< 2 Samuel 21 >

1 During the time that David [ruled], there was a famine [in Israel] for three years. David prayed to Yahweh about it. And Yahweh said, “[In order for the famine to end], Saul’s family needs to be punished [MTY] because Saul killed many people from Gibeon [city].”
Pa nthawi ya ulamuliro wa Davide kunali njala kwa zaka zitatu zotsatana. Kotero Davide anapemphera kwa Yehova. Yehova anati, “Izi zachitika chifukwa chakuti Sauli ndi banja lake akanali ndi mlandu wakupha Agibiyoni.”
2 The people of Gibeon were not Israelis; they were a small group of the Amor people-group whom the Israelis had solemnly promised to protect. But Saul had tried to kill all of them because he (was very zealous/wanted very much) to enable the people of Judah and Israel [to be the only ones living in that land]. So the king summoned the leaders of Gibeon
Mfumu inayitanitsa Agibiyoni ndipo inayankhula nawo. (Tsono Agibiyoni sanali Aisraeli, koma otsala mwa Aamori. Aisraeli analumbira kuwasiya ndi moyo, koma Sauli chifukwa cha chikondi cha pa Israeli ndi Yuda, anafuna kuwawonongeratu).
3 and said to them, “What shall I do for you? How can I make amends/up for what was done to your people, in order that you will bless us who belong to Yahweh?”
Davide anafunsa Agibiyoni kuti, “Kodi ine ndikuchitireni chiyani? Ndipepese bwanji kuti inu mudalitse cholowa cha Yehova?”
4 They replied, “You cannot settle our quarrel with Saul and his family by giving us silver or gold. And we do not have the right to kill any Israelis.” So David asked, “Then/So what do you say that I should do for you?”
Agibiyoni anamuyankha kuti, “Ife tilibe ufulu woti nʼkulamula Sauli ndi banja lake kuti atipatse siliva kapena golide, tilibenso ufulu woti nʼkupha wina aliyense mu Israeli.” Davide anafunsa, “Mukufuna ine ndikuchitireni chiyani?”
5 They replied, “Saul [wanted to] get rid of us. He wanted to annihilate/kill all of us, in order that none of us would live anywhere in Israel.
Iwo anayankha mfumu kuti, “Tsono za munthu amene anatiwononga ndi kukonza chiwembu choti titheretu ndi kukhala wopanda malo mu Israeli,
6 Hand over to us seven of Saul’s descendants. We will hang them where Yahweh is worshiped in Gibeon, our town, the town where Saul, whom Yahweh previously chose to be king, lived.” The king replied, “Okay, I will hand them over to you.”
mutipatse adzukulu ake aamuna asanu ndi awiri kuti tiwaphe ndi kuwapereka pamaso pa Yehova ku Gibeya wa Sauli, wosankhidwa wa Yehova.” Choncho mfumu inati, “Ine ndidzakupatsani.”
7 The king did not hand over to them Saul’s grandson Mephibosheth, because of what he and [Mephibosheth’s father] Jonathan had solemnly promised to each other.
Koma mfumu inasunga Mefiboseti mwana wa Yonatani, mwana wa Sauli, chifukwa cha kulumbira kumene mfumu Davide ndi Yonatani mwana wa Sauli anachita pamaso pa Yehova.
8 Instead, he took Armoni and another man named Mephibosheth, the two sons that Saul’s slave wife Rizpah, the daughter of Aiah, had given birth to, and the five sons that Saul’s daughter Merab had given birth to. Merab’s husband was Adriel, the son of a man named Barzillai from Meholah [town].
Ndipo mfumu inatenga Arimoni ndi Mefiboseti, ana aamuna awiri a Rizipa, mwana wamkazi wa Ayiwa, amene anaberekera Sauli pamodzi ndi ana asanu a Merabi mwana wamkazi wa Sauli, amene anabereka Adirieli mwana wa Barizilai Mmeholati.
9 David handed those men over to the men from Gibeon. Then they hanged those seven men on a hill where they worshiped Yahweh. They were all killed during the time of the year that the people started to harvest the barley.
Iye anawapereka kwa anthu a ku Gibiyoni, amene anawapha nawayika pa phiri la Yehova. Onse asanu ndi awiri anafera limodzi. Iwo anaphedwa masiku oyamba kukolola barele.
10 Then Rizpah took coarse cloth made from goats’ hair, and spread it on the rock [where the corpses lay]. She stayed there from the time that people started to harvest the barley until the rains started. She did not allow any birds to come near the corpses during the day, and she did not allow any animals to come near during the night.
Rizipa mwana wamkazi wa Ayiwa anatenga chiguduli ndi kudziyalira pa mwala (pamene panali mitemboyo). Kuyambira nthawi yoyamba kukolola mpaka pamene mvula inayambanso kugwa, iye sanalole kuti mbalame zikhudze mitemboyo masana kapena nyama zakuthengo usiku.
11 When someone told David what Rizpah had done,
Davide atawuzidwa zimene Rizipa mwana wamkazi wa Ayiwa, mzikazi wa Sauli anachita,
12 he went with some of his servants to Jabesh in [the] Gilead [region] and got the bones of Saul and his son Jonathan. The people of Jabesh had stolen their bones from the (plaza/public square) in Beth-Shan [city], where the men from Philistia had hanged them previously, on the day that they had killed Saul and Jonathan on Gilboa [Mountain].
anapita kukatenga mafupa a Sauli ndi mwana wake Yonatani kwa anthu a ku Yabesi Giliyadi (iwo anawatenga mwamseri kuchoka pabwalo la ku Beti-Sani, kumene Afilisti anawapachika atapha Sauli ku Gilibowa).
13 David and his men took the bones of Saul and Jonathan, and they also took the bones of the seven men [from Gibeon] whom the men from Philistia had hanged.
Davide anakatenga mafupa a Sauli ndi mwana wake Yonatani kumeneko ndiponso mafupa otayidwa a amene anaphedwa nawasonkhanitsa pamodzi.
14 They buried the bones of Saul and Jonathan in Zela [town] in the land of [the tribe of] Benjamin. Doing all that the king commanded, they buried their bones in the tomb where Saul’s father Kish [was buried]. After that, [because] God [saw that Saul’s family had been punished to pay for Saul’s murder of many people from Gibeon, he] answered the Israelis’ prayers for their land, and caused the famine to end.
Iwo anayika mafupa a Sauli ndi mwana wake Yonatani mʼmanda a Kisi abambo ake a Sauli ku Zera mʼdziko la Benjamini, ndipo anachita zonse zimene mfumu inalamula. Atachita zimenezi, Mulungu anayankha pemphero lopempherera dzikolo.
15 The army of Philistia again started to fight against the army of Israel. And David and his soldiers went to fight the Philistines. During the battle, David became weary.
Nthawi inanso panali nkhondo pakati pa Afilisti ndi Aisraeli, Davide anapita ndi ankhondo ake kukamenyana ndi Afilisti ndipo iye anatopa kwambiri.
16 One of the Philistia men thought that he could kill David. His name was Ishbi-Benob. He was a descendant of [a group of] giants. He carried a bronze spear that weighed about (7-1/2 pounds/3-1/2 kg.), and he also had a new sword.
Ndipo Isibi-Benobi, mmodzi mwa zidzukulu za Rafa, amene mkondo wake unkalemera makilogalamu atatu ndi theka ndipo analinso ndi lupanga latsopano, anati adzapha Davide.
17 But Abishai came to help David, and attacked the giant and killed him. Then David’s soldiers forced him to promise that he would not go with them into a battle again. They said to him, “[If you die, and none of your descendants become king, that would be like] [MET] extinguishing the last light in Israel.”
Koma Abisai mwana wa Zeruya anabwera kudzapulumutsa Davide. Iye anamukantha Mfilisitiyo ndi kumupha. Pamenepo asilikali a Davide analumbira kwa iye kuti, “Inu simudzapita nafenso ku nkhondo, kuti nyale ya Israeli isadzazimitsidwe.”
18 Some time after that, there was a battle with the army of Philistia near Gob [village]. During the battle, Sibbecai, from [the] Hushah [clan], killed Saph, one of the descendants of the Rapha giants.
Patapita nthawi, panali nkhondo ina ndi Afilisti ku Gobu. Pa nthawi imeneyo Sibekai Mhusati anapha Safu, mmodzi mwa zidzukulu za Arefai.
19 [Later] there was another battle with the army of Philistia at Gob. During that battle, Elhanan, the son of Jaare-Oregim from Bethlehem, killed [the brother of] Goliath from Gath [city]; Goliath’s spear shaft/handle was (very thick, like the bar on a weaver’s loom/over two inches thick).
Pa nkhondo inanso ndi Afilisti ku Gobu, Elihanani mwana wa Yaare-Oregimu wa ku Betelehemu anapha Goliati Mgiti, amene anali ndi mkondo ngati ndodo yowombera nsalu.
20 Later there was another battle near Gath. There was a (huge man/giant) there who liked to fight [in battles]. He had six fingers on each hand and six toes on each foot. He was descended from [the] Rapha [giants].
Pa nkhondo inanso imene inachitika ku Gati panali munthu wina wamtali kwambiri wa zala zisanu ndi chimodzi mʼmanja ndi mʼmapazi ndipo zonse pamodzi zinalipo 24. Iyenso anali chidzukulu cha Rafa.
21 But when he (made fun of/ridiculed) the men in the Israeli [army], Jonathan, the son of David’s [older] brother Shimeah, killed him.
Pamene iye ankanyoza Aisraeli, Yonatani mwana wa Simea, mʼbale wake wa Davide anamupha.
22 Those four men were some of the descendants of the Rapha giants who had lived in Gath, who were killed [MTY] by David and his soldiers.
Anthu anayi amenewa anali zidzukulu za Rafa ku Gati, ndipo onse anaphedwa ndi Davide ndi ankhondo ake.

< 2 Samuel 21 >