< Psalms 11 >

1 [For the Chief Musician. By David.] In YHWH, I take refuge. How can you say to my soul, "Flee as a bird to your mountain."
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Mwa Yehova ine ndimathawiramo. Nanga mungathe bwanji kunena kwa ine kuti, “Thawira ku phiri lako ngati mbalame.
2 For, look, the wicked bend their bows. They set their arrows on the strings, that they may shoot in darkness at the upright in heart.
Pakuti taona oyipa akunga mauta awo; ayika bwino mivi yawo pa zingwe za uta, pobisala pawo kuti alase olungama mtima.
3 If the foundations are destroyed, what can the righteous do?
Tsono ngati maziko awonongeka, olungama angachite chiyani?”
4 YHWH is in his holy temple. YHWH is on his throne in heaven. His eyes look upon the poor. His eyes examine the descendants of Adam.
Yehova ali mʼNyumba yake yoyera; Yehova ali pa mpando wake waufumu kumwamba. Iye amayangʼanitsitsa ana a anthu; maso ake amawayesa.
5 YHWH examines the righteous, but the wicked and the one who loves violence his soul hates.
Yehova amayesa olungama, koma moyo wake umadana ndi oyipa, amene amakonda zachiwawa.
6 On the wicked he will rain blazing coals; fire, sulfur, and scorching wind shall be the portion of their cup.
Iye adzakhuthulira pa oyipa makala amoto ndi sulufule woyaka; mphepo yotentha idzakhala yowayenera.
7 For YHWH is righteous. He loves righteousness. The upright shall see his face.
Pakuti Yehova ndi wolungama, Iye amakonda chilungamo; ndipo anthu olungama adzaona nkhope yake.

< Psalms 11 >