< Nahum 1 >

1 [I am] Nahum, from Elkosh [village]. [This is] a message about Nineveh [city, the capital of Assyria that was given] to me in a vision [by Yahweh].
Uthenga wonena za Ninive. Buku la masomphenya a Nahumu wa ku Elikosi.
2 Yahweh our God (is jealous/does not want people to worship any other god). He is very angry [with those who worship other gods], and he gets revenge [DOU] [on all] those who oppose him [DOU].
Yehova ndi Mulungu wansanje ndiponso wobwezera; Yehova amabwezera ndipo ndi waukali. Yehova amabwezera adani ake ndipo ukali wake umakhala nthawi zonse pa adani akewo.
3 Yahweh does not quickly become angry; but he is very powerful, and he will certainly punish [LIT] those who have done evil things [MTY]. He shows his power by sending whirlwinds and storms, and clouds are [like] [MET] the dust [stirred up by] his feet.
Yehova sakwiya msanga koma ndi wa mphamvu yayikulu; ndipo sadzalola kuti munthu wolakwa asalangidwe. Iye amayenda mʼkamvuluvulu ndi mʼnamondwe, ndipo mitambo ndi fumbi la ku mapazi ake.
4 When he commands oceans and rivers to become dry, they dry up. [He causes the grass in the fields in] the Bashan [region] and [on the slopes of] Carmel [Mountain] to wither, [and causes] the flowers in Lebanon to fade.
Amalamulira nyanja ndipo imawuma; amawumitsa mitsinje yonse. Zomera za ku Basani ndi Karimeli zimawuma ndipo maluwa a ku Lebanoni amafota.
5 When he appears, [it is as though] the mountains shake and the hills melt; the earth quakes and [the people on] the earth tremble.
Mapiri amagwedera pamaso pake ndipo zitunda zimasungunuka. Dziko lapansi limanjenjemera pamaso pake, dziko lonse ndi zonse zokhala mʼmenemo.
6 There is no one [RHQ] who can resist him when he becomes extremely angry; there is no one [RHQ] who can survive when his anger is very hot. When he is very angry, [it is as though] his anger is like [SIM] a blazing fire, and [it is as though] mountains are shattered into pieces.
Ndani angathe kuyima pamaso pake Iye akalusa? Ndani angapirire mkwiyo wake woopsa? Ukali wake ukuyaka ngati moto; matanthwe akunyeka pamaso pake.
7 But he is good; he protects [us his people] when we experience troubles. He takes care of those who trust in him.
Yehova ndi wabwino, ndiye kothawirako nthawi ya masautso. Amasamalira amene amamudalira,
8 But he will get rid of his enemies; he will be to them [like] [MET] a flood that destroys everything. He will chase his enemies into the darkness [of the place where the dead are].
koma ndi madzi achigumula choopsa Iye adzawononga adani ake (Ninive); adzapirikitsira adani ake ku malo a mdima.
9 [So], it is useless [RHQ] for you [people of Nineveh] to plot against Yahweh. He will not [need to] strike you two times to destroy you; he will destroy you [by striking you only once].
Chiwembu chilichonse chimene akukonzekera kumuchitira Yehova adzachiwononga kotheratu; msautso sudzabweranso kachiwiri.
10 [It will be as though his enemies] are tangled in thorns, and they will stagger like people who have drunk a lot of wine. They will be burned up like [SIM] a fire completely burns up stubble/straw.
Iwo adzakodwa mu ziyangoyango za minga ndipo adzaledzera ndi vinyo wawo; adzatenthedwa ngati ziputu zowuma.
11 In Nineveh [city] there was a man who advised people to do very wicked things to Yahweh.
Kwa iwe, Ninive, kunachokera munthu wa cholinga choyipa, wofuna kuchitira Yehova chiwembu, amene amapereka uphungu woyipa.
12 But this is what Yahweh says [about you Israeli people]: “Although the people of Assyria have very many people and their army is very powerful, they will be destroyed and will disappear. [I say to my people in Judah, ] ‘have [already] punished you, but I will not punish you again.
Yehova akuti, “Ngakhale Asiriyawo ali ndi abwenzi, kaya iwowo ndi ambiri, koma adzawonongedwa ndi kutheratu. Ngakhale ndinakuzunza iwe Yuda, sindidzakuzunzanso.
13 Now I will cause the [people of Assyria] to no longer control/oppress you [MET]; [it will be as though] I will tear off the shackles/chains on your [hands and feet].”
Tsopano ndidzathyola goli lake pa khosi lako ndipo ndidzadula maunyolo ako.”
14 [And this is what] Yahweh also declares about you people of Nineveh: “You will not have any descendants who will continue to have your family names. And I will destroy all the statues of your gods that were carved or formed in molds. I will cause you [to be killed and] sent to your graves, because you are vile/despicable!”
Yehova walamulira za iwe, Ninive kuti, “Sudzakhala ndi zidzukulu zimene zidzadziwike ndi dzina lako. Ndidzawononga zifanizo zosema ndi mafano owumba amene ali mʼnyumba ya milungu yako. Ine ndidzakukumbira manda chifukwa ndiwe woyipitsitsa.”
15 [You people of Judah, ] look! A messenger will be coming across the mountains, and he [SYN] will be bringing good news [to you]. He will be declaring [that you will now have] peace [because Assyria will have been conquered]. [So, ] celebrate your festivals, and do what you solemnly promised to do [when your enemies were threatening to attack you], because your wicked [enemies] will not invade your country again, [because] they will be completely destroyed.
Taonani, pa phiripo, mapazi a munthu amene akubweretsa nkhani yabwino, amene akulengeza za mtendere! Inu anthu a ku Yuda, chitani madyerero anu ndipo kwaniritsani malumbiro anu. Anthu oyipa sadzakuthiraninso nkhondo; iwo adzawonongedwa kotheratu.

< Nahum 1 >