< Deuteronomy 31 >

1 And Moses went, and spake these words unto all Israel;
Tsono Mose anapita ndi kukayankhula mawu awa kwa Aisraeli onse:
2 and said unto them—A hundred and twenty years old, am I to-day, I can no more go out and come in, —Yahweh indeed hath said unto me, Thou shall not pass over this Jordan.
“Tsopano ndili ndi zaka 120, ndipo sindingathenso kukutsogolerani. Yehova wandiwuza kuti, ‘Iwe sudzawoloka Yorodani.’
3 Yahweh thy God, is passing over before thee, he, will destroy these nations from before thee so shalt thou dispossess them, —Joshua is passing over before thee, as Yahweh hath spoken.
Mwini wake Yehova Mulungu wanu ndiye amene adzakutsogolerani powoloka. Iye adzawononga mitundu ina yonse, ndipo inu mudzatenga dziko lawo. Yoswa adzakutsogoleraninso powoloka, monga momwe ananenera Yehova.
4 So will Yahweh do unto them as he did unto Sihon and unto Og, kings of the Amorites, and unto the land of them whom he destroyed.
Ndipo Yehova adzawawononga iwo monga momwe anawonongera Sihoni ndi Ogi, mafumu Aamori, amene Iye anawawononga pamodzi ndi dziko lawo.
5 So will Yahweh deliver them up before you, —and ye shall do unto them—according to all the commandment which I have commanded you.
Ambuye adzawapereka kwa inu, ndipo inu mukawachitire zonse zimene ndakulamulani.
6 Be firm and bold, do not fear nor tremble because of them, —for Yahweh thy God, it is who is going with thee, he will not fail thee nor forsake thee.
Khalani amphamvu ndi olimba mtima. Musachite nawo mantha kapena kunjenjemera pamaso pawo, chifukwa Yehova Mulungu wanu apita nanu. Sadzakusiyani kapena kukutayani.”
7 And Moses called for Joshua, and said unto him, in the sight of all Israel. Be firm and bold, for, thou, shalt go with this people into the land which Yahweh sware unto their fathers to give unto them, and, thou shalt cause them to inherit it.
Pamenepo Yehova anayitana Yoswa pamaso pa Aisraeli onse ndipo anamuwuza kuti, “Khala wamphamvu ndi wolimba mtima, pakuti iwe udzatsogolera anthu awa ku dziko limene Yehova analumbira kulipereka kwa makolo awo, ndipo iwe ukaligawe pakati pawo kuti likakhale cholowa chawo.
8 But, Yahweh, it is who is going before thee, he will be with thee, he will not fail thee nor forsake thee, —thou must not fear nor be dismayed.
Yehova mwini ndiye akukutsogolerani ndipo adzakhala nanu. Sadzakusiyani kapena kukutayani. Usachite mantha ndiponso usataye mtima.”
9 And Moses wrote this law, and delivered it unto the priests the sons of Levi, who were bearing the ark of the covenant of Yahweh, —and unto all the elders of Israel.
Choncho Mose analemba malamulo awa nawapereka kwa ansembe, ana Alevi, amene amanyamula Bokosi la Chipangano la Yehova, ndiponso kwa akuluakulu onse a Aisraeli.
10 And Moses commanded them, saying, —At the end of seven years in the appointed season of the year of release, during the festival of booths;
Kenaka Mose anawalamula kuti, “Pamapeto pa zaka zisanu ndi ziwiri zilizonse, chaka cha kukhululukidwa ngongole, pa nthawi ya Chikondwerero cha Misasa,
11 when all Israel cometh in to see the face of Yahweh thy God, in the place which he shall choose, thou shalt read this law before all Israel, in their hearing.
pamene Aisraeli onse abwera kudzaonekera pamaso pa Yehova Mulungu wanu pamalo pamene Iye adzasankhe, mudzawerenge malamulo onsewa iwo akumva.
