< Isaiah 53 >

1 Who believed what we have heard? And, the arm of Yahweh, to whom was it revealed?
Ndani wakhulupirira zimene tanenazi; kapena ndani amene Yehova wamuzindikiritsa mphamvu zake?
2 When he came up as a sapling before him. And as a root-sprout out of dry ground, He had neither beauty nor majesty, —When we beheld him, there was nothing to behold, that we should desire him;
Iye anakula ngati mphukira pamaso pake, ndiponso ngati muzu mʼnthaka yowuma. Iye analibe thupi labwino kapena nkhope yokongola yoti ife nʼkumamuchewukira, analibe maonekedwe woti ife nʼkumamukhumbira.
3 Despised was he, and forsaken of men, Man of pains and familiar with sickness, —Yea, like one from whom the face is hidden, Despised, and we esteemed him not.
Iye ananyozedwa ndi kukanidwa ndi anthu, munthu amene moyo wake unali wamasautso, wozolowera zowawa, ndipo anali ngati munthu amene anzake amaphimba nkhope zawo akamuona. Iye ananyozedwa, ndipo ife sitinamuyese kanthu.
4 Yet surely, our sicknesses, he, carried, And, as for our pains, he bare the burden of them, —But, we, accounted him stricken. Smitten of God and humbled,
Ndithudi, iye anamva zowawa mʼmalo mwa ife; ndipo anasautsidwa mʼmalo mwathu. Koma ife tinkaganiza kuti ndi Mulungu amene akumulanga, kumukantha ndi kumusautsa.
5 Yet, he, was pierced for transgressions that were ours, was crushed for iniquities that were ours, —the chastisement for our well-being, was upon him, And by his stripes, there is healing for us.
Koma iye analasidwa chifukwa cha zolakwa zathu, ndipo anamuzunza chifukwa cha zoyipa zathu; iye analangidwa kuti ife tikhale ndi mtendere, ndipo ndi mabala ake ife tinachiritsidwa.
6 We all, like sheep, had gone astray, Every man—to his way, had we burned, —And Yahweh! caused to light upon him The guilt of, us all!
Ife tonse, ngati nkhosa, tasochera, aliyense mwa ife akungodziyendera; ndipo Yehova wamusenzetsa zoyipa zathu zonse.
7 Hard pressed—yet, he, humbled himself Nor opened his mouth—As, a lamb, to the slaughter, is led, And, as a sheep, before her shearers, is dumb—Nor opened his mouth.
Anthu anamuzunza ndi kumusautsa, koma sanayankhule kanthu. Monga mwana wankhosa wopita naye kokamupha amachitira, kapena monga nkhosa imakhalira duu poyimeta, momwemonso iye sanatsekule pakamwa pake.
8 By constraint and by sentence, was he taken away, And of his age, who considered That he was cut off out of the land of the living, For my people’s transgression, did the stroke fall on him?
Atatha kumugwira mwankhanza ndikumuyimba mlandu, kenaka anapita naye kukamupha. Ndipo ndani amene analabadirako za zidzukulu zake, poona kuti iye anachotsedwa mʼdziko la anthu amoyo? Ndani anaganizirapo poona kuti iye anakanthidwa chifukwa cha zolakwa za anthu anga?
9 And, appointed with lawless men, was his grave, And with the wicked, his tomb, —Though no violence, had he done, Nor was guile in his mouth.
Anamukonzera manda ake pamodzi ndi anthu oyipa ndipo anamuyika mʼmanda pamodzi ndi anthu achuma, ngakhale kuti iye sanachite za chiwawa, kapena kuyankhula za chinyengo.
10 Yet, Yahweh, purposed to bruise him, He laid on him sickness: —If his soul become an offering for guilt, He shall see a seed, He shall prolong his days, —And the purpose of Yahweh, in his hand, shall prosper:
Komatu ndi Yehova amene anafuna kuti amuzunze ndi kumusautsa. Yehova anapereka moyo wa mtumiki wake kuti ukhale nsembe yoperekedwa chifukwa cha zolakwa. Tsono iye adzaona zidzukulu zake ndipo adzakhala ndi moyo wautali, ndipo chifuniro cha Yehova chidzachitika mwa iye.
11 Of the travail of his soul, shall he see He shall be satisfied with his knowledge, A setting right when set right himself, shall my Servant win for the Many, Since of their iniquities, he, taketh the burden.
Atatha mazunzo a moyo wake, adzaona kuwala, ndipo adzakhutira. Mwa nzeru zake mtumiki wanga wolungamayo adzalungamitsa anthu ambiri, popeza adzasenza zolakwa zawo.
12 Therefore, will I give him a portion in the great, And the strong, shall he apportion as spoil, Because he poured out, to death his own soul, And with transgressors, let himself be numbered, —Yea, he, the sin of Many, bare, And for transgressors, interposeth.
Motero Ine ndidzamupatsa ulemu pamodzi ndi akuluakulu, adzagawana zofunkha ndi ankhondo amphamvu, popeza anapereka moyo wake mpaka kufa, ndipo anamuyika mʼgulu la anthu olakwa kuti akhululukidwe. Pakuti iye anasenza machimo a anthu ambiri, ndipo anawapempherera anthu olakwa.

< Isaiah 53 >