< Luke 13 >

1 Now there were present some, in that very season, bringing tidings to him, concerning the Galilaeans whose blood Pilate had mingled with their sacrifices.
Nthawi yomweyo panali ena amene analipo omwe amamuwuza Yesu za Agalileya amene magazi awo Pilato anawasakaniza ndi nsembe zawo.
2 And, answering, he said unto them—Suppose ye, that, these Galilaeans, had become, sinners beyond all the Galilaeans, because, these things, they have suffered?
Yesu anayankha kuti, “Kodi mukuganiza kuti Agalileya amenewa anali ochimwa kwambiri kuposa Agalileya ena onse chifukwa anavutika mʼnjira iyi?
3 Nay! I tell you, but, except ye repent, ye, all, in like manner, shall perish.
Ine ndikuti, ayi! Koma ngati inu simutembenuka mtima, inunso mudzawonongeka nonse.
4 Or, those eighteen, upon whom fell the tower in Siloam, and slew them, suppose ye that, they, had become, debtors, beyond all the men who were dwelling in Jerusalem?
Kapena anthu 18 aja amene anafa nsanja ya Siloamu itawagwera, kodi mukuganiza kuti iwo aja anali ochimwa kwambiri kuposa onse amene amakhala mu Yerusalemu?
5 Nay! I tell you, but, except ye repent, ye, all, in the same way, shall perish.
Ine ndikuti, ayi! Koma ngati inu simutembenuka mtima, inunso mudzawonongeka nonse.”
6 And he went on to speak this parable: —A certain man had, a fig-tree, planted in his vineyard, and he canto seeking fruit therein, and found none.
Kenaka Iye anawawuza fanizo kuti, “Munthu wina anali ndi mtengo wamkuyu, umene anadzala mʼmunda wamphesa, ndipo Iye anapita kukayangʼana zipatso, koma sanazipeze.
7 And he said unto the vine-dresser—Lo! three years, I come, seeking fruit in this fig-tree, and find none. Cut it down! Why doth it make, even the round useless?
Tsono kwa munthu amene amasamalira munda wamphesawo anati, ‘Kwa zaka zitatu tsopano ndakhala ndikubwera kudzafuna chipatso pa mtengo uwu ndipo sindinachipeze. Udule! Nʼchifukwa chiyani ukuwononga nthaka?’
8 And, he, answering, saith unto him—Sir! let it alone this year also, until such time as I dig about it, and throw in manure, —
“Munthuyo anayankha kuti, ‘Bwana, tawusiyani kwa chaka chimodzi chokha ndipo ine ndikumba ngalande mozungulira ndi kuthira manyowa.
9 and if it may bear fruit for the future; …but, otherwise, certainly, thou shalt cut it down.
Ngati udzabale zipatso chaka chamawa, zili bwino! Koma ngati sudzabala, pamenepo mudzawudule.’”
10 And he was teaching in one of the synagogues, on the Sabbath.
Pa Sabata Yesu ankaphunzitsa mʼsunagoge ina,
11 And lo! a woman, having a spirit of weakness eighteen years, —and was bowed together, and unable to lift herself up, at all.
ndipo momwemo munali mayi amene anali ndi mzimu woyipa umene unamudwalitsa zaka 18. Iye anali wokhota msana ndipo samatha kuweramuka ndi pangʼono pomwe.
12 And, seeing her, Jesus called her and said to her—Woman! thou art loosed from thy weakness, —
Yesu atamuona anamuyitana kutsogolo ndipo anati kwa iye, “Amayi, mwamasulidwa ku mavuto.”
13 and laid on her his hands; and, instantly, she was made straight again, and began glorifying God.
Kenaka anasanjika manja ake pa iye, ndipo nthawi yomweyo anawongoka nayamika Mulungu.
14 But the synagogue-ruler, answering, being greatly displeased that, on the Sabbath, Jesus had healed, began saying unto the multitude—Six days, there are, in which men ought to get their work done; On them, therefore, come and be healed, and, not on the day of rest.
Chifukwa cha kuyipidwa kuti Yesu anachiritsa pa Sabata, wolamulira sunagoge anati kwa anthu, “Pali masiku asanu ndi limodzi ogwira ntchito. Choncho bwerani kuti mudzachiritsidwe masiku amenewo osati pa Sabata.”
15 The Lord answered him, and said—Hypocrites! Doth not, each one of you, on the Sabbath, loose his ox or ass from the manger, and, leading it away, give it drink?
Ambuye anamuyankha kuti, “Iwe wachiphamaso! Kodi nonsenu simumasula pa Sabata ngʼombe zanu kapena bulu kumuchotsa mʼkhola ndi kupita naye kukamupatsa madzi?
16 But, this woman, being a daughter of Abraham, whom Satan had bound, lo! eighteen years, was there not a needs-be that she should be loosed from this bond, on the day of rest?
Nanga mayiyu, amene ndi mwana wa Abrahamu, ndipo anamangidwa ndi Satana zaka 18, kodi siwoyenera kuti amasulidwe msinga imeneyi pa tsiku la Sabata?”
17 And, as he was saying, these, things, all who had been setting themselves against him were being put to shame; and, all the multitude, were rejoicing over all the glorious things which were being brought to pass by him.
Atanena izi, onse omutsutsa anachititsidwa manyazi, koma anthu anakondwera ndi zodabwitsa zonse zimene Iye anazichita.
18 He went on to say, therefore—Whereunto, is the kingdom of God, like? And, whereunto, shall I liken it?
Kenaka Yesu anafunsa kuti, “Kodi ufumu wa Mulungu uli ngati chiyani? Kodi Ine ndingawufanizire ndi chiyani?
