< Nehemiah 4 >

1 And it was just when he heard Sanballat that we [were] rebuilding the wall and it burned to him and he was angry greatly and he mocked the Jews.
Sanibalati atamva kuti tikumanganso khoma anapsa mtima nayamba kuseka ndi kunyogodola Ayuda kwambiri.
2 And he said - before brothers his and [the] army of Samaria and he said what? [are] the Jews feeble doing ¿ will they restore for themselves ¿ will they offer sacrifices ¿ will they finish in the day ¿ will they restore the stones from [the] heaps of debris and they [are] burned.
Ndipo anayankhula pamaso pa abale ake ndi asilikali a Samariya kuti, “Kodi Ayuda ofowokawa akuchita chiyani? Kodi iwo nʼkumanganso khoma? Kodi adzaperekanso nsembe? Kodi adzatsiriza ntchitoyi tsiku limodzi? Kodi adzachita kutenga miyala yakale ija ndi mmene inapseramo?”
3 And Tobiah the Ammonite [was] beside him and he said also [that] which they [are] building if it will go up a fox and it will break down [the] wall of stones their.
Tobiya wa ku Amoni, amene anali naye anati, “Chimene akumangacho ngati nkhandwe itakwerapo, itha kugwetsa khoma lawolo!”
4 Hear O God our for we are contempt and return reproach their to own head their and give them to plunder in a land of captivity.
Tsono ndinayamba kupemphera kuti, “Timvereni, Inu Mulungu wathu, mmene akutinyozera. Mulole kuti mawu awo onyoza awabwerere, ndipo atengedwe ukapolo ku dziko lachilendo.
5 And may not you cover over iniquity their and sin their from to before you may not it be wiped out for they have provoked to anger to before the builders.
Musawakhululukire mphulupulu zawo kapena kufafaniza machimo awo pamaso panu popeza aputa ukali wanu pamaso pa anthu omanga khoma.”
6 And we rebuilt the wall and it was joined together all the wall to middle its and it belonged a heart to the people to work.
Choncho ife tinamangabe khomalo kufikira lonse litafika theka la msinkhu wake, chifukwa chakuti anthu anagwira ntchitoyo ndi mtima wawo wonse.
7 And it was just when he heard Sanballat and Tobiah and the Arabs and the Ammonites and the Ashdodites that it had gone up [the] repair of [the] walls of Jerusalem that they had begun the broken down [parts] to be closed and it burned to them exceedingly.
Koma pamene Sanibalati, Tobiya, Aarabu, Aamoni ndi anthu a ku Asidodi anamva kuti ntchito yokonzanso makoma a Yerusalemu ikupitirirabe ndipo kuti mipata ikutsekedwa, anapsa mtima kwambiri.
8 And they conspired all of them together to come to wage war against Jerusalem and to make for it confusion.
Tsono onse anapangana za chiwembu kuti abwere ndi kudzathira nkhondo anthu a ku Yerusalemu ndi kuyambitsa mapokoso pakati pawo.
9 And we prayed to God our and we stationed a guard on them by day and night because of them.
Koma ife tinapemphera kwa Mulungu wathu ndipo tinayika alonda otiteteza kwa adaniwo usiku ndi usana.
10 And it said Judah it has failed [the] strength of the burden-bearer[s] and the debris [is] much and we not we will be able to rebuild the wall.
Pa nthawi yomweyi anthu a ku Yuda anati, “Mphamvu za anthu onyamula zinyalala zikutha ndipo pali zinyalala zambiri. Choncho ife sititha kumanga khomali.”
11 And they said opponents our not they will know and not they will see until that we will come into [the] midst of them and we will kill them and we will put an end to the work.
Adani athunso anati, “Iwo asanadziwe izi, kapena kutiona, tidzakhala tili pakati pawo ndipo tidzawapha ndi kuyimitsa ntchitoyo.”
12 And it was just when they came the Jews who were dwelling beside them and they said to us ten times from all the places which you will turn to us.
Ndipo Ayuda amene ankhala pafupi ndi adani athuwo anabwera kakhumi konse kuchokera konse kumene ankakhala kudzatiwuza kuti tibwereko ku ntchito.