12 Call together the people—the men and the women and the little ones, and thy sojourner who is within thy gates, —that they may hear, and that they may learn, so shall they revere Yahweh your God, and observe to do all the words of this law;
Mudzasonkhanitse anthu onse pamodzi, amuna, akazi ndi ana pamodzi ndi alendo amene akukhala mʼmizinda yanu, kuti adzawamve ndi kuphunzira kuopa Yehova Mulungu wanu ndi kutsatira mosamala mawu onse a mʼmalamulowa.
13 and that their children who know not, may hear and learn, that they may revere Yahweh your God, —all the days that ye are living upon the soil, which ye are passing over the Jordan to possess.
Ana awo amene sadziwa malamulo awa, ayenera kuwamva ndi kuphunzira kuopa Yehova Mulungu wanu nthawi zonse pamene mukukhala mʼdziko limene mukuwoloka Yorodani kukalitenga.”
14 Then said Yahweh unto Moses: Lo! thy days have drawn near that thou must die. Call Joshua and station yourselves in the tent of meeting, that I may command him. So Moses went, with Joshua, and they took their station in the tent of meeting.
Yehova anawuza Mose kuti, “Nthawi ya kufa kwako yafika. Itana Yoswa ndipo mubwere ku tenti ya msonkhano, kumene Ine ndidzamulangiza.” Choncho Mose ndi Yoswa anabwera ku tenti ya msonkhano.
15 And Yahweh appeared in the tent, in a pillar of cloud, —and the pillar of cloud stood, at the entrance of the tent.
Pamenepo Yehova anaonekera ku tenti mʼchipilala cha mtambo, ndipo mtambowo unayima pamwamba pa khomo lolowera mu tenti.
16 Then said Yahweh unto Moses, Lo! thou art about to sleep with thy fathers, —and this people will rise up, and go away unchastely after the gods of the foreigners of the land into the midst of whom they are entering, and will forsake me and break my covenant which I solemnised with them.
Ndipo Yehova anawuza Mose kuti, “Iwe ukupita kukapuma kumene kuli makolo ako, ndipo ukangomwalira, anthu awa adzayamba kupembedza milungu yachilendo ya mʼdziko limene akukalowamo. Adzanditaya ndi kuphwanya pangano lomwe ndinachita nawo.
17 Then will mine anger kindle upon them in that day, and I will forsake them and will hide my face from them and they shall be consumed, and many calamities and misfortunes shall find them out, —and they will say, in that day, Is it not because my God is not in my midst, that these calamities have found me out?
Tsiku limenelo Ine ndidzawakwiyira ndi kuwataya. Ndidzawabisira nkhope yanga, ndipo adzawonongedwa. Masautso ambiri ndi zovuta zambiri zidzawagwera, ndipo tsiku limenelo adzafunsa kuti, ‘Kodi masautso awa sanagwere ife chifukwa Yehova Mulungu wathu sali nafe?’
18 But, I, will utterly, hide, my face, in that day, because of all the wickedness which they have done, in that they have turned away unto other gods.
Ndipo Ine ndidzabisa ndithu nkhope yanga pa tsiku limenelo chifukwa cha zoyipa zimene anachita potembenukira kwa milungu ina.
19 Now, therefore write ye for you this Song, and teach it unto the sons of Israel put it in their mouths, —that this Song may become for me a witness against the sons of Israel.
“Tsopano ulembe mawu a nyimbo iyi ndipo uwaphunzitse Aisraeli, uwawuze kuti aziyimba, kuti ikhale mboni yanga yowatsutsa.
20 When I bring them upon the soil which I sware unto their fathers, flowing with milk and honey, and they shall eat and be filled and wax fat, then will they turn away unto other gods and serve them, and despise me, and break my covenant.
Pamene ndawalowetsa mʼdziko loyenda mkaka ndi uchi, dziko limene ndinalonjeza mwalumbiro kwa makolo awo, ndipo pamene adzadya ndi kukhuta ndi kumasangalala, iwo adzatembenukira kwa milungu ina ndi kumayipembedza, kundikana Ine ndi kuphwanya pangano langa.
