Abihu, Eliezara ndi Itamara.
24 Also the sonnes of Korah: Assir, and Elkanah, and Abiasaph: these are the families of the Korhites.
Ana a Kora anali Asiri, Elikana ndi Abiasafu. Awa ndiwo mafuko a Kora.
25 And Eleazar Aarons sonne tooke him one of the daughters of Putiel to his wife, which bare him Phinehas: these are the principall fathers of the Leuites throughout their families.
Eliezara mwana wa Aaroni anakwatira mmodzi mwa ana aakazi a Putieli, ndipo anabereka Finehasi. Awa anali atsogoleri a mabanja a Levi, monga mwa mafuko awo.
26 These are Aaron and Moses to whom the Lord said, Bring the children of Israel out of the land of Egypt, according to their armies.
Aaroni ndi Mose ndi aja amene Yehova anawawuza kuti, “Tulutsani Aisraeli mu Igupto mʼmagulu awo.”
27 These are that Moses and Aaron, which spake to Pharaoh King of Egypt, that they might bring the children of Israel out of Egypt.
Mose ndi Aaroni ndiwo amene anayankhula ndi Farao mfumu ya Igupto kuti atulutse Aisraeli mu Igupto.
28 And at that time when the Lord spake vnto Moses in the land of Egypt,
Tsopano pamene Yehova anayankhula kwa Mose mu Igupto,
29 When the Lord, I say, spake vnto Moses, saying, I am the Lord, speake thou vnto Pharaoh the King of Egypt all that I say vnto thee,
anati, “Ine ndine Yehova. Umuwuze Farao mfumu ya Igupto zonse zimene Ine ndikuwuze iwe.”
30 Then Moses said before the Lord, Behold, I am of vncircumcised lips, and how shall Pharaoh heare me?
Koma Mose anati kwa Yehova, “Farao akandimvera bwanji, pakuti ine sinditha kuyankhula bwino?”

< Exodus 6 >