< Proverbs 16 >

1 People plan what they want to do, but Yahweh is the one who decides [MTY] what really will happen.
Zolinga za mu mtima ndi za munthu, koma kwa Yehova ndiye kumachokera yankho.
2 People may think that their actions are right, but Yahweh really knows why people do what they do.
Zochita zonse za munthu zimaoneka zabwino pamaso pake, koma Yehova ndiye amasanthula zolinga zako.
3 (Request/Rely on) Yahweh to direct what you plan to do; [if you do that], you will succeed in what you plan.
Pereka ntchito zako zonse mʼmanja mwa Yehova, ndipo zolinga zako zidzachitikadi.
4 Yahweh knows why he does everything that he does; he has even prepared the wicked for the time that he will punish them.
Yehova amachita zonse ndi cholinga chake, ngakhale anthu oyipa kuti aone tsiku latsoka.
5 Yahweh hates/detests everyone who is proud [IDM]; you can be certain [IDM] that they will be punished [LIT].
Munthu aliyense wodzikuza amamunyansa Yehova. Koma dziwani izi: Iwo sadzakhala osalangidwa.
6 Be loyal to Yahweh and faithfully [obey] him; if you do that, he will forgive you for having sinned. If we revere him, nothing evil will happen to us (OR, he will prevent evil things from happening to us).
Chifukwa cha chikondi chosasinthika ndi kukhulupirika, munthu amakhululukidwa machimo ake; chifukwa cha kuopa Yehova munthu amapewa zoyipa.
7 When our behavior pleases Yahweh, he even causes our enemies to act peacefully toward us.
Pamene makhalidwe a munthu akondweretsa Yehova, ngakhale adani ake amakhala naye mwa mtendere.
8 It is better to have a small amount of money that is earned honestly than to have a lot of money that is acquired dishonestly.
Kuli bwino kukhala ndi zinthu pangʼono zozipeza mwachilungamo, kusiyana ndi kukhala ndi zinthu zambiri zozipeza popanda chilungamo.
9 People plan what they want to do, but Yahweh directs/determines what they will [really] be able to do.
Mtima wa munthu umalingalira zochita, koma Yehova ndiye amakhazikitsa njira zake.
10 [If] God directs what a king says, what he decides is [always] right/fair.
Mawu a mfumu ali ngati mawu ochokera kwa Mulungu; ndipo pakamwa pake sipalakwa poweruza mlandu.
11 Yahweh wants us to use scales that are correct; the weights in his bag are correct, [because] he made them.
Miyeso ndi masikelo achilungamo zimachokera kwa Yehova; miyala yonse yoyesera ya mʼthumba anayipanga ndi Yehova.
12 Kings detest those who do evil, because [it is people doing what] is fair/right that causes their governments to be [MTY] strong.
Kuchita zoyipa kumanyansa mafumu, pakuti chilungamo ndiye maziko a ufumu wake.
13 Kings are delighted to hear people say [MTY] what is true; they love those who say what is right/honest.
Mawu owona amakondweretsa mfumu. Iyo imakonda munthu woyankhula choonadi.
14 If a king becomes angry, he [may] command that someone be executed, [so] wise people will [try to] cause him to be calm.
Ukali wa mfumu ndi mthenga wa imfa, koma munthu wanzeru amawupepesa ukaliwo.
15 If a king has a smile [MTY] on his face, he will enable people to have a [long] life (OR, he will not order people to be executed); his being pleased [with people] is [as delightful] as rain in the springtime [when seeds are planted].
Kuwala kwa nkhope ya mfumu kumapatsa moyo; ndipo kukoma mtima kwake kuli ngati mitambo ya mvula nthawi ya chilimwe.
16 Becoming wise is better than aquiring gold; getting good understanding/insight is better than acquiring silver.
Nʼkwabwino kwambiri kupeza nzeru kupambana golide. Kukhala womvetsa bwino zinthu nʼkwabwino kupambana ndi kukhala ndi siliva.
17 Those whose behavior [MET] is good/right turn away from doing evil; those who guard their conduct [MTY] protect their lives.
