< Psalms 55 >

1 To him that excelleth on Neginoth. A Psalme of David to give instruction. Heare my prayer, O God, and hide not thy selfe from my supplication.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya Davide. Pa zoyimbira za zingwe. Mvetserani pemphero langa, Inu Mulungu, musakufulatire kupempha kwanga,
2 Hearken vnto me, and answere me: I mourne in my prayer, and make a noyse,
mverani ndipo mundiyankhe. Maganizo anga akundisautsa ndipo ndathedwa nzeru
3 For the voyce of the enemie, and for the vexation of ye wicked, because they haue brought iniquitie vpon me, and furiously hate me.
chifukwa cha mawu a adani anga, chifukwa cha kupondereza kwa anthu oyipa; pakuti andidzetsera masautso ndipo akundizunza mu mkwiyo wawo.
4 Mine heart trembleth within mee, and the terrours of death are fallen vpon me.
Mtima wanga ukupweteka mʼkati mwanga; mantha a imfa andigwera.
5 Feare and trembling are come vpon mee, and an horrible feare hath couered me.
Mantha ndi kunjenjemera zandizinga; mantha aakulu andithetsa nzeru.
6 And I said, Oh that I had wings like a doue: then would I flie away and rest.
Ndinati, “Ndithu, ndikanakhala ndi mapiko ankhunda! Ndikanawulukira kutali ndi kukapuma.
7 Beholde, I woulde take my flight farre off, and lodge in the wildernes. (Selah)
Ndikanathawira kutali ndi kukakhala mʼchipululu.
8 Hee would make haste for my deliuerance from the stormie winde and tempest.
Ndikanathamangira kumalo anga a chitetezo; kutali ndi mphepo yaukali ndi yamkuntho.”
9 Destroy, O Lord, and deuide their tongues: for I haue seene crueltie and strife in the citie.
Sokonezani maganizo a oyipa, Inu Ambuye, tsutsani mawu awo; pakuti ine ndikuona chiwawa ndi mkangano mu mzinda.
10 Day and night they goe about it vpon the walles thereof: both iniquitie and mischiefe are in the middes of it.
Usana ndi usiku iwo akuzungulirazungulira pa makoma ake; nkhwidzi ndi kuzunza kuli mʼkati mwake.
11 Wickednes is in the middes thereof: deceit and guile depart not from her streetes.
Mphamvu zowononga zili pa ntchito mu mzinda; kuopseza ndi mabodza sizichoka mʼmisewu yake.
12 Surely mine enemie did not defame mee: for I could haue borne it: neither did mine aduersarie exalt himselfe against mee: for I would haue hid me from him.
Akanakhala mdani akundinyoza, ine ndikanapirira; akanakhala mdani akudzikweza yekha kutsutsana nane, ndikanakabisala.
13 But it was thou, O man, euen my companion, my guide and my familiar:
Koma iweyo mnzanga, mnzanga woyenda naye, bwenzi langa la pondaapanʼpondepo, ndi amene ukuchita zimenezi.
14 Which delited in consulting together, and went into the House of God as companions.
Mnzanga amene nthawi ina tinkasangalala pa chiyanjano chokoma ku nyumba ya Mulungu.
15 Let death sense vpon them: let them goe downe quicke into the graue: for wickednes is in their dwellings, euen in the middes of them. (Sheol h7585)
Mulole imfa itenge adani anga mwadzidzidzi; alowe mʼmanda ali amoyo pakuti choyipa chili pakati pawo. (Sheol h7585)
16 But I will call vnto God, and the Lord will saue me.
Koma ine ndinafuwulira kwa Mulungu, ndipo Yehova anandipulumutsa.
17 Euening and morning, and at noone will I pray, and make a noyse, and he wil heare my voice.
Madzulo, mmawa ndi masana ndimalira mowawidwa mtima, ndipo Iye amamva mawu anga.
18 He hath deliuered my soule in peace from the battel, that was against me: for many were with me.
Iye amandiwombola ine osavulazidwa pa nkhondo imene yafika kulimbana nane, ngakhale kuti ndi ambiri amene akunditsutsa.
19 God shall heare and afflict them, euen hee that reigneth of olde, (Selah) because they haue no changes, therefore they feare not God.
Mulungu amene ali pa mpando wake kwamuyaya, adzandimenyera nkhondo; adzawatsitsa adani anga, chifukwa safuna kusintha njira zawo zoyipa ndipo saopa Mulungu.
20 Hee layed his hande vpon such, as be at peace with him, and he brake his couenant.
Mnzanga woyenda naye wathira nkhondo abwenzi ake; iye akuphwanya pangano ake.
21 The wordes of his mouth were softer then butter, yet warre was in his heart: his words were more gentle then oyle, yet they were swordes.
Mawu ake ndi osalala kuposa batala komabe nkhondo ili mu mtima mwake; mawu ake ndi osalala kwambiri kuposa mafuta, komatu mawuwo ndi malupanga osololoka.
22 Cast thy burden vpon the Lord, and hee shall nourish thee: he wil not suffer the righteous to fall for euer.
Tulani nkhawa zanu kwa Yehova ndipo Iye adzakulimbitsani; Iye sadzalola kuti wolungama agwe.
23 And thou, O God, shalt bring them downe into the pitte of corruption: the bloudie, and deceitfull men shall not liue halfe their dayes: but I will trust in thee.
Koma Inu Mulungu mudzawatsitsa anthu oyipa kulowa mʼdzenje lachiwonongeko; anthu okhetsa magazi ndi anthu achinyengo sadzakhala moyo theka la masiku awo, koma ine ndimadalira Inu.

< Psalms 55 >