21 And it shall come to pass, when many calamities and misfortunes shall find them out, then shall this Song respond to their face, as a witness, for it shall not be forgotten out of the mouth of their seed, for I know their imagination, which they are forming to-day, ere yet I bring them into the land of which I sware unto their fathers.
Ndipo pamene masautso ambiri ndi zovuta zambiri zidzawagwera, nyimbo iyi idzakhala mboni yanga yowatsutsa, chifukwa zidzukulu zawo sizidzayiwala nyimboyi. Ine ndikudziwa zimene iwo akulingalira kuchita, ngakhale kuti sindinawalowetse mʼdziko limene ndinalonjeza mwa lumbiro.”
22 Moses therefore wrote this Song on that day, —and taught it unto the sons of Israel.
Choncho Mose analemba nyimbo iyi tsiku limenelo ndi kuwaphunzitsa Aisraeli.
23 And he commanded Joshua, son of Nun, and said—Be firm and bold, for, thou shalt bring the sons of Israel into the land which I have sworn to them, —and, I, will be with thee.
Yehova analamula Yoswa mwana wa Nuni kuti, “Khala wamphamvu ndipo limba mtima, chifukwa udzalowetsa Aisraeli mʼdziko limene ndinawalonjeza mwa lumbiro, ndipo Ine mwini ndidzakhala nawe.”
24 And it came to pass, when Moses had made an end of writing the words of this law, upon a scroll, —until he had finished them,
Mose atatha kulemba malamulowa mʼbuku, osasiyako kanthu,
25 then Moses commanded the Levites, who were bearing the ark of the covenant of Yahweh, saying:
analamula Alevi amene ananyamula Bokosi la Chipangano la Yehova kuti,
26 Take this scroll of the law, and put it at the side of the ark of the covenant of Yahweh your God, —so shall it be there in thy midst as a witness.
“Tengani Buku ili la Malamulo ndi kuliyika pambali pa Bokosi la Chipangano la Yehova Mulungu wanu. Likhale kumeneko ngati mboni yokutsutsani.
27 For, I, know thy perverseness, and thy stiff neck, —lo! while I am yet alive with you to-day, ye are, quarrelling, with Yahweh, and how much more after my death?
Pakuti Ine ndikudziwa kuwukira kwanu ndi kuwuma mtima kwanu. Ngati inu mwakhala mukuwukira Yehova ine ndili moyo ndiponso ndili nanu pamodzi, nanga mudzawukira motani ine ndikamwalira!
28 Call together unto me all the elders of your tribes and your officers, —and let me speak in their hearing these words, and let me take to witness against them the heavens and the earth.
Mundisonkhanitsire atsogoleri onse a mafuko anu pamodzi ndi akuluakulu onse, kuti ndiyankhule mawu awa iwo akumva ndipo kumwamba ndi dziko lapansi zikhale mboni yowatsutsa.
29 For I know that after my death, ye will break faith, and turn aside out of the way which I have commanded you, —and calamity will befall you in the afterpart of the days, because ye will do the thing that is wicked in the eyes of Yahweh, to provoke him with the work of your own hands.
Chifukwa ndikudziwa kuti ine ndikamwalira mudzayipa kwambiri ndi kutembenuka kuleka njira imene ndinakulamulani. Masiku amene akubwera, masautso adzakugwerani chifukwa mudzachita zoyipa pamaso pa Yehova ndi kuputa mkwiyo wake chifukwa cha zimene manja anu anapanga.”
30 So Moses spake in the hearing of all the convocation of Israel the words of this Song, until they were ended: —
Ndipo Mose ananena mawu a nyimbo iyi kuyiimba koyambira mpaka potsiriza gulu lonse la Aisraeli likumva:

< Deuteronomy 31 >