13 And I stationed from [the] lower parts of the place from behind of the wall (in the open places *QK) and I stationed the people to clans with swords their spears their and bows their.
Choncho kumbuyo kwa khoma, cha mʼmunsi mwake komanso malo amene anali asanathe ndinayikamo anthu mʼmabanja atatenga malupanga, mikondo ndi mauta awo.
14 And I saw and I arose and I said to the nobles and to the officials and to [the] rest of the people may not you be afraid of them [the] Lord great and awesome remember and fight on brothers your sons your and daughters your wives your and houses your.
Popeza anthu ankachita mantha, tsono ndinawawuza anthu olemekezeka, akuluakulu ndiponso anthu onse kuti, “Musawaope. Kumbukirani kuti Ambuye ndi wamkulu ndipo ndi woopsa. Choncho menyerani nkhondo abale anu, ana aamuna ndi aakazi, akazi anu ndi nyumba zanu.”
15 And it was just when they heard enemies our that it was known to us and he had frustrated God purpose their (and we returned *Qk) all of us to the wall each one to work his.
Adani athu atamva kuti ife tadziwa za chiwembu chawo, anadziwanso kuti Yehova walepheretsa zimene ankafuna kutichita. Choncho tinabwerera aliyense ku ntchito yake yomanga khoma.
16 And it was - from the day that half of young men my [were] doing the work and half of them [were] holding and the spears the shields and the bows and the body armor and the commanders [were] behind all [the] house of Judah.
Kuyambira tsiku limenelo mpaka mʼtsogolo mwake, theka la antchito anga linkagwira ntchito, pamene theka linalo limatenga mikondo, zishango, mauta ndi kuvala malaya azitsulo. Akuluakulu ankalimbikitsa Ayuda onse
17 Who were rebuilding the wall and the [ones who] were carrying in burden [were] carrying [it] with [the] one hand his doing the work and one [hand] [was] holding the weapon.
amene ankamanga khoma. Anthu onyamula zinyalala aja ankagwira ntchito ndi dzanja limodzi, dzanja linali atanyamula chida chankhondo.
18 And the builders each one sword his [were] girded on hips his and [were] building and the [one who] gave a blast on the ram's horn [was] beside me.
Mʼmisiri aliyense ankamangirira lupanga lake mʼchiwuno mwake akamagwira ntchito. Koma munthu woyimba lipenga anali pambali panga nthawi zonse.
19 And I said to the nobles and to the officials and to [the] rest of the people the work [is] much and extensive and we [are] separate on the wall distant each from brother his.
Ndipo ine ndinati kwa anthu olemekezeka ndi anthu ena onse, “Ntchitoyi ndi yayikulu ndipo ili padera lalikulu ndipo ifeyo takhala motayanatayana kwambiri pa khoma.
20 In [the] place where you will hear [the] sound of the ram's horn there towards you will assemble to us God our he will fight for us.
Tsono kulikonse kumene muliko, mukamva kulira kwa lipenga bwerani mudzasonkhane kumene kuli ine kuno. Mulungu wathu adzatimenyera nkhondo.”
21 And we [were] doing the work and half of them [were] keeping hold on spears from when came up the dawn until came out the stars.
Choncho enafe tinapitiriza kugwira ntchito, pamene theka lina linkanyamula mikondo kuyambira mʼbandakucha mpaka nyenyezi zitaoneka.
22 Also at the time that I said to the people each one and servant his let them spend [the] night in [the] midst of Jerusalem and they will be for us the night a guard and the day work.
Pa nthawi imeneyo ndinawuzanso anthuwo kuti, “Aliyense pamodzi ndi wantchito wake agone mu Yerusalemu kuti tikhale ndi otilondera usiku ndi kuti masana tizigwira ntchito.”
23 And not I and brothers my and servants my and [the] men of the guard who [were] behind me not we [were] stripping off clothes our each one weapon his the water.
Choncho ine, anzanga, antchito anga, ndi anthu otiteteza amene ankanditsata panalibe ndi mmodzi yemwe anavula zovala zake pogona. Aliyense anasunga chida chake chankhondo pambali pake.

< Nehemiah 4 >