< Philippians 4 >

1 So then, my brethren, beloved and longed for, my joy and crown, —thus, stand fast in the Lord, beloved.
Tsono abale anga, ndimakukondani ndipo ndikukulakalakani. Ndinu chimwemwe changa ndi chipewa cha ulemerero wanga. Abwenzi okondedwa, chilimikani choncho mwa Ambuye.
2 Euodia, I exhort, and, Syntche, I exhort, —on the same thing, to be resolved in the Lord: —
Ndikudandaulira Euodiya ndi Suntuke kuti akhale ndi mtima umodzi mwa Ambuye.
3 Yea! I request thee also, true yokefellow, be thou helping together with these women, —who, indeed, in the joyful message, have maintained the combat with me, along with Clement also, and the rest of my fellow-workers, whose names, are in the book of life.
Inde, ndikupempha iwe mnzanga pa ntchitoyi, thandiza amayiwa amene ndagwira nawo ntchito ya Uthenga Wabwino pamodzi ndi Klementonso ndi ena onse antchito anzanga amene mayina awo ali mʼbuku lamoyo.
4 Rejoice in the Lord always: again, I will say—rejoice!
Nthawi zonse muzikondwa mwa Ambuye. Ndikubwerezanso; muzikondwa!
5 Let, your considerateness, be known unto all men. The Lord, is near: —
Kufatsa kwanu kuzioneka pamaso pa anthu onse. Ambuye anu ali pafupi.
6 For nothing, be anxious, but, in everything, by your prayer and supplication with thanksgiving, let, your petitions, be made known unto God;
Musade nkhawa ndi kanthu kalikonse, koma pa china chilichonse, mwa pemphero ndi chidandaulo pamodzi ndi chiyamiko, perekani zopempha zanu kwa Mulungu.
7 And, the peace of God, which riseth above every mind, shall guard your hearts and your thoughts, in Christ Jesus.
Ndipo mtendere wa Mulungu, umene upambana nzeru zonse udzasunga bwino mitima yanu ndi maganizo anu mwa Khristu Yesu.
8 For the rest, brethren, whatsoever things are true, whatsoever things are dignified, whatsoever things are righteous, whatsoever things are chaste, whatsoever things are lovely, whatsoever things are of good report, —if there be any virtue, and if any praise, the same, be taking into account;
Potsiriza, abale, muziyika mtima wanu pa zinthu zilizonse zabwino ndi zotamandika monga, zinthu zoona, zinthu zolemekezeka, zinthu zolungama, zinthu zoyera, zinthu zokongola ndi zinthu zosiririka.
9 The things which ye have both learned, and accepted, and heard, and seen in me, the same, practise; —and, the God of peace, shall be with you.
Muzichita chilichonse chimene mwaphunzira kapena kulandira kapena kumva kuchokera kwa ine kapena mwaona mwa ine. Ndipo Mulungu wamtendere adzakhala nanu.
10 Howbeit I have been made to rejoice in the Lord greatly—that, now, at length, ye have flourished in your care for me, —although, indeed, ye were caring, but lacked opportunity.
Ndikukondwa kwambiri mwa Ambuye kuti patapita nthawi tsopano mwayambanso kuonetsa kuti mumandiganizira. Zoonadi, mwakhala mukundikumbukira, koma munalibe mpata woti muonetsere zimenezi.
11 Not that, as to coming short, I am speaking, for, I, have learned, in whatsoever circumstances I am, to be, independent:
Sindikunena izi chifukwa choti ndikusowa thandizo, poti ine ndaphunzira kukhala wokwaniritsidwa ndi zimene ndili nazo.
12 I know [what it is] even to be kept low, and I know [what it is] to have more than enough, —in every way, and in all things, have I been let into the secret—both to be well fed, and to be hungering, both to have more than enough, and to be coming short:
Ndimadziwa kusauka nʼkutani, ndipo ndimadziwa kulemera nʼkutani. Ndaphunzira chinsinsi chokhala wokhutitsidwa mwa njira ina iliyonse, kaya nʼkudya bwino kapena kukhala ndi njala, kaya kukhala ndi chuma kapena umphawi.
13 I have might, for all things, in him that empowereth me.
Ndikhoza kuchita zonse kudzera mwa Iye amene amandipatsa mphamvu.
14 Nevertheless, nobly, have ye done, in taking fellowship with me in my tribulation.
Komatu munachita bwino kundithandiza mʼmavuto anga.
15 Ye know, moreover, even ye, Philippians, —that, in the beginning of the glad-message, when I went forth from Macedonia, not, so much as one assembly, with me had fellowship—in the matter of giving and receiving—save, ye alone, —
Ndipo inu Afilipi mukudziwa kuti masiku oyambirira olalikira Uthenga Wabwino, nditachoka ku Makedoniya, panalibe mpingo ndi umodzi omwe umene unagwirizana nane pa nkhani yopereka ndi kulandira, kupatula inu.
16 That, even in Thessalonica, both once and again, unto my need, ye sent: —
Pakuti ngakhale pamene ndinali ku Tesalonika, munanditumizira kangapo zondithandiza pa zosowa zanga.
17 Not that I seek after the gift, but I seek after the fruit that is to abound unto your account.
Osati ndikufuna mphatso zanu, koma ndikufuna kuti pa zimene muli nazo pawonjezerekepo phindu.
18 But I have all things in full, and have more than enough, I am filled, having welcomed from Epaphroditus the things that came from you, —a fragrance of sweet smell, an acceptable sacrifice, well pleasing unto God.
Ndalandira zonse ndipo ndili nazo zokwanira zoposa zosowa zanga popeza ndalandira kwa Epafrodito mphatso zochuluka zimene munatumiza. Ndizo zopereka za fungo labwino, nsembe zolandiridwa zokondweretsa Mulungu.
19 And, my God, will fill up your every need, according to his riches in glory in Christ Jesus.
Ndipo Mulungu wanga adzakwaniritsa zosowa zanu monga mwa chuma chake chaulemerero mwa Khristu Yesu.
20 Now, unto our God and Father, be the glory—unto the ages of ages. Amen! (aiōn g165)
Kwa Mulungu ndi Atate athu, kukhale ulemerero mpaka muyaya. Ameni. (aiōn g165)
21 Salute ye every saint in Christ Jesus. The brethren who are with me, salute you.
Perekani moni kwa oyera mtima onse mwa Khristu Yesu. Abale amene ali ndi ine akupereka moni wawo.
22 All the saints salute you, but especially they who are of Caesar’s household.
Oyera mtima onse akupereka moni, makamaka iwo a ku nyumba ya Kaisara.
23 The favour of our Lord Jesus Christ, be with your spirit.
Chisomo cha Ambuye Yesu Khristu chikhale ndi mzimu wanu. Ameni.

< Philippians 4 >