< Job 35 >

1 Elihu spake moreouer, and said,
Ndipo Elihu anawonjeza kunena kuti,
2 Thinkest thou this right, that thou hast said, I am more righteous then God?
“Kodi mukuganiza kuti mukukhoza? Mukunena kuti, ‘Ndine wolungama pamaso pa Mulungu.’
3 For thou hast said, What profiteth it thee and what auaileth it me, to purge me from my sinne?
Komanso inu mukufunsa kuti, ‘Kodi phindu langa nʼchiyani, ndipo ndimapeza chiyani ndikapanda kuchimwa?’
4 Therefore will I answere thee, and thy companions with thee.
“Ine ndikufuna ndikuyankheni inu pamodzi ndi abwenzi anu omwe.
5 Looke vnto the heauen, and see and behold the cloudes which are hyer then thou.
Yangʼanani kumwamba ndipo muone mitambo imene ili kutali ndi inuyo.
6 If thou sinnest, what doest thou against him, yea, when thy sinnes be many, what doest thou vnto him?
Inuyo mukachimwa, Iye zimamukhudza motani? Ngati machimo anu ndi ochuluka, zimenezo zimachita chiyani kwa Iye?
7 If thou be righteous, what giuest thou vnto him? or what receiueth he at thine hand?
Ngati inu ndinu wolungama, mumamupatsa Iyeyo chiyani? Kapena Iye amalandira chiyani chochokera mʼdzanja lanu?
8 Thy wickednesse may hurt a man as thou art: and thy righteousnes may profite ye sonne of man.
Kuyipa kwanu kumangokhudza anthu ngati inuyo, ndipo chilungamo chanu chimakhudza anthu anzanu.
9 They cause many that are oppressed, to crye, which crye out for ye violence of the mightie.
“Anthu akufuwula chifukwa cha kuzunzidwa; akufuna chithandizo kuti achoke pansi pa ulamuliro wa anthu amphamvu.
10 But none saieth, Where is God that made me, which giueth songs in the nyght?
Koma palibe amene akunena kuti, ‘Kodi ali kuti Mulungu, Mlengi wanga, amene amatisangalatsa nthawi ya usiku,
11 Which teacheth vs more then the beastes of the earth, and giueth vs more wisdome then the foules of the heauen.
amene amatiphunzitsa kupambana nyama za dziko lapansi ndipo amatipatsa nzeru kupambana mbalame zowuluka?’
12 Then they crye because of the violence of the wicked, but he answereth not.
Iye sayankha pamene anthu akufuwulira kwa Iye chifukwa cha kudzikuza kwa anthu oyipa.
13 Surely God will not heare vanitie, neyther will the Almightie regard it.
Ndithu, Mulungu samva kupempha kwawo kopanda pake; Wamphamvuzonse sasamalira zimenezi.
14 Although thou sayest to God, Thou wilt not regard it, yet iudgement is before him: trust thou in him.
Ndipo ndi bodza lalikulu kunena kuti Iye saona zimene zikuchitika. Iye adzaweruza molungama ngati inu mutamudikira
15 But nowe because his anger hath not visited, nor called to count the euill with great extremitie,
ndiye tsono popeza kuti ukali wake sukupereka chilango, zoyipa zambiri zimene anthu amachita,
16 Therfore Iob openeth his mouth in vaine, and multiplieth wordes without knowledge.
abambo Yobu mumangoyankhula zopandapake, mukungochulukitsa mawu opanda nzeru.”

< Job 35 >