Msewu wa munthu wowongoka mtima umapewa zoyipa; wopenyetsetsa kumene akupita amasunga moyo wake.
18 Being proud will (lead to your having/cause you to have) disasters; despising others will result in your being ruined.
Kunyada kumafikitsa ku chiwonongeko, ndipo munthu wodzikuza adzagwa.
19 It is better to be humble and poor than [to associate with] proud [people] and [to become rich by] dividing with them (plunder/goods captured in a battle).
Nʼkwabwino kukhala ndi mtima wodzichepetsa pakati pa anthu oponderezedwa, kusiyana ndi kugawana zolanda ndi anthu onyada.
20 Those who heed good teaching/instruction will prosper; happy are those who trust in Yahweh.
Munthu womvera malangizo zinthu zimamuyendera bwino, ndipo wodala ndi amene amadalira Yehova.
21 People say that those who are wise learn what is right/good behavior, and those who talk pleasantly [are able to] influence others [to do what is right].
A mtima wanzeru amatchedwa ozindikira zinthu, ndipo mawu ake okoma amawonjezera nzeru.
22 Being wise is [like having] a fountain that gives life [MET], but foolish people are punished as a result of their acting foolishly.
Kumvetsa zinthu ndi kasupe wa moyo kwa iwo amene ali nako, koma uchitsiru umabweretsa chilango kwa zitsiru.
23 Those who are wise think carefully before they talk, and as a result they are able to influence/persuade others [to do what is right].
Mtima wanzeru umathandiza munthu kuyankhula mwa nzeru, ndipo mawu ake amawonjezera nzeru.
24 Kind words are like honey [SIM]: We enjoy them both, and both cause our bodies to be healthy/strong.
Mawu okometsera ali ngati chisa cha njuchi, amakoma mu mtima ndipo amalimbitsa thupi.
25 There are some kinds of behavior [MET] that people think are right, but (walking on those roads [MET]/continually doing those things) causes those people to die.
Pali njira ina yooneka ngati yowongoka kwa munthu koma kumatsiriziro kwake ndi imfa.
26 If a worker (has an appetite/is hungry), that urges him to work hard because he [SYN] wants to [earn money to buy things to] eat.
Njala ya munthu wantchito imamuthandiza kulimbikira; njalayo imamukakamiza kuchitapo kanthu.
27 Worthless people plan [ways to cause] trouble [for others], and [even] what they say [injures people] like a hot fire does [SIM].
Munthu wopanda pake amakonzekera kuchita zoyipa ndipo mawu ake ali ngati moto wopsereza.
28 Deceitful people cause strife/quarreling among other people; those who say false things about other people cause people who are friends to become enemies.
Munthu woyipa mtima amayambitsa mikangano, ndipo miseche imalekanitsa anthu okondana kwambiri.
29 Those who act violently entice/encourage others [to also act violently] and lead them along a road that will end in disaster.
Munthu wandewu amakopa mnansi wake, ndipo amamuyendetsa njira imene si yabwino.
30 People [sometimes] show with [one of] their eyes [to signal to their friends that they are] planning to do something to harm [others]; they smirk when they are about to do something evil.
Amene amatsinzinira maso ake amalingalira zinthu zokhota; amene amachita msunamo amakonzeka kuchita zoyipa.
31 Gray hair is [like] a glorious crown [MET] that is given to people who have always behaved righteously.
Imvi zili ngati chipewa chaufumu chaulemerero; munthu amazipeza akakhala moyo wolungama.
32 Those who do not become angry quickly are better than those who are powerful; it is better to (control your temper/keep yourself from becoming very angry) than to conquer a city.
Munthu wosapsa mtima msanga amaposa munthu wankhondo, munthu wowugwira mtima wake amaposa amene amalanda mzinda.
33 People (cast lots/throw marked stones) [to decide what should be done], but God is the one who truly decides what will happen.
Maere amaponyedwa pa mfunga, koma ndiye Yehova amene amalongosola zonse.

< Proverbs 16 >