< Hosea 13 >

1 When Ephraim, spake, there was terror, exalted was, he, in Israel, —but, when he became guilty with Baal, then he died.
Kale Efereimu ankati akayankhula, anthu ankanjenjemera; anali wolemekezeka mu Israeli. Koma analakwa popembedza Baala, motero anafa.
2 Now, therefore they go on to sin, and have made them a Molten Thing out of their silver, after the notion of idols, the workmanship of craftsmen, all of it! Of them, are they saying—Ye sacrificers of men! The Great Calf, shall ye surely kiss!
Tsopano akunka nachimwirachimwirabe; akudzipangira mafano pogwiritsa ntchito siliva wawo, zifanizo zopangidwa mwaluso, zonsezo zopangidwa ndi amisiri. Amanena za anthu awa kuti, “Amatenga munthu ndi kumupereka nsembe ndipo amapsompsona fano la mwana wangʼombe.”
3 Therefore, shall they become like the morning cloud, and like the dew early departing, —like chaff storm-driven out of the threshing-floor, and like smoke out of a chimney.
Choncho adzakhala ngati nkhungu yammawa, ngati mame amene amakamuka msanga, ngati mungu wowuluka kuchokera pa malo opunthira tirigu, ngati utsi umene ukutulukira pa zenera.
4 Yet, I, Yahweh, have been thy God from the land of Egypt, —and, god beside me, shalt thou not acknowledge, for, saviour, is there none besides me.
Koma Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndinakutulutsani mu Igupto. Simuyenera kudziwa Mulungu wina, koma Ine ndekha, palibe Mpulumutsi wina kupatula Ine.
5 I, tended thee in the desert, —in a land parched with drought:
Ndinakusamalira mʼchipululu, mʼdziko lotentha kwambiri.
6 Whenever they were pastured, then were they satisfied, They were satisfied, and their heart, was lifted up, —because of this, they forgat me.
Pamene ndinawadyetsa, iwo anakhuta; iwo atakhuta anayamba kunyada; ndipo anandiyiwala Ine.
7 Therefore am I become to them as a lion, —As a leopard by the way, do I watch.
Motero ndidzawalumphira ngati mkango, ndidzawabisalira mu msewu ngati kambuku.
8 I will fall upon them as a bear bereaved, and will read asunder the enclosure of their heart, —that I may devour them there, like a lioness, the wild beast of the field, shall tear them in pieces.
Ngati chimbalangondo cholandidwa ana ake, ndidzawambwandira ndi kuwathyolathyola. Ndidzawapwepweta ngati mkango; chirombo chakuthengo chidzawakhadzula.
9 It hath utterly destroyed thee, O Israel, for it was against me, as thy helper!
“Iwe Israeli, wawonongedwa, chifukwa ukutsutsana ndi Ine, ukutsutsana ndi mthandizi wako.
10 Where is thy king, then, that he may save thee throughout all thy cities? and thy judges, concerning whom thou saidst, Oh give me a king and rulers?
Kodi mfumu yako ili kuti, kuti ikupulumutse? Olamulira ako a mʼmizinda yonse ali kuti, amene iwe unanena za iwo kuti, ‘Patseni mfumu ndi akalonga?’
11 I might give thee a king in mine anger, and take him away in my wrath.
Choncho Ine ndinakupatsani mfumu mwachipseramtima, ndipo ndinayichotsa mwaukali.
12 Bound up, is the iniquity of Ephraim, stored away, his sin.
Kulakwa kwa Efereimu kwasungidwa, machimo ake alembedwa mʼbuku.
13 The pangs of a woman in labour, shall overtake him, —he, is a son, not wise, for, now, he cannot stand still, when children are about to be born.
Zowawa zonga za mayi pa nthawi yobala mwana zamugwera, koma iye ndi mwana wopanda nzeru, pamene nthawi yake yobadwa yafika iyeyo safuna kutuluka mʼmimba mwa amayi ake.
14 Out of the hand of hades, will I ransom them, out of death, will I redeem them, —Where is thy pestilence, O death? Where thy plague, O hades? Repentance, shall be hid from mine eyes. (Sheol h7585)
“Ndidzawapulumutsa ku mphamvu ya manda; ndidzawawombola ku imfa. Kodi iwe imfa, miliri yako ili kuti? Kodi iwe manda, kuwononga kwako kuli kuti? “Sindidzachitanso chifundo, (Sheol h7585)
15 Though, he, among brethren, be fruitful, there shall come in an east wind, the blast of Yahweh out of the desert coming up, that his spring, may dry up, and his fountain, be exhausted, he, will rob the treasure-house of all the vessels of delight.
ngakhale Efereimu akondwe pakati pa abale ake, mphepo ya kummawa yochokera kwa Yehova idzabwera, ikuwomba kuchokera ku chipululu. Kasupe wake adzaphwa ndipo chitsime chake chidzawuma. Chuma chake chonse chamtengowapatali chidzafunkhidwa ndipo chidzatengedwa.
16 Samaria, shall be held guilty, for she hath rebelled against her God, By the sword, shall they fall, their infants, shall be dashed to the ground, and, his women with child, shall be ripped up.
Anthu a ku Samariya adzalangidwa chifukwa cha zolakwa zawo, chifukwa anawukira Mulungu wawo. Adzaphedwa ndi lupanga; ana awo adzaphedwa mowamenyetsa pansi, akazi awo oyembekezera adzatumbulidwa pa mimba.”

< Hosea 13 >