< Job 10 >

1 My soul is weary of my life; I will give free course to my complaint; I will speak in the bitterness of my soul.
“Ine ndatopa nawo moyo wanga; choncho ndidzanena zodandaula zanga momasuka ndipo ndidzayankhula mwa kuwawidwa mtima kwanga.
2 I will say unto God, Do not condemn me; shew me wherefore thou contendest with me.
Ndidzati kwa Mulungu wanga: Musandiweruze kuti ndine wolakwa, koma mundiwuze chifukwa chimene Inu mukukanganira ndi ine.
3 Is it good unto thee that thou shouldest oppress, that thou shouldest despise the work of thine hands, and shine upon the counsel of the wicked?
Kodi mumakondwera mukamandizunza, kunyoza ntchito ya manja anu, chonsecho mukusekerera ndi zochita za anthu oyipa?
4 Hast thou eyes of flesh, or seest thou as man seeth?
Kodi maso anu ali ngati a munthu? Kodi mumaona zinthu monga momwe amazionera munthu?
5 Are thy days as the days of man, or thy years as man’s days,
Kodi masiku anu ali ngati masiku a munthu, kapena zaka zanu ngati zaka za munthu,
6 That thou inquirest after mine iniquity, and searchest after my sin,
kuti Inu mufufuze zolakwa zanga ndi kulondola tchimo langa,
7 Although thou knowest that I am not wicked; and there is none that can deliver out of thine hand?
ngakhale mukudziwa kuti sindine wolakwa ndiponso kuti palibe amene angandilanditse mʼdzanja lanu?
8 Thine hands have framed me and fashioned me together round about; yet thou dost destroy me.
“Munandiwumba ndi kundipanga ndi manja anu. Kodi tsopano Inu mudzatembenuka ndi kundiwononga?
9 Remember, I beseech thee, that thou hast fashioned me as clay; and wilt thou bring me into dust again?
Kumbukirani kuti munandipanga ndi dothi, kodi tsopano mundibwezeranso ku fumbi?
10 Hast thou not poured me out as milk, and curdled me like cheese?
Suja munapatsa abambo anga mphamvu zoti andibale, suja munandikuza bwino mʼmimba mwa amayi anga?
11 Thou hast clothed me with skin and flesh, and knit me together with bones and sinews.
Munandikuta ndi khungu ndi mnofu ndi kundilumikiza pamodzi ndi mafupa ndi mitsempha?
12 Thou hast granted me life and favour, and thy visitation hath preserved my spirit.
Munandipatsa moyo ndi kundionetsa chifundo chanu, ndipo munasamalira bwino moyo wanga.
13 Yet these things thou didst hide in thine heart; I know that this is with thee:
“Koma izi ndi zimene munabisa mu mtima mwanu, ndipo ndikudziwa kuti zinali mʼmaganizo anu:
14 If I sin, then thou markest me, and thou wilt not acquit me from mine iniquity.
Kuti ngati ndingachimwe mudzakhala mukundipenyetsetsa ndipo kuti simudzalola kuti ndisalangidwe chifukwa cha kulakwa kwanga.
15 If I be wicked, woe unto me; and if I be righteous, yet shall I not lift up my head; being filled with ignominy and looking upon mine affliction.
Ngati ndili wolakwa, tsoka langa! Koma ngakhale ndili wosalakwa sindingathe kutukula mutu wanga, pakuti ndagwidwa ndi manyazi ndipo ndamizidwa mʼmavuto anga.
16 And if [my head] exalt itself, thou huntest me as a lion: and again thou shewest thyself marvelous upon me.
Ndipo ndikatukula mutu wanga, Inu mumandisaka ngati mkango ndiponso mumandiopseza ndi mphamvu yanu.
17 Thou renewest thy witnesses against me, and increasest thine indignation upon me; changes and warfare are with me.
Mumabweretsa mboni zatsopano potsutsana nane ndipo mkwiyo wanu pa ine umanka nukulirakulira ndi magulu anu olimbana nane amanka nachulukirachulukira.
18 Wherefore then hast thou brought me forth out of the womb? I had given up the ghost, and no eye had seen me.
“Chifukwa chiyani Inu munalola kuti ndibadwe? Ndi bwino ndikanafa diso lililonse lisanandione.
19 I should have been as though I had not been; I should have been carried from the womb to the grave.
Ndikanapanda kubadwa, kapena akanangonditenga nditabadwa kupita nane ku manda!
20 Are not my days few? cease then, and let me alone, that I may take comfort a little,
Kodi masiku anga owerengeka sali pafupi kutha? Ndilekeni kuti ndipumule pangʼono pokha
21 Before I go whence I shall not return, [even] to the land of darkness and of the shadow of death;
ndisanapite ku malo amene munthu sabwererako ku dziko la imfa ndi kwa mdima wandiweyani,
22 A land of thick darkness, as darkness [itself]; [a land] of the shadow of death, without any order, and where the light is as darkness.
ku dziko la mdima wandiweyani ndi chisokonezo, kumene kuwala kumakhala ngati mdima.”

< Job 10 >