19 It is, like, unto a grain of mustard seed, which a man took and cast into his own garden; and it grew, and became a tree, and, the birds of heaven, lodged amongst its branches.
Uli ngati mbewu ya mpiru, imene munthu anatenga ndi kudzala mʼmunda mwake. Inakula, nʼkukhala mtengo, ndipo mbalame zamlengalenga zinakhala mʼnthambi zake.”
20 And, again, he said—Whereunto, shall I liken the kingdom of God?
Iye anafunsanso kuti, “Kodi ufumu wa Mulungu ndingawufanizire ndi chiyani?
21 It is, like leaven, which a woman took and hid in three measures of flour, until, the whole, was leavened.
Uli ngati yisiti amene mayi anatenga ndi kusakaniza ndi ufa wambiri mpaka anafufumitsa ufawo.”
22 And he was journeying on, city by city and village by village, and making, progress, unto Jerusalem.
Ndipo Yesu anayendayenda mʼmizinda ndi mʼmidzi, kumaphunzitsa pamene Iye ankapita ku Yerusalemu.
23 And one said unto him—Lord! are they, few, who are being saved? And, he, said unto them—
Wina anamufunsa Iye kuti, “Ambuye, kodi ndi anthu ochepa okha amene adzapulumutsidwe?” Iye anawawuza kuti,
24 Be striving to enter through the narrow door; for, many, I say unto you, will seek to enter, and will not be able, —
“Yesetsani kulowa pa khomo lopapatiza, chifukwa ndikukuwuzani kuti ambiri adzafuna kulowa koma sadzatha kutero.
25 when once the householder shall rouse himself, and lock the door, and ye begin to stand, outside, and to knock at the door, saying—Lord! open to us; and he shall answer and say unto you—I know you not, whence ye are.
Nthawi yomwe mwini nyumba adzayimirira ndi kutseka chitseko, inu mudzayima kunja kugogoda ndi kudandaula kuti, ‘Bwana, tatitsekulirani khomo.’ “Koma Iye adzayankha kuti, ‘Ine sindikukudziwani ndipo sindikudziwanso kumene mwachokera.’
26 Then, will ye begin to say—We did eat and drink in thy presence, and, in our broadways, thou didst, teach;
“Ndipo inu mudzati, tinkadya ndi kumwa ndi inu ndipo munkaphunzitsa mʼmisewu yathu.
27 And he will speak, saying unto you—I know not whence ye are; Depart from me, all workers of unrighteous—
“Koma Iye adzayankha kuti, ‘Ine sindikukudziwani ndipo sindikudziwanso kumene mwachokera. Chokereni inu nonse ochita zoyipa!’
28 There, will be weeping and gnashing of teeth, as soon as ye see Abraham and Isaac and Jacob and all the prophets, in the kingdom of God, and, yourselves, being thrust forth outside.
“Mudzalira ndi kukuta mano mukadzaona Abrahamu, Isake ndi Yakobo ndi aneneri onse ali mu ufumu wa Mulungu koma inuyo mutaponyedwa kunja.
29 And they shall have come from east and west, and from north and south, and be made recline in the kingdom of God.
Anthu adzachokera kummawa ndi kumadzulo, kumpoto ndi kummwera, kudzakhala pa phwando mu ufumu wa Mulungu.
30 And lo! there are, last, who shall be, first, and there are, first, who shall be, last;
Ndithudi otsirizira ndiye adzakhale oyambirira, ndipo oyambirira ndiye adzakhale otsirizira.”
31 In that very hour, came near certain Pharisees, saying unto him, Go forth, and be journeying hence, because, Herod, desireth to slay thee.
Pa nthawi imeneyo Afarisi anabwera kwa Yesu ndipo anati kwa Iye, “Chokani malo ano ndipo pitani kumalo ena aliwonse. Herode akufuna kukuphani.”
32 And he said unto them—Go and tell this fox, Lo! I am casting out demons, and, cures, am I finishing, to-day, and to-morrow, —
Iye anayankha kuti, “Pitani kawuzeni nkhandweyo, Ine ndikutulutsa ziwanda ndi kuchiritsa anthu lero ndi mawa ndipo tsiku lachitatu ndidzakwaniritsa cholinga changa.”
33 and, on the third, I am to be made perfect. Nevertheless, I must needs, to-day, and tomorrow, and the following, be journeying on, because it is impossible that a prophet perish, outside Jerusalem.
Mʼnjira ina iliyonse, Ine ndiyenera kupitirira ulendo wanga lero, mawa ndi mkuja. Zoona nʼzakuti mneneri sangafere kunja kwa Yerusalemu.
34 Jerusalem! Jerusalem! she that slayeth the prophets, and stoneth them that are sent unto her! How often, have I desired to gather together thy children, like as a hen, her own brood, under her wings, —and ye did not desire!
Iwe Yerusalemu, Yerusalemu! Umapha aneneri ndi kuwagenda miyala anthu amene atumizidwa kwa iwe. Nthawi zambiri ndakhala ndikufuna kusonkhanitsa ana ako pamodzi, monga nkhuku imasonkhanitsira anapiye pansi pa mapiko ake, koma iwe sunafune!
35 Lo! your house is left to you. [And] I say unto you—In nowise shall ye see me, until ye say, —Blessed, is he that cometh in the name of the Lord!
Taona, nyumba yako yasanduka bwinja. Ine ndikukuwuza kuti, sudzandionanso mpaka pamene udzati, “Wodala amene akubwera mʼdzina la Ambuye!”

< Luke 13 >