< Ezekiel 4 >

1 [Yahweh also said to me, ] “You human, take a large clay tablet/brick and put it in front of you. Then on the [engrave/draw] on it lines that represent Jerusalem.
Mulungu anati, “Iwe mwana wa munthu, tsopano tenga njerwa, uliyike pamaso pako ndipo ujambulepo chithunzi cha mzinda wa Yerusalemu.
2 [draw figures around it to represent enemy soldiers who will] surround the city. Make mounds around it and a dirt ramp up against the [around the city]. [figures around it that represent] (battering rams/heavy logs that will break though the walls).
Ndipo uwuzinge mzindawo motere: uwumangire nsanja zowuzinga, uwumbire mitumbira ya nkhondo, uwumangire misasa ya nkhondo ndipo uyike zida zogumulira kuzungulira mzindawo.
3 Then take an iron pan, and place it [to be] like an iron wall between you [the drawing of] the city. Then turn your face toward the drawing. It will symbolize [enemy troops will] surround the city to attack it. That will be a warning to the Israeli people [MTY].
Kenaka utenge chiwaya chachitsulo uchiyike ngati khoma lachitsulo pakati pa iwe ndi mzindawo. Uyangʼanitsitse mzindawo ndipo udzakhala wozingidwa ndi nsanja za nkhondo. Choncho umangire nsanja zankhondo. Chimenechi chidzakhala chizindikiro kwa Aisraeli.
4 Then lie on your left side, and stay like that for 390 days. That [symbolize that the Israeli people will be punished for] their sins; you must lie like that one day for each year during which they will be punished.
“Tsono iwe ugonere kumanzere kwako ndipo ndidzayika pa iwe tchimo la Aisraeli. Iwe udzasenza tchimolo masiku onse amene udzagonere mbali imeneyo.
5
Ine ndakuyikira masiku okwana 390 malingana ndi zaka za machimo awo. Umu ndi mmene udzasenzere machimo a Aisraeli.
6 After that, lie down again. This time, lie on your right side for 40 days. That [symbolize that the Israeli people will be punished more] for their sins, one day for each [during which they will be punished].
“Utatha zimenezo udzagonerenso mbali ya kudzanja lamanja, ndipo udzasenza machimo a anthu a ku Yuda masiku makumi anayi, tsiku lililonse kuyimira chaka chimodzi.
7 Turn your face [the drawing of] Jerusalem and bare your [like a soldier does who prepares to go into a battle] [MTY], and prophesy [what will happen to] the city.
Tsono udzayangʼanitsitse nsanja za nkhondo zozinga. Dzanja la mkanjo wako utalikwinya ndi dzanja lako utakweza, udzalosere modzudzula Yerusalemu.
8 [You will not be able to move; it will be as though] I have tied you with ropes in order that you cannot turn from one side to the other until you have [symbolizing how many years the city] will be (besieged/surrounded by enemy soldiers).
Ine ndidzakumanga ndi zingwe kotero kuti sudzatha kutembenukira uku ndi uku mpaka utatsiriza masiku akuzingidwa ako.
9 [Before you do that, ] take some wheat and barley, beans, lentils, spelt and millet, and put them in a [storage] jar, and use that to bake [for yourself]. That is what you will eat during the 390 days while you lie on your [left] side.
“Tsono tenga tirigu ndi barele, nyemba ndi mphodza, mapira ndi mchewere; ndipo uyike zonsezi mʼmbale imodzi ndipo upange buledi wako. Uzidya pa masiku 390 amene udzakhala ukugonera mbali imodzi.
10 You will eat (8 ounces/a small loaf) of bread each day.
Uyeze theka la kilogalamu la chakudyacho kuti uzidya tsiku lililonse kamodzi kokha.
11 [Also] measure out (1.5 pints/0.6 liter) of water to drink each day.
Uyezenso zikho ziwiri zamadzi ndipo uzimwa tsiku ndi tsiku.
12 Eat that bread like you would eat a loaf of barley bread. But use your own dried dung for fuel to bake the bread while people are watching.
Uzidya chakudya chako ngati momwe amadyera keke ya barele. Uzidzaphika chakudyacho anthu akuona pogwiritsa ntchito ndowe ya munthu ngati nkhuni.”
13 That will symbolize that the Israeli people will be forced to eat food that is unacceptable to me when they are living in the nations to which I will force them to go.”
Yehova anati, “Chimodzimodzi anthu a Israeli adzadya chakudya chodetsedwa ku mayiko achilendo kumene Ine ndidzawapirikitsira.”
14 Then I said, “No, Yahweh God![Do not force me to do that]! I have never caused myself to become unacceptable to you [by doing anything like that]. From the time when I was young, I have never eaten meat of any [animal] that was found dead or that had been killed by wild animals. And I have never eaten any meat that is unacceptable to you.”
Koma ine ndinati, “Zisatero, Ambuye Yehova! Ine sindinadziyipitsepo pa zachipembedzo. Kuyambira ubwana wanga mpaka tsopano, sindinadyepo kanthu kalikonse kopezeka katafa kapena kophedwa ndi zirombo za kutchire. Palibe nyama yodetsedwa pa zachipembedzo imene inalowa pakamwa panga.”
15 Yahweh replied, “Okay, I will allow you to bake your bread using dried cow manure instead of human [for fuel].”
Iye anati, “Chabwino, ndidzakulola kuti uphike buledi wako ndi ndowe za ngʼombe mʼmalo mwa ndowe za munthu.”
16 Then he said to me, “You human, I will cause the supply of food to Jerusalem to be cut off. [Then] the people will eat the small amounts of food and drink the small amounts of [that the government permits them to have], and they will be [very] distressed and anxious as they do that,
Pambuyo pake anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, anthu a ku Yerusalemu ndidzawachepetsera chakudya. Anthuwo adzadya chakudya chochita kuyeza ndipo azidzadya mwa nkhawa. Azidzamwanso madzi ochita kuyeza ndiponso mwa mantha.
17 because water and food will be very scarce. They will see each other becoming extremely thin, and they will be appalled; [but this will happen] because they are being punished [for the sins that they have committed].”
Ndidzachita zimenezi kuti adzasowe chakudya ndi madzi. Choncho adzachita nkhawa akumapenyana ndipo adzatheratu ndi kuwonda chifukwa cha machimo awo.”

< Ezekiel 4 >