< 1 Chronicles 17 >

1 And it came to pass, when David had taken up his abode in his house, that David said unto Nathan the prophet, Lo! I, am dwelling in a house of cedars, but, the ark of the covenant of Yahweh, is under curtains.
Davide atakhazikika mʼnyumba yake yaufumu, anawuza mneneri Natani kuti, “Ine pano ndikukhala mʼnyumba yaufumu yomanga ndi mitengo ya mkungudza, pomwe Bokosi la Chipangano la Yehova lili mu tenti.”
2 Then said Nathan unto David, All that is in thy heart, do, —for, God, is with thee.
Natani anayankha Davide kuti, “Chitani chilichonse chimene chili mu mtima mwanu, chifukwa Mulungu ali nanu.”
3 But so it was that, in that night, the word of God came unto Nathan, saying:
Usiku umenewo mawu a Mulungu anafika kwa Natani, ndipo anati,
4 Go and say unto David my servant, Thus, saith Yahweh, —Thou, shalt not build me a house, to dwell in;
“Pita kamuwuze mtumiki wanga Davide kuti, ‘Yehova akunena kuti, sudzandimangira ndiwe nyumba yokhalamo.’
5 seeing that I have not dwelt in a house, since the day that I brought up Israel, until this day, —but have been from tent to tent, and without a habitation.
Ine sindinakhalepo mʼnyumba kuyambira tsiku limene ndinatulutsa Israeli mʼdziko la Igupto mpaka lero lino. Ndakhala ndikuyenda kuchoka mʼtenti ina kupita mʼtenti ina, kuchoka malo ena kupita malo ena.
6 Wheresoever I have wandered with all Israel, spake I ever, a word, with one of the judges of Israel, whom I charged to shepherd my people, saying, —Wherefore have ye not built me a house of cedars?
Konse ndakhala ndikuyenda ndi Aisraeli onse, kodi ndinanenapo kwa wina aliyense wa atsogoleri awo amene ndinamulamula kuweta anthu anga kuti, ‘Kodi nʼchifukwa chiyani simunandimangire nyumba ya mitengo ya mkungudza?’”
7 Now, therefore, thus, shalt thou say unto my servant David, Thus, saith Yahweh of hosts, I myself, took thee from the pasture, from after the flock, —to become leader over my people Israel;
Ndipo tsopano umuwuze mtumiki wanga Davide kuti, “Yehova Wamphamvuzonse akuti, Ine ndinakutenga ku busa ukuweta nkhosa, kuti ukhale mtsogoleri wa anthu anga, Aisraeli.
8 and was with thee whithersoever thou didst go, and have cut off all thine enemies, from before thee, —and will make thee a name, like the name of the great ones, who are in the earth;
Ineyo ndinali nawe kulikonse kumene unkapita, ndipo ndachotsa adani ako onse pamaso pako. Tsopano ndidzakuza dzina lako kuti likhale mʼgulu la mayina a anthu otchuka kwambiri pa dziko lapansi.
9 and will appoint a place for my people Israel, and will plant them, and they shall inhabit their place, and be unsettled no more, —neither shall the sons of perversity again wear them out, as at the first;
Ndipo ndidzawapatsa malo anthu anga, Aisraeli ndipo ndidzawadzala pamalo awoawo kuti asadzavutitsidwenso. Anthu oyipa sadzawazunzanso monga ankachitira poyamba paja;
10 even from the days when I put judges in charge over my people Israel, and have subdued all thine enemies, —that I might make thee great, yea, a house, will Yahweh build for thee.
monga akhala akuchitira kuchokera nthawi imene ndinasankha atsogoleri a anthu anga Aisraeli. Ine ndidzagonjetsanso adani anu onse. “‘Ine ndikulengeza kwa iwe kuti Yehova adzakhazikitsa banja lako.
11 And it shall be that, when thy days are fulfilled, to sleep with thy fathers, then will I raise up thy seed after thee, who shall be of thy sons, —and I will establish his kingdom.
Masiku ako akadzatha ndipo ukadzatsatira makolo ako, Ine ndidzawutsa mphukira yako imene idzalowa mʼmalo mwako, mmodzi mwa ana ako, ndipo ndidzakhazikitsa ufumu wake.
12 He, shall build me a house, —and I will establish his throne unto times age-abiding.
Iye ndiye amene adzandimangira nyumba, ndipo ndidzakhazikitsa ufumu wake kwamuyaya.
13 I, will become his father, and, he, shall become my son, —and, my lovingkindness, will I not cause to depart from him, —as I caused it to depart from him who was before thee;
Ine ndidzakhala abambo ake, ndipo iye adzakhala mwana wanga. Ine sindidzasiya kumukonda monga ndinachitira ndi amene unalowa mʼmalo mwawo.
14 but I will cause him to remain over my house and over my kingdom, unto times age-abiding, —and, his throne, shall be established, unto times age-abiding.
Ndidzamuyika kukhala wolamulira nyumba yanga ndi ufumu wanga kwamuyaya. Mpando wake waufumu udzakhazikika kwamuyaya.’”
15 According to all these words, and according to all this vision, so, spake Nathan unto David.
Natani anafotokozera Davide mawu onse avumbulutso limene analandira.
16 Then entered King David, and tarried before Yahweh, —and said, Who am, I, O Yahweh God, and what is my house, that thou hast brought me hitherto;
Choncho Mfumu Davide analowa mu tenti nakhala pamaso pa Yehova, ndipo anati, “Ine ndine yani, Inu Yehova Mulungu, ndipo banja langa nʼchiyani kuti mundifikitse pamene ndafikapa?
17 and hast made this seem little in thine eyes, O God, in that thou hast spoken concerning the house of thy servant, for a great while to come? Thus wilt thou provide for me, according to the rank of manhood, and hast exalted me, O Yahweh God!
Inu Mulungu, kukhala ngati izi ndi zosakwanira pamaso panu, Inuyo mwayankhula zatsogolo la banja la mtumiki wanu. Mwandiyangʼana ndipo mwandiyesa ngati munthu wolemekezeka kwambiri pakati pa anthu, Inu Yehova Mulungu.”
18 What, yet further, can David say unto thee, [thus] to honour thy servant, —seeing that, thou thyself, knowest, thine own servant?
“Kodi Davide anenenso chiyani kwa Inu, pakuti mwachitira ulemu wotere mtumiki wanu? Pakuti Inu mukumudziwa mtumiki wanu.
19 O Yahweh, for the sake of thy servant, and according to thine own heart, hast thou done all this great thing, —making known all the great things.
Inu Yehova, chifukwa cha mtumiki wanu komanso mwa chifuniro chanu, mwachita chinthu chachikulu ichi ndipo mwawulula malonjezo anu aakulu onse.
20 O Yahweh, there is none like unto thee, yea there is no God besides thee, according to all that we have heard with our ears.
“Palibe wina wofanana nanu, Inu Yehova, ndipo palibe Mulungu wina koma Inu nokha monga tamvera ndi makutu athu.
21 Who then is like thy people Israel, a nation alone in the earth, —whom God went to redeem, to be his own people, to make for thyself a name for great and fearful things, to drive out, nations, from before thy people, whom thou didst redeem out of Egypt;
Ndipo ndi ndani wofanana ndi anthu anu Aisraeli, mtundu wokhawo pa dziko lapansi umene Mulungu wake anapita kukawuwombola, monga anthu akeake ndi kukadzitchukitsa yekha pochita zinthu zodabwitsa zazikulu, pothamangitsa mitundu ina pamaso pa anthu ake, amene Inu munawawombola ku Igupto?
22 and didst appoint thy people Israel for thyself as a people, unto times age-abiding, —thou thyself, also, O Yahweh, becoming their God?
Inu munawapanga anthu anu Aisraeli kukhala anuanu kwamuyaya, ndipo Inu, Inu Yehova ndinu Mulungu wawo.
23 Now, therefore, O Yahweh, the word which thou hast spoken concerning thy servant, and concerning his house, be it steadfast unto times age-abiding, —and do as thou hast spoken:
“Ndipo tsopano Yehova, sungani kwamuyaya lonjezo limene mwachita ndi mtumiki wanu ndi banja lake, likhazikitseni kwamuyaya. Chitani monga mwalonjezera,
24 yea let it be steadfast, and so let thy Name be magnified unto times age-abiding, saying, Yahweh of hosts, the God of Israel, is a God to Israel! seeing that, the house of David thy servant, is established before thee.
kotero dzina lanu likhazikike ndi kukhala lotchuka mpaka muyaya. Ndipo anthu adzanena kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa woyangʼanira Israeli, ndi Mulungu wa Israeli!’ Ndipo banja la mtumiki wanu Davide lidzakhazikika pamaso panu.
25 For, thou, O my God, hast unveiled the ear of thy servant, that thou wilt build for him a house, —for this cause, hath thy servant found [it in his heart] to pray before thee.
“Inu Mulungu wanga, mwaululira mtumiki wanu kuti mudzamumangira nyumba. Nʼchifukwa chake ine mtumiki wanu ndalimba mtima kupemphera motere.
26 Now, therefore, O Yahweh, thou, art God, —therefore hast thou spoken concerning thy servant this goodness.
Inu Yehova, ndinu Mulungu! Mwalonjeza zinthu zabwinozi kwa mtumiki wanu.
27 Now, therefore, let it please thee to bless the house of thy servant, that it may be unto times age-abiding before thee, —for, thou O Yahweh, hast blessed, and it is to be blessed unto times age-abiding.
Ndipo chakukomerani kudalitsa banja la mtumiki wanu kuti likhale pamaso panu mpaka muyaya. Pakuti Inu Yehova mwalidalitsa, lidzakhala lodalitsika mpaka muyaya.”

< 1 Chronicles 17 >