< Exodus 26 >

1 Moreover you shall make the tabernacle with ten curtains of fine twined linen, and blue, and purple, and scarlet: with cherubim of cunning work shall you make them.
“Panga chihema pogwiritsa ntchito nsalu khumi zofewa, zosalala ndi zolukidwa bwino, zobiriwira, zapepo ndi zofiira. Ndipo anthu aluso apete pa nsaluzo Akerubi.
2 The length of one curtain shall be eight and twenty cubits, and the breadth of one curtain four cubits: and every one of the curtains shall have one measure.
Nsalu zonse zikhale zofanana. Mulitali mwake zikhale mamita khumi ndi atatu, mulifupi mamita awiri.
3 The five curtains shall be coupled together one to another; and other five curtains shall be coupled one to another.
Ulumikize nsalu zisanu kuti ikhale nsalu imodzi. Uchite chimodzimodzi ndi nsalu zisanu zinazo.
4 And you shall make loops of blue on the edge of the one curtain from the selvedge in the coupling; and likewise shall you make in the uttermost edge of another curtain, in the coupling of the second.
Panga zokolowekamo za nsalu yobiriwira mʼmphepete mwa nsalu imodzi yotsiriza ya mbali ina. Uchitenso chimodzimodzi ndi nsalu yotsiriza ya mbali inayo.
5 Fifty loops shall you make in the one curtain, and fifty loops shall you make in the edge of the curtain that is in the coupling of the second; that the loops may take hold one of another.
Upange zokolowekamo 50 pa nsalu yoyamba ndi zokolowekamo makumi asanu zinanso pa nsalu inayo. Upange motero kuti zokolowekamozo ziziyangʼanana.
6 And you shall make fifty clasps of gold, and couple the curtains together with the clasps: and it shall be one tabernacle.
Kenaka upange ngowe zagolide makumi asanu zolumikizira nsalu ziwirizo kuti zipange chihema chimodzi.
7 And you shall make curtains of goats’ hair to be a covering on the tabernacle: eleven curtains shall you make.
“Upange nsalu za ubweya wambuzi zophimba pamwamba pa chihemacho. Nsalu zonse pamodzi zikhale khumi ndi imodzi.
8 The length of one curtain shall be thirty cubits, and the breadth of one curtain four cubits: and the eleven curtains shall be all of one measure.
Nsalu zonse khumi ndi imodzi zikhale zofanana. Mulitali mwake mukhale mamita khumi ndi anayi ndipo mulifupi mwake mukhale mamita awiri.
9 And you shall couple five curtains by themselves, and six curtains by themselves, and shall double the sixth curtain in the forefront of the tabernacle.
Ulumikize nsalu zisanu kuti ikhale nsalu imodzi ndipo zina zisanu ndi imodzi uzilumikizenso kuti ikhale nsalu imodzinso. Nsalu yachisanu ndi chimodzi imene ili kutsogolo kwa tenti uyipinde pawiri.
10 And you shall make fifty loops on the edge of the one curtain that is outmost in the coupling, and fifty loops in the edge of the curtain which couples the second.
Upange zokolowekamo 50 mʼmphepete mwa nsalu imodzi yotsirizira ya nsalu yoyamba yolumikiza ija. Upangenso zokolowekamo zina 50 mʼmphepete mwa nsalu yotsirizira ya nsalu inanso yolumikiza ija.
11 And you shall make fifty clasps of brass, and put the clasps into the loops, and couple the tent together, that it may be one.
Kenaka upange ngowe 50 zamkuwa ndipo uzilowetse mu zokolowekazo. Ndiye uphatikize nsalu ziwirizo kuti tentiyo ikhale imodzi.
12 And the remnant that remains of the curtains of the tent, the half curtain that remains, shall hang over the backside of the tabernacle.
Theka lotsalira la nsaluyo lidzalendewera kumbuyo kwa chihemacho.
13 And a cubit on the one side, and a cubit on the other side of that which remains in the length of the curtains of the tent, it shall hang over the sides of the tabernacle on this side and on that side, to cover it.
Nsalu yotsalira ya masentimita 46 mulitali mwake mʼmbali zonse ziwiri idzalendewere kuphimba mbali ziwirizo.
14 And you shall make a covering for the tent of rams’ skins dyed red, and a covering above of badgers’ skins.
Upange chikopa cha nkhosa zazimuna cha utoto wofiira chophimbira tentiyo ndipo pamwamba pake upangireponso chophimbira china cha zikopa za akatumbu.
15 And you shall make boards for the tabernacle of shittim wood standing up.
“Upange maferemu amatabwa amtengo wa mkesha oyimikira chihemacho.
16 Ten cubits shall be the length of a board, and a cubit and a half shall be the breadth of one board.
Feremu iliyonse ikhale yotalika mamita anayi ndipo mulifupi mwake mukhale masentimita 69.
17 Two tenons shall there be in one board, set in order one against another: thus shall you make for all the boards of the tabernacle.
Thabwa lililonse likhale ndi zolumikizira ziwiri. Upange maferemu onse a chihemacho ndi matabwa otere.
18 And you shall make the boards for the tabernacle, twenty boards on the south side southward.
Upange maferemu makumi awiri a mbali yakummwera kwa chihemacho.
19 And you shall make forty sockets of silver under the twenty boards; two sockets under one board for his two tenons, and two sockets under another board for his two tenons.
Ndipo upange matsinde 40 asiliva ndipo uwayike pansi pa maferemuwo. Pansi pa feremu iliyonse pakhale matsinde awiri ogwiriziza zolumikizira ziwiri zija.
20 And for the second side of the tabernacle on the north side there shall be twenty boards:
Ndipo mbali yakumpoto ya chihemacho upangenso maferemu makumi awiri.
21 And their forty sockets of silver; two sockets under one board, and two sockets under another board.
Upangenso matsinde 40 asiliva, awiri pansi pa feremu iliyonse.
22 And for the sides of the tabernacle westward you shall make six boards.
Upange maferemu asanu ndi imodzi a kumbuyo kwa tenti, kumbali yakumadzulo.
23 And two boards shall you make for the corners of the tabernacle in the two sides.
Ndipo upangenso maferemu awiri a pa ngodya yakumbuyo kwenikweni kwa tenti.
24 And they shall be coupled together beneath, and they shall be coupled together above the head of it to one ring: thus shall it be for them both; they shall be for the two corners.
Pa ngodya ziwirizi pakhale maferemu awiri, kuyambira pansi mpaka pamwamba ndipo alumikizidwe pa ngowe imodzi. Maferemu onse akhale ofanana.
25 And they shall be eight boards, and their sockets of silver, sixteen sockets; two sockets under one board, and two sockets under another board.
Choncho pakhale maferemu asanu ndi atatu ndiponso matsinde 16 asiliva, awiri akhale pansi pa feremu iliyonse.
26 And you shall make bars of shittim wood; five for the boards of the one side of the tabernacle,
“Upange mitanda ya matabwa amtengo wa mkesha: mitanda isanu ikhale ya maferemu a mbali imodzi ya chihema,
27 And five bars for the boards of the other side of the tabernacle, and five bars for the boards of the side of the tabernacle, for the two sides westward.
mitanda isanu inanso ikhale ya maferemu a mbali inayo. Pakhalenso mitanda ina isanu ya mbali yakumadzulo, kumapeto kwenikweni kwa chihema.
28 And the middle bar in the middle of the boards shall reach from end to end.
Mtanda wapakati pa maferemuwo uchokere pa maferemu a mbali ina mpaka mbali inanso.
29 And you shall overlay the boards with gold, and make their rings of gold for places for the bars: and you shall overlay the bars with gold.
Maferemuwo uwakute ndi golide ndiponso upange mphete zagolide zogwiriziza mitandayo. Ndipo mitandayonso uyikute ndi golide.
30 And you shall raise up the tabernacle according to the fashion thereof which was showed you in the mount.
“Upange chihema mofanana ndi momwe ndinakuonetsera pa phiri paja.
31 And you shall make a veil of blue, and purple, and scarlet, and fine twined linen of cunning work: with cherubim shall it be made:
“Upange nsalu yokhala ndi mtundu wamtambo, wapepo ndi ofiira ndipo nsaluyo ikhale yolukidwa bwino, yofewa ndi yosalala. Ndipo anthu aluso apetepo zithunzi za Akerubi.
32 And you shall hang it on four pillars of shittim wood overlaid with gold: their hooks shall be of gold, on the four sockets of silver.
Nsaluyo uyikoloweke pa nsanamira zinayi zamtengo wa mkesha zokutidwa ndi golide zomwe zili ndi ngowe zagolide, zomwe zayima pa matsinde asiliva anayi.
33 And you shall hang up the veil under the clasps, that you may bring in thither within the veil the ark of the testimony: and the veil shall divide to you between the holy place and the most holy.
Ukoloweke kataniyo ku ngowe ndipo uyike Bokosi la Chipangano mʼkatimo. Kataniyo idzalekanitse malo wopatulika ndi malo wopatulika kwambiri.
34 And you shall put the mercy seat on the ark of the testimony in the most holy place.
Uyike chivundikiro pa bokosi laumboni ku malo wopatulika kwambiri.
35 And you shall set the table without the veil, and the candlestick over against the table on the side of the tabernacle toward the south: and you shall put the table on the north side.
Uyike tebulo kunja kwa katani yotchinga cha kumpoto kwa chihema ndipo uyike choyikapo nyale chija kummwera moyangʼanana ndi tebulolo.
36 And you shall make an hanging for the door of the tent, of blue, and purple, and scarlet, and fine twined linen, worked with needlework.
“Pa chipata cholowera mu chihema, uyikepo nsalu yamtundu wamtambo, wapepo ndi ofiira, yomwe ndi yofewa ndi yosalala, yopetedwa bwino ndi amisiri aluso.
37 And you shall make for the hanging five pillars of shittim wood, and overlay them with gold, and their hooks shall be of gold: and you shall cast five sockets of brass for them.
Upange ngowe zagolide za nsaluyo ndi nsanamira zisanu zamtengo wa mkesha ndipo uzikute ndi golide. Upangenso matsinde asanu amkuwa a nsanamirazo.”

< Exodus 26 >