< Proverbs 14 >

1 A wise woman buildeth her house: but the foolish destroyeth it with her owne handes.
Mkazi wanzeru amamanga banja lake, koma mkazi wopusa amalimasula ndi manja ake omwe.
2 He that walketh in his righteousnes, feareth the Lord: but he that is lewde in his wayes, despiseth him.
Amene amayenda molungama amaopa Yehova, koma amene njira zake ndi zoyipa amanyoza Yehova.
3 In the mouth of the foolish is the rod of pride: but the lippes of the wise preserue them.
Kuyankhula kwa chitsiru kumamuyitanira ndodo pa msana, koma milomo ya munthu wanzeru imamuteteza.
4 Where none oxen are, there the cribbe is emptie: but much increase cometh by the strength of the oxe.
Pakasowa ngʼombe zolima gome limakhala lopanda chakudya, koma pakakhala ngʼombe zamphamvu zakudya zimachulukanso.
5 A faithfull witnes will not lye: but a false record will speake lyes.
Mboni yokhulupirika sinama, koma mboni yonyenga imayankhula zabodza.
6 A scorner seeketh wisdome, and findeth it not: but knowledge is easie to him that will vnderstande.
Wonyoza anzake amafunafuna nzeru koma osayipeza, koma munthu womvetsa bwino amadziwa zinthu msanga.
7 Depart from the foolish man, when thou perceiuest not in him the lippes of knowledge.
Khala kutali ndi munthu wopusa chifukwa sudzapeza mawu a nzeru.
8 The wisdome of ye prudent is to vnderstand his way: but the foolishnes of the fooles is deceite.
Nzeru za munthu wochenjera zagona pakuzindikira njira zake. Koma uchitsiru wa zitsiru umapusitsidwa ndi chinyengo chawo chomwe.
9 The foole maketh a mocke of sinne: but among the righteous there is fauour.
Zitsiru zimanyoza za kulapa machimo, awo, koma kufuna kwabwino kumapezeka mwa anthu olungama.
10 The heart knoweth the bitternes of his soule, and the stranger shall not medle with his ioy.
Mtima uliwonse umadziwa wokha zowawa zake, ndipo palibe wina aliyense angadziwe kukondwa kwake.
11 The house of the wicked shalbe destroyed: but the tabernacle of the righteous shall florish.
Nyumba ya munthu woyipa idzapasuka, koma tenti ya munthu wowongoka mtima idzakhazikika.
12 There is a way that seemeth right to a man: but the issues thereof are the wayes of death.
Pali njira ina yooneka ngati yabwino kwa munthu, koma kumatsiriziro kwake ndi ku imfa.
13 Euen in laughing the heart is sorowful, and the ende of that mirth is heauinesse.
Ngakhale poseka mtima utha kumva kuwawa, ndipo mathero achimwemwe akhoza kukhala chisoni.
14 The heart that declineth, shall be saciate with his owne wayes: but a good man shall depart from him.
Munthu wosakhulupirika adzalandira zogwirizana ndi ntchito yake, koma munthu wabwino adzalandira mphotho ya ntchito yake.
15 The foolish will beleeue euery thing: but the prudent will consider his steppes.
Munthu wopusa amakhulupirira chilichonse, koma munthu wochenjera amaganizira bwino mayendedwe ake.
16 A wise man feareth, and departeth from euill: but a foole rageth, and is carelesse.
Munthu wanzeru amaopa Mulungu ndipo amapewa zoyipa, koma munthu wopusa ndi wokula mtima amakhala wosasamala.
17 He that is hastie to anger, committeth follie, and a busie body is hated.
Munthu wopsa mtima msanga amachita zinthu za uchitsiru, ndipo anthu amadana ndi munthu wachinyengo.
18 The foolish do inherite follie: but the prudent are crowned with knowledge.
Anthu opusa amalandira uchitsiru, koma anthu ochenjera amavekedwa chipewa cha ulemerero wa kudziwa zinthu.
19 The euill shall bowe before the good, and the wicked at the gates of the righteous.
Anthu oyipa adzagwada pamaso pa anthu abwino, ndipo anthu oyipa adzapempha thandizo kwa anthu olungama.
20 The poore is hated euen of his own neighbour: but the friendes of the rich are many.
Munthu wosauka ngakhale anansi ake omwe amamuda, koma munthu wolemera ali ndi abwenzi ambiri.
21 The sinner despiseth his neighbour: but he that hath mercie on the poore, is blessed.
Wonyoza mnansi wake ndi wochimwa koma ndi wodala amene amachitira chifundo anthu osowa.
22 Doe not they erre that imagine euill? but to them that thinke on good things, shalbe mercie and trueth.
Kodi amene amakonzekera zoyipa sasochera? Koma amene amakonzekera zabwino anthu amawaonetsa chikondi ndi kukhulupirika.
23 In all labour there is abundance: but the talke of the lippes bringeth onely want.
Ntchito iliyonse imakhala ndi phindu, koma kuyankhulayankhula kumabweretsa umphawi.
24 The crowne of the wise is their riches, and the follie of fooles is foolishnes.
Chipewa chaulemu cha anthu a nzeru ndi chuma chawo chomwe, koma malipiro a zitsiru ndi uchitsiru.
25 A faithfull witnes deliuereth soules: but a deceiuer speaketh lyes.
Mboni yokhulupirika imapulumutsa miyoyo, koma mboni yabodza imaphetsa.
26 In the feare of the Lord is an assured strength, and his children shall haue hope.
Amene amaopa Yehova ali ndi chitetezo chokwanira ndipo iye adzakhala pothawira pa ana ake.
27 The feare of the Lord is as a welspring of life, to auoyde the snares of death.
Kuopa Yehova ndiye kasupe wamoyo, kumathandiza munthu kuti apewe msampha wa imfa.
28 In the multitude of the people is the honour of a King, and for the want of people commeth the destruction of the Prince.
Gulu lalikulu la anthu ndiye ulemerero wa mfumu, koma popanda anthu kalonga amawonongeka.
29 He that is slowe to wrath, is of great wisdome: but he that is of an hastie minde, exalteth follie.
Munthu wosapsa mtima msanga amamvetsa zinthu kwambiri, koma munthu wopsa mtima msanga amaonetsa uchitsiru wake.
30 A sounde heart is the life of the flesh: but enuie is the rotting of the bones.
Mtima wodekha umapatsa thupi moyo, koma nsanje imawoletsa mafupa.
31 He that oppresseth the poore, reprooueth him that made him: but hee honoureth him, that hath mercie on the poore.
Amene amapondereza mʼmphawi amanyoza mlengi wake, koma wochitira chifundo munthu wosowa amalemekeza Mulungu.
32 The wicked shall be cast away for his malice: but the righteous hath hope in his death.
Anthu oyipa adzakanthidwa chifukwa cha ntchito zawo zomwe, koma olungama adzatetezedwa mwa imfa yawo.
33 Wisedome resteth in the heart of him that hath vnderstanding, and is knowen in the mids of fooles.
Nzeru zimakhala mu mtima mwa anthu omvetsa zinthu, koma nzeru sipezeka mu mtima mwa zitsiru.
34 Iustice exalteth a nation, but sinne is a shame to the people.
Chilungamo chimakweza mtundu wa anthu, koma uchimo umachititsa manyazi mtundu uliwonse.
35 The pleasure of a King is in a wise seruant: but his wrath shalbe toward him that is lewde.
Mfumu imasangalatsidwa ndi wantchito wanzeru, koma imachitira ukali wantchito wochititsa manyazi.

< Proverbs